Categories
CHIVUMBULUTSO

CHIVUMBULUTSO 20

Satana womangidwa zaka chikwi

1 Ndipo ndinaonamngeloanatsika Kumwamba, nakhala nacho chifungulo cha ku chiphompho chakuya, ndi unyolo waukulu m’dzanja lake.

2 Ndipo anagwira chinjoka, njoka yakaleyo, ndiye mdierekezi ndiSatana, nammanga iye zaka chikwi,

3 namponya ku chiphompho chakuya, natsekapo, nasindikizapo chizindikiro pamwamba pake, kuti asanyengensoamitundukufikira kudzatha zaka chikwi; patsogolo pake ayenera kumasulidwa iye kanthawi.

4 Ndipo ndinaona mipando yachifumu, ndipo anakhala pamenepo; ndipo anawapatsa chiweruziro; ndipo ndinaona mizimu ya iwo amene adawadula khosi chifukwa cha umboni wa Yesu, ndi chifukwa cha mau a Mulungu, ndi iwo amene sanalambire chilombo, kapena fano lake, nisanalandire lembalo pamphumi ndi padzanja lao; ndipo anakhala ndi moyo, nachita ufumu pamodzi ndiKhristuzaka chikwi.

5 Otsala a akufa sanakhalenso ndi moyo kufikira kudzatha zaka chikwi. Ndiko kuuka kwa akufa koyamba.

6 Wodala ndi woyera mtima ali iye amene achita nao pa kuuka koyamba; pa iwowa imfa yachiwiri ilibe ulamuliro; komatu adzakhala ansembe a Mulungu ndi a Khristu, nadzachita ufumu pamodzi ndi Iye zaka chikwizo.

Satana amasulidwa naonongeka

7 Ndipo pamene zidzatha zaka chikwi, adzamasulidwa Satana m’ndende yake;

8 nadzatuluka kudzasokeretsa amitundu ali mungodya zinai za dziko,Gogi, ndi Magogi, kudzawasonkhanitsa achite nkhondo: chiwerengero chao cha iwo amene chikhala ngati mchenga wa kunyanja.

9 Ndipo anakwera nafalikira m’dziko, nazinga tsasa la oyera mtima ndi mzinda wokondedwawo: ndipo unatsika moto wakumwamba nuwanyeketsa.

10 Ndipo mdierekezi wakuwasokeretsa anaponyedwa m’nyanja ya moto ndisulufure, kumeneko kulinso chilombocho ndi mneneri wonyengayo; ndipo adzazunzidwa usana ndi usiku kunthawi za nthawi.

Chiweruziro chotsiriza

11 Ndipo ndinaona, mpando wachifumu waukulu woyera, ndi Iye wakukhalapo, amene dziko ndi m’mwamba zinathawa pamaso pake, ndipo sanapezedwe malo ao.

12 Ndipo ndinaona akufa, aakulu ndi aang’ono alinkuima kumpando wachifumu; ndipo mabuku anatsegulidwa; ndipo buku lina linatsegulidwa, ndilo la moyo; ndipo akufa anaweruzidwa mwa zolembedwa m’mabuku, monga mwa ntchito zao.

13 Ndipo nyanja inapereka akufawo anali momwemo, ndipo imfa ndi dziko la akufa zinapereka akufawo anali m’menemo; ndipo anaweruzidwa yense monga mwa ntchito zake.

14 Ndipo imfa ndi dziko la akufa zinaponyedwa m’nyanja yamoto. Iyo ndiyo imfa yachiwiri, ndiyo nyanja yamoto.

15 Ndipo ngati munthu sanapezedwe wolembedwa m’buku la moyo, anaponyedwa m’nyanja yamoto.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/REV/20-d2dbb3211f1a325187873729fa126e49.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *