Categories
MASALIMO

MASALIMO 14

Anthu oipadi

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Wauchitsiru amati mumtima mwake, Kulibe Mulungu.

Achita zovunda, achita ntchito zonyansa;

kulibe wakuchita bwino.

2 Yehova mu Mwamba anaweramira pa ana a anthu,

kuti aone ngati aliko wanzeru,

wakufuna Mulungu.

3 Anapatuka onse; pamodzi anavunda mtima;

palibe wakuchita bwino ndi mmodzi yense.

4 Kodi onse ochita zopanda pake sadziwa kanthu?

Pakudya anthu anga monga akudya mkate,

ndipo saitana pa Yehova.

5 Pamenepa anaopaopatu,

pakuti Mulungu ali mu mbadwo wa wolungama.

6 Munyazitsa uphungu wa wozunzika,

koma Yehova ndiye pothawira pake.

7 Mwenzi chipulumutso cha Israele chitachokera kuZiyoni!

Pakubweretsa Yehova anthu ake a m’nsinga,

pamenepo adzakondwera Yakobo, nadzasekera Israele.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/14-077b876ad14e0f22bfb7d2de2c9b5075.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 15

Chikhalidwe cha munthu woona wa Mulungu

Salimo la Davide.

1 Yehova, ndani adzagonera m’chihema mwanu?

Adzagonera ndani m’phiri lanu lopatulika?

2 Iye wakuyendayo mokwanira, nachita chilungamo,

nanena zoonadi mumtima mwake.

3 Amene sasinjirira ndi lilime lake,

nachitira mnzake choipa,

ndipo satola miseche pa mnansi wake.

4 M’maso mwake munthu woonongeka anyozeka;

koma awachitira ulemu akuopa Yehova.

Atalumbira kwa tsoka lake, sasintha ai.

5 Ndalama zake sakongoletsa mofuna phindu lalikulu,

ndipo salandira chokometsera mlandu kutsutsa wosachimwa.

Munthu wakuchita izi sadzagwedezeka kunthawi zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/15-b5acfb14ce5ab7bfc019521093f17172.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 16

Munthu wokhulupirira Mulungu akhazikika mtima, osaopa kutayika

Mikitamu wa Davide.

1 Ndisungeni ine, Mulungu: pakuti ndakhulupirira Inu.

2 Ndinati kwa Yehova, Inu ndinu Ambuye wanga,

ndilibe chabwino china choposa Inu.

3 Za oyera mtima okhala padziko lapansi,

iwo ndiwo omveka mbiri,

mwa iwowo muli chikondwero changa chonse.

4 Zidzachuluka zisoni zao za iwo otsata Mulungu wina.

Sindidzathira nsembe zao zamwazi,

ndipo sindidzatchula maina ao pakamwa panga.

5 Yehova ndiye gawo la cholowa changa ndi chikho changa,

ndinu wondigwirira cholandira changa.

6 Zingwe zandigwera mondikondweretsa;

inde cholowa chokoma ndili nacho.

7 Ndidzadalitsa Yehova, amene anandichitira uphungu,

usikunso impso zanga zindilangiza.

8 Ndaika Yehova patsogolo panga nthawi zonse;

popeza ali padzanja langa lamanja, sindidzagwedezeka.

9 Chifukwa chake wasekera mtima wanga,

nukondwera ulemu wanga;

mnofu wanganso udzakhala mokhazikika.

10 Pakuti simudzasiya moyo wanga kumanda;

simudzalola wokondedwa wanu avunde.

11 Mudzandidziwitsa njira ya moyo,

pankhope panu pali chimwemwe chokwanira;

m’dzanja lanu lamanja muli zokondweretsa zomka muyaya.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/16-f9ecd68e0862fca5c3c92330c486c3b5.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 17

Davide apempha Mulungu amsunge pa ofuna kumuononga

Pemphero la Davide.

1 Yehova, imvani chilungamo, mverani mfuu wanga;

tcherani khutu ku pemphero langa

losatuluka m’milomo ya chinyengo.

