Categories
NEHEMIYA

NEHEMIYA 12

Maina a ansembe ndi Alevi ofika ku Yerusalemu pamodzi ndi Zerubabele

1 Ndipo ansembe ndi Alevi amene anakwera ndi Zerubabele mwana wa Sealatiele, ndi Yesuwa, ndi awa: Seraya, Yeremiya, Ezara,

2 Amariya, Maluki, Hatusi,

3 Sekaniya, Rehumu, Meremoti,

4 Ido, Ginetoyi, Abiya,

5 Miyamini, Maadiya, Biliga,

6 Semaya, ndi Yoyaribu, Yedaya.

7 Salu, Amoki, Hilikiya, Yedaya. Awa ndi akulu a ansembe ndi abale ao m’masiku a Yesuwa.

8 Ndi Alevi ndiwo Yesuwa, Binuyi, Kadimiyele, Serebiya, Yuda, ndi Mataniya; iye ndi abale ake amatsogolera mayamiko.

9 Ndi Bakibukiya ndi Uni, abale ao, anawayang’anira maulonda.

10 Ndi Yesuwa anabala Yoyakimu, ndi Yoyakimu anabala Eliyasibu ndi Eliyasibu anabala Yoyada,

11 ndi Yoyada anabala Yonatani, ndi Yonatani, anabala Yaduwa.

12 Ndi m’masiku a Yoyakimu ansembe aakulu a nyumba za makolo ndiwo: wa Seraya, Meraya; wa Yeremiya, Hananiya;

13 wa Ezara, Mesulamu; wa Amariya, Yehohanani;

14 wa Maluki, Yonatani; wa Sebaniya, Yosefe;

15 wa Harimu, Adina; wa Meraiyoti, Helikai;

16 wa Ido, Zekariya; wa Ginetoni, Mesulamu;

17 wa Abiya, Zikiri; wa Miniyamini, wa Mowadiya, Pilitai;

18 wa Biliga, Samuwa; wa Semaya, Yehonatani;

19 ndi wa Yoyaribu, Matenai; wa Yedaya, Uzi;

20 wa Salai, Kalai; wa Amoki, Eberi;

21 wa Hilikiya, Hasabiya; wa Yedaya, Netanele.

22 M’masiku a Eliyasibu, Yoyada, Yohanani, ndi Yaduwa, Alevi analembedwa akulu a nyumba za makolo; ansembe omwe, mpaka ufumu wa Dariusi wa ku Persiya.

23 Ana a Levi, akulu a nyumba za makolo, analembedwa m’buku la machitidwe, mpaka masiku a Yohanani mwana wa Eliyasibu.

24 Ndi akulu a Alevi: Hasabiya, Serebiya, ndi Yesuwa mwana wa Kadimiyele, ndi abale ao openyana nao, kulemekeza ndi kuyamika, monga mwa lamulo la Davide munthu wa Mulungu, alonda kupenyana alonda.

25 Mataniya, ndi Bakibukiya, Obadiya, Mesulamu, Talimoni, Akubu, ndiwo odikira akulonda pa nyumba za chuma zili kuzipata.

26 Awa anakhala m’masiku a Yoyakimu mwana wa Yesuwa, mwana wa Yozadaki, ndi m’masiku a Nehemiya kazembe, ndi a Ezara wansembe mlembiyo.

Kuperekedwa kwa linga la Yerusalemu

27 Ndipo popereka linga laYerusalemuanafunafuna Alevi m’malo mwao monse, kubwera nao ku Yerusalemu, kuti achite kuperekaku mokondwera, ndi mayamiko, ndi kuimbira, ndi nsanje, zisakasa, ndi azeze.

28 Ana a oimbirawo anasonkhana ochokera ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi kumidzi ya Anetofa,

29 ndi ku Betegiligala, ndi ku minda ya Geba ndi Azimaveti; popeza oimbirawo adadzimangira midzi pozungulira Yerusalemu.

30 Ndipo ansembe ndi Alevi anadziyeretsa okha, nayeretsa anthu, ndi zipata, ndi linga.

31 Pamenepo ndinakwera nao akulu a Yuda pa lingali, ndinaikanso oyamikira magulu awiri akulu oyenda molongosoka; lina loyenda ku dzanja lamanja palinga kunka ku Chipata cha Kudzala;

32 ndi pambuyo pao anayenda Hosaya, ndi limodzi la magawo awiri a akulu a Yuda,

33 ndi Azariya, Ezara ndi Mesulamu,

34 Yuda, ndi Benjamini, ndi Semaya, ndi Yeremiya,

35 ndi ana ena a ansembe ndi malipenga: Zekariya mwana wa Yonatani, mwana wa Semaya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mikaya, mwana wa Zakuri, mwana wa Asafu,

36 ndi abale ake: Semaya, ndi Azarele, Milalai, Gilalai, Maai, Netanele, ndi Yuda, Hanani, ndi zoimbira za Davide munthu wa Mulungu; ndi Ezara mlembiyo anawatsogolera;

37 ndi ku Chipata cha ku Chitsime, ndi kundunji kwao, anakwerera pa makwerero a mzinda wa Davide, potundumuka linga, popitirira pa nyumba ya Davide, mpaka ku Chipata cha Madzi kum’mawa.

38 Ndi gulu lina la oyamikira linamuka mokomana nao, ndi ine ndinawatsata, pamodzi ndi limodzi la magawo awiri la anthu palinga, napitirira pa Nsanja ya Ng’anjo, mpaka kulinga lachitando;

39 ndi pamwamba pa Chipata cha Efuremu, ndi ku Chipata Chakale, ndi ku Chipata cha Nsomba, ndi Nsanja ya Hananele, ndi Nsanja ya Zana, mpaka ku Chipata cha Nkhosa; ndipo anaima ku Chipata cha Akaidi.

40 Atatero, magulu awiriwo a iwo oyamikira anaima m’nyumba ya Mulungu, ndipo ine ndi limodzi la magawo awiri a olamulira pamodzi ndi ine;

41 ndi ansembe, Eliyakimu, Maaseiya, Miniyamini, Mikaya, Eliyoenai, Zekariya, ndi Hananiya, ali nao malipenga;

42 ndi Maaseiya, ndi Semaya, ndi Eleazara, ndi Uzi, ndi Yehohanani, ndi Malikiya, ndi Elamu, ndi Ezere. Ndipo oimbira anaimbitsa Yezeraya ndiye woyang’anira wao.

43 Ndipo anaphera nsembe zambiri tsiku lija, nasekerera; pakuti Mulungu anawakondweretsa ndi chimwemwe chachikulu; ndi akazi omwe ndi ana anakondwera; ndi chikondwerero cha Yerusalemu chinamveka kutali.

Akonzanso za kupereka limodzi la magawo khumi

44 Ndipo tsiku lomwelo anaika anthu asunge zipinda za chuma, za nsembe zokweza, za zipatso zoyamba, ndi za limodzilimodzi la magawo khumi, kulonga m’mwemo, monga mwa minda ya midzi, magawo onenedwa ndi chilamulo, akhale a ansembe ndi Alevi; popeza Yuda anakondwera nao ansembe ndi Alevi akuimirirako.

45 Ndipo iwo anasunga udikiro wa Mulungu wao, ndi udikiro wa mayeretsedwe; momwemonso oimbira ndi odikira, monga mwa lamulo la Davide ndi la Solomoni mwana wake.

46 Pakuti m’masiku a Davide ndi Asafu kalelo kunali mkulu wa oimbira, ndi wa nyimbo zolemekeza ndi zoyamikira Mulungu.

47 Ndi Aisraele onse m’masiku a Zerubabele, ndi m’masiku a Nehemiya, anapereka magawo a oimbira ndi odikira, monga mudafunika tsiku ndi tsiku; nawapatulira Alevi; ndi Alevi anawapatulira ana a Aroni.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NEH/12-d60c071c94d49bac6f5232f0a30014b0.mp3?version_id=1068—

Categories
NEHEMIYA

