1 Chikondi cha pa abale chikhalebe.
2 Musaiwale kuchereza alendo; pakuti mwa ichi ena anacherezaangeloosachidziwa.
3 Kumbukirani am’nsinga, monga am’nsinga anzao; ochitidwa zoipa, monga ngati inunso adatero nanu m’thupi.
4 Ukwati uchitidwe ulemu ndi onse, ndi pogona pakhale posadetsedwa; pakuti adama ndi achigololo adzawaweruza Mulungu.
5 Mtima wanu ukhale wosakonda chuma; zimene muli nazo zikukwanireni; pakuti Iye anati, Sindidzakusiya konse, kungakhale kukutaya, sindidzakutaya ndithu.
6 Kotero kuti tinena molimbika mtima,
Mthandizi wanga ndiye Ambuye; sindidzaopa;
adzandichitira chiyani munthu?
7 Kumbukirani atsogoleri anu, amene analankhula nanu Mau a Mulungu; ndipo poyang’anira chitsiriziro cha mayendedwe ao mutsanze chikhulupiriro chao.
8 YesuKhristuali yemweyo dzulo, ndi lero, ndi kunthawi zonse.
9 Musatengedwe ndi maphunzitso a mitundumitundu, ndi achilendo; pakuti nkokoma kuti mtima ukhazikike ndi chisomo; kosati ndi zakudya, zimene iwo adazitsata sanapindule nazo.
10 Tili nalo guwa la nsembe, limene iwo akutumikira chihema alibe ulamuliro wa kudyako.
11 Pakuti matupi a nyama zija, mwazi wa izo umatengedwa, ndi mkulu wa ansembe kulowa m’malo opatulidwa, chifukwa cha zoipa, amatenthedwa kunja kwa tsasa.
12 Mwa ichi Yesunso, kuti akayeretse anthuwo mwa mwazi wa Iye yekha, adamva chowawa kunja kwa chipata.
13 Chifukwa chake titulukire kwa Iye kunja kwa tsasa osenza tonzo lake.
14 Pakuti pano tilibe mzinda wokhalitsa, komatu tifunafuna ulinkudzawo.
15 Potero mwa Iye tipereke chiperekere nsembe yakuyamika Mulungu, ndiyo chipatso cha milomo yovomereza dzina lake.
16 Koma musaiwale kuchitira chokoma ndi kugawira ena; pakuti nsembe zotere Mulungu akondwera nazo.
17 Mverani atsogoleri anu, nimuwagonjere; pakuti alindirira moyo wanu, monga akuwerengera; kuti akachite ndi chimwemwe, osati mwachisoni: pakuti ichi sichikupindulitsani inu.
18 Mutipempherere ife; pakuti takopeka mtima kuti tili nacho chikumbumtima chokoma m’zonse, pofuna kukhala nao makhalidwe abwino.
19 Ndipo ndikudandaulirani koposa kuchita ichi, kuti kubwera kwanga kwa inu kufulumidwe.
20 Koma Mulungu wa mtendere amene anabwera naye wotuluka mwa akufa Mbusa wamkulu wa nkhosa ndi mwazi wachipanganochosatha, ndiye Ambuye wathu Yesu,
21 akuyeseni inu opanda chilema m’chinthu chilichonse chabwino, kuti muchite chifuniro chake; ndi kuchita mwa ife chomkondweretsa pamaso pake, mwa Yesu Khristu; kwa Iyeyu ukhale ulemerero kunthawi za nthawi.Amen.
22 Koma ndidandaulira inu, abale, lolani mau a chidandauliro; pakutinso ndalembera inu mwachidule.
23 Zindikirani kuti mbale wathu Timoteo wamasulidwa; pamodzi ndi iye, ngati akudza msanga, ndidzakuonani inu.
24 Perekani moni kwa atsogoleri anu onse, ndi oyera mtima onse. Akupatsani moni iwo a ku Italiya.
25 Chisomo chikhale ndi inu nonse, Amen.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/HEB/13-6c22d691f3869cf94b3e09168362e92f.mp3?version_id=1068—