2 Pankhope panu patuluke chiweruzo changa;

maso anu apenyerere zolunjika.

3 Mwayesera mtima wanga; mwandizonda usiku;

mwandisuntha, simupeza kanthu;

mwatsimikiza mtima kuti m’kamwa mwanga simudzalakwa.

4 Za machitidwe a anthu, ndachenjera ndi mau a milomo yanu

ndingalowe njira za woononga.

5 M’mayendedwe anga ndasunga mabande anu,

mapazi anga sanaterereke.

6 Ine ndinakuitanani, pakuti mudzandiyankha, Mulungu;

tcherani khutu lanu kwa ine, imvani mau anga.

7 Onetsani chifundo chanu chodabwitsa,

Inu wakupulumutsa okhulupirira Inu

kwa iwo akuwaukira ndi dzanja lanu lamanja.

8 Ndisungeni monga kamwana ka m’diso,

ndifungatireni mu mthunzi wa mapiko anu,

9 kundilanditsa kwa oipa amene andipasula,

adani a pa moyo wanga amene andizinga.

10 Mafuta ao awatsekereza;

m’kamwa mwao alankhula modzikuza.

11 Tsopano anatizinga m’mayendedwe athu,

apenyetsetsa m’maso kuti atigwetse pansi.

12 Afanana ndi mkango wofuna kumwetula,

ndi msona wa mkango wakukhala mobisalamo.

13 Ukani Yehova, Mumtsekereze, mumgwetse,

landitsani moyo wanga kwa woipa ndi lupanga lanu;

14 kwa anthu, ndi dzanja lanu, Yehova,

kwa anthu a dziko lapansi pano

amene cholowa chao chili m’moyo uno,

ndipo mimba yao muidzaza ndi chuma chanu chobisika;

akhuta mtima ndi ana,

nasiyira ana amakanda zochuluka zao.

15 Koma ine ndidzapenyerera nkhope yanu m’chilungamo,

ndidzakhuta mtima ndi maonekedwe anu, pamene ndidzauka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/17-9d8ddf7ef741f74133cbdf9abe033de3.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 18

Nyimbo yoyamikira Yehova ya Davide

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide, mtumiki wa Yehova, amene ananena kwa Yehova mau a nyimbo iyi m’mene Yehova anamlanditsa m’dzanja la adani ake onse, ndi m’dzanja la Saulo: ndipo anati,

1 Ndikukondani, Yehova, mphamvu yanga.

2 Yehova ndiye thanthwe langa, ndi linga langa,

ndi Mpulumutsi wanga;

Mulungu wanga, ngaka yanga, ndidzakhulupirira Iye;

chikopa changa, nyanga ya chipulumutso changa, msanje wanga.

3 Ndidzaitanira Yehova, woyenera kutamandika,

ndipo adzandipulumutsa ine kwa adani anga.

4 Zingwe za imfa zinandizinga,

ndipo mitsinje ya zopanda pake inandiopsa.

5 Zingwe za manda zindizinga,

misampha ya imfa inandifikira ine.

6 M’kusauka kwanga ndinaitana Yehova,

ndipo ndinakuwira Mulungu wanga;

mau anga anawamva mu Kachisi mwake,

ndipo mkuwo wanga wa pankhope pake unalowa m’makutu mwake.

7 Pamenepo linagwedezeka, ndi kutenthemera dziko lapansi,

ndi maziko a mapiri ananjenjemera

nagwedezeka, pakuti anakwiya Iyeyo.

8 Unakwera utsi wotuluka m’mphuno mwake,

ndi moto wa m’kamwa mwake unanyeka

nuyakitsa makala.

9 Ndipo Iye anaweramitsa thambo, natsika;

ndipo pansi pa mapazi ake panali mdima bii.

10 Ndipo anaberekeka pakerubi, nauluka;

nauluka msanga pa mapiko a mphepo.

11 Anaika mdima pobisala pake, hema wake womzinga;

mdima wa madzi, makongwa a kuthambo.

12 Mwa kuchezemira kunali pamaso pake makongwa anakanganuka,

matalala ndi makala amoto.

13 Ndipo anagunda m’mwamba Yehova,

ndipo Wam’mwambamwamba anamvetsa liu lake;

matalala ndi makala amoto.

14 Ndipo anatuma mivi yake nawabalalitsa;

inde mphezi zaunyinji, nawamwaza.

15 Ndipo zidaoneka zoyendamo madzi,

nafukuka maziko a dziko lapansi,

mwa kudzudzula kwanu, Yehova,

mwa mpumo wa mpweya wa m’mphuno mwanu.

16 Anatuma kuchokera m’mwamba, ananditenga;

anandivuula m’madzi ambiri.

17 Anandipulumutsa ine kwa mdani wanga wamphamvu,

ndi kwa iwo ondida ine, pakuti anandiposa mphamvu.

18 Anandipeza ine tsiku la tsoka langa;

koma Yehova anali mchirikizo wanga.

19 Ananditulutsanso andifikitse motakasuka;

anandilanditsa, pakuti anakondwera ndi ine.

20 Yehova anandibwezera monga mwa chilungamo changa;

anandisudzula monga mwa kusisira kwa manja anga.

21 Pakuti ndasunga njira za Yehova,

ndipo sindinachitire choipa kusiyana ndi Mulungu wanga.

22 Pakuti maweruzo ake onse anali pamaso panga,

ndipo malemba ake sindinawachotse kwa ine.

23 Ndipo ndinakhala wangwiro ndi Iye,

ndipo ndinadzisunga wosachita choipa changa.

24 Ndimo anandisudzulira Yehova monga mwa chilungamo changa,

monga mwa kusisira kwa manja anga pamaso pake.

25 Pa wachifundo mukhala wachifundo;

pa munthu wangwiro mukhala wangwiro.

26 Pa woyera mtima mukhala woyera mtima;

pa wotsutsatsutsa mukhala wotsutsana naye.

27 Pakuti Inu muwapulumutsa anthu aumphawi;

koma maso okweza muwatsitsa.

28 Pakuti Inu muyatsa nyali yanga;

Yehova, Mulungu wanga, aunikira mdima wanga.

29 Pakuti mwa Inu ndipyola khamu la anthu;

ndipo mwa Mulungu wanga ndilumphira linga.

30 Mulungu ndiye wangwiro m’njira zake;

mau a Yehova ngoyengeka;

ndiye chikopa cha onse okhulupirira Iye.

31 Pakuti Mulungu ndani wosati Yehova?

Ndipo thanthwe ndani wosati Mulungu wathu?

32 Mulungu ndiye wondizingiza mphamvu m’chuuno,

nakonza njira yanga ikhale yangwiro.

33 Alinganiza mapazi anga ngati a mbawala,

nandiimitsa pamsanje panga.

34 Aphunzitsa manja anga agwire nkhondo;

kuti walifuka uta wamkuwa ndi manja anga.

35 Ndipo mwandipatsa chikopa cha chipulumutso chanu;

ndipo dzanja lamanja lanu landigwiriziza,

ndipo chifatso chanu chandikuza ine.

36 Mwandipondetsa patalipatali,

sanaterereke mapazi anga.

37 Ndidzalondola adani anga, ndi kuwapeza,

ndipo sindidzabwerera asanathe psiti.

38 Ndidzawapyoza kuti sangakhoze kuuka,

adzagwa pansi pa mapazi anga.

39 Pakuti mwandizingiza mphamvu m’chuuno ku nkhondoyo;

mwandigonjetsera amene andiukira.

40 Ndipo adani anga mwawalozetsa m’mbuyo kwa ine,

kuti ndipasule ondidawo.

41 Anafuula, koma panalibe wopulumutsa;

ngakhale kwa Yehova, koma sanawavomereze.

42 Pamenepo ndinawapera ngati fumbi la kumphepo;

ndinawakhuthula ngati matope a pabwalo.

43 Mwandipulumutsa pa zolimbana nane za anthu;

mwandiika mutu waamitundu;

mtundu wa anthu sindinaudziwe udzanditumikira.

44 Pakumva m’khutu za ine adzandimvera,

alendo adzandigonjera monyenga.

45 Alendo adzafota,

nadzatuluka monjenjemera m’ngaka mwao.

46 Yehova ngwa moyo; ndipo lidalitsike thanthwe langa;

nakwezeke Mulungu wa chipulumutso changa.

47 Ndiye Mulungu amene andibwezerera chilango,

nandigonjetsera mitundu ya anthu.

48 Andipulumutsa kwa adani anga.

Inde mundikweza pa iwo akundiukira ine,

mundikwatula kwa munthu wachiwawa.

49 Chifukwa chake Yehova ndidzakuyamikani mwa amitundu,

ndipo dzina lanu ndidzaliimbira.

50 Alanditsa mfumu yake ndi chipulumutso chachikulu;

nachitira chifundo wodzozedwa wake,

Davide, ndi mbumba yake, kunthawi zonse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/18-941b51d1b23796a989b54e0b72f4dd8b.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 19

Davide alemekeza zolengedwa ndi Mulungu, ndi malamulo ao omwe

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Zakumwamba zimalalikira ulemerero wa Mulungu;

ndipo thambo lionetsa ntchito ya manja ake.

2 Usana ndi usana uchulukitsa mau,

ndipo usiku ndi usiku uonetsa nzeru.

3 Palibe chilankhulidwe, palibe mau;

liu lao silimveka.

4 Muyeso wao wapitirira padziko lonse lapansi,

ndipo mau ao ku malekezero a m’dziko muli anthu.

Iye anaika hema la dzuwa m’menemo,

5 ndipo lili ngati mkwati wakutuluka m’chipinda mwake,

likondwera ngati chiphona kuthamanga m’njira.

6 Kutuluka kwake lituluka kolekezera thambo,

ndipo kuzungulira kwake lifikira ku malekezero ake;

ndipo kulibe kanthu kobisalira kutentha kwake.

7 Malamulo a Yehova ali angwiro, akubwezera moyo;

mboni za Yehova zili zokhazikika, zakuwapatsa opusa nzeru.

8 Malangizo a Yehova ali olungama, akukondweretsa mtima;

malamulo a Yehova ali oyera, akupenyetsa maso.

9 Kuopa Yehova kuli mbee, kwakukhalabe nthawi zonse;

maweruzo a Yehova ali oona, alungama konsekonse.

10 Ndizo zifunika koposa golide,

inde, golide wambiri woyengetsa;

zizuna koposa uchi ndi zakukha za zisa zake.

11 Ndiponso kapolo wanu achenjezedwa nazo,

m’kuzisunga izo muli mphotho yaikulu.

12 Adziwitsa zolowereza zake ndani?

Mundimasule kwa zolakwa zobisika.

13 Ndiponso muletse kapolo wanu pa zodzitama;

zisachite ufumu pa ine.

Pamenepo ndidzakhala wangwiro,

ndi wosachimwa cholakwa chachikulu.

14 Mau a m’kamwa mwanga ndi maganizo a m’mtima wanga

avomerezeke pamaso panu,

Yehova, thanthwe langa, ndi Mombolo wanga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/19-dbb1b75cff85c5c4a164cc3805ea20cf.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 20

Kupempherera mfumu potulukira iye kunkhondo

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Yehova akuvomereze tsiku la nsautso;

dzina la Mulungu wa Yakobo likuike pamsanje;

2 likutumizire thandizo lotuluka m’malo oyera,

ndipo likugwirizize kuchokera muZiyoni;

3 likumbukire zopereka zako zonse,

lilandire nsembe yako yopsereza;

4 likupatse cha mtima wako,

ndipo likwaniritse upo wako wonse.

5 Tidzafuula mokondwera mwa chipulumutso chanu,

ndipo m’dzina la Mulungu wathu tidzakweza mbendera;

Yehova akwaniritse mapempho ako onse.

6 Tsopano ndidziwa kuti Yehova apulumutsa wodzozedwa wake;

adzamvomereza mu Mwamba mwake moyera

ndi mphamvu ya chipulumutso cha dzanja lake lamanja.

7 Ena atama magaleta, ndi ena akavalo;

koma ife tidzatchula dzina la Yehova Mulungu wathu.

8 Iwowa anagonjeka, nagwa;

koma ife tauka, ndipo takhala chilili.

9 Yehova, pulumutsani,

mfumuyo ativomereze tsiku lakuitana ife.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/20-17416fa199165412977454d9dde10c18.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 21

Davide ayamika Mulungu pa kugonjetsa adani

Kwa Mkulu wa Nyimbo. Salimo la Davide.

1 Yehova, adzasekera mfumu mu mphamvu yanu;

adzakondwera kwakukulu m’chipulumutso chanu!

2 Mwampatsa iye chikhumbo cha mtima wake,

ndipo simunakane pempho la milomo yake.

3 Pakuti mufika kwa iye ndi madalitso okoma;

muika korona wa golide woyengetsa pamutu pake.

4 Anakupemphani moyo, mwampatsa iye;

mwamtalikitsira masiku kunthawi za nthawi.

5 Ulemerero wake ngwaukulu mwa chipulumutso chanu;

mumchitira iye ulemu ndi ukulu.

6 Pakuti mumuikira madalitso kunthawi zonse;

mumkondweretsa ndi chimwemwe pankhope panu.

7 Pakuti mfumu akhulupirira Yehova,

ndipo mwa chifundo cha Wam’mwambamwamba sadzagwedezeka iye.

8 Dzanja lanu lidzapeza adani anu onse,

dzanja lanu lamanja lidzapeza iwo akuda Inu.

9 Mudzawaika ngati ng’anjo yamoto pa nyengo ya mkwiyo wanu.

Yehova adzawatha m’kukwiya kwake,

ndipo moto udzawanyeketsa.

10 Mudzaziononga zobala zao kuzichotsa padziko lapansi,

ndi mbeu zao mwa ana a anthu.

11 Pakuti anakupangirani choipa,

anapangana chiwembu, osakhoza kuchichita.

12 Pakuti mudzawabweza m’mbuyo,

popiringidza m’nsinga zanu pankhope pao.

13 Kwezekani, Yehova, mu mphamvu yanu;

potero tidzaimba ndi kulemekeza chilimbiko chanu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/21-3b1823598324ec263045853364f077b7.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 22

Posautsidwa Davide adandaulira, apemphera, ayamika Mulungu

Kwa Mkulu wa Nyimbo: pa Ajelet Hasakara. Salimo la Davide.

1 Mulungu wanga, Mulungu wanga, mwandisiyiranji ine?

Mukhaliranji kutali kwa chipulumutso changa,

ndi kwa mau a kubuula kwanga?

2 Mulungu wanga, ndiitana usana, koma simuvomereza;

ndipo usiku, sindikhala chete.

3 Koma Inu ndinu woyera,

wakukhala m’malemekezo a Israele.

4 Makolo athu anakhulupirira Inu;

anakhulupirira, ndipo munawalanditsa.

5 Anafuula kwa Inu, napulumutsidwa;

anakhulupirira Inu, ndipo sanachite manyazi.

6 Koma ine ndine nyongolotsi, si munthu ai,

chotonza cha anthu, ndi wonyozedwa ndi anthu.

7 Onse akundipenya andiseka;

akwenzula, apukusa mutu, nati,

8 Adadzitengera kwa Yehova; kuti adzampulumutsa,

amlanditse tsopano popeza akondwera naye.

9 Pakuti Inu ndinu wondibadwitsa;

wondikhulupiritsa pokhala ine pa bere la mai wanga.

10 Chibadwire ine anandisiyira Inu,

kuyambira kwa mai wanga Mulungu wanga ndinu.

11 Musandikhalire kutali; pakuti nsautso ili pafupi,

pakuti palibe mthandizi.

12 Ng’ombe zamphongo zambiri zandizinga;

mphongo zolimba za ku Basani zandizungulira.

13 Andiyasamira m’kamwa mwao,

ngati mkango wozomola ndi wobangula.

14 Ndathiridwa pansi monga madzi,

ndipo mafupa anga onse anaguluka.

Mtima wanga ukunga sera;

wasungunuka m’kati mwa matumbo anga.

15 Mphamvu yanga yauma ngati phale;

ndi lilime langa likangamira kunsaya zanga;

ndipo mwandifikitsa kufumbi la imfa.

16 Pakuti andizinga agalu,

msonkhano wa oipa wanditsekereza;

andiboola m’manja anga ndi m’mapazi anga.

17 Ndikhoza kuwerenga mafupa anga onse;

iwo ayang’ana nandipenyetsetsa ine.

18 Agawana zovala zanga,

nachita maere pa malaya anga.

19 Koma Inu, Yehova, musakhale kutali;

mphamvu yanga Inu, mufulumire kundithandiza.

20 Landitsani moyo wanga kulupanga;

wokondedwa wanga kumphamvu ya galu,

21 ndipulumutseni m’kamwa mwa mkango;

inde mwandiyankha ine ndili pa nyanga za njati.

22 Ndidzalalikira dzina lanu kwa abale anga,

pakati pa msonkhano ndidzakulemekezani.

23 Inu akuopa Yehova, mumlemekeze;

inu nonse mbumba ya Yakobo, mumchitire ulemu;

ndipo muchite mantha ndi Iye, inu nonse mbumba ya Israele.

24 Pakuti sanapeputse ndipo sananyansidwe

ndi zunzo la wozunzika;

ndipo sanambisire nkhope yake;

koma pomfuulira Iye, anamva.

25 Lemekezo langa lidzakhala la Inu mu msonkhano waukulu,

zowinda zanga ndidzazichita pamaso pa iwo akumuopa Iye.

26 Ozunzika adzadya nadzakhuta,

adzayamika Yehova iwo amene amfuna,

ukhale moyo mtima wako nthawi zonse.

27 Malekezero onse a dziko lapansi adzakumbukira

nadzatembenukira kwa Yehova,

ndipo mafuko onse aamitunduadzagwadira pamaso panu.

28 Pakuti ufumuwo ngwa Yehova;

Iye achita ufumu mwa amitundu.

29 Onenepa onse a padziko lapansi adzadya nadzagwadira;

onse akutsikira kufumbi adzawerama pamaso pake,

ndi iye amene sadziwa kusunga moyo wake.

30 Mbumba ya anthu idzamtumikira;

kudzanenedwa za Ambuye ku mibadwo yakudza.

31 Iwo adzadza nadzafotokozera chilungamo chake

kwa anthu akadzabadwa, kuti Iye anachichita.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/22-be2bc28b2bd260d5d7142d35176ffe14.mp3?version_id=1068—

Categories
MASALIMO

MASALIMO 23

Amwai amene Yehova akhala Mbusa wao

Salimo la Davide.

1 Yehova ndiye mbusa wanga; sindidzasowa.

2 Andigonetsa kubusa lamsipu,

anditsogolera kumadzi odikha.

3 Atsitsimutsa moyo wanga;

anditsogolera m’mabande a chilungamo, chifukwa cha dzina lake.

4 Inde, ndingakhale ndiyenda m’chigwa cha mthunzi wa imfa,

sindidzaopa choipa; pakuti Inu muli ndi ine;

chibonga chanu ndi ndodo yanu, izi zindisangalatsa ine.

5 Mundiyalikira gome pamaso panga m’kuona kwa adani anga;

mwandidzoza mutu wanga mafuta; chikho changa chisefuka.

6 Inde ukoma ndi chifundo zidzanditsata

masiku onse a moyo wanga,

ndipo ndidzakhala m’nyumba ya Yehova masiku onse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/PSA/23-87d6e75eac2f73168f547c4625dcb6ed.mp3?version_id=1068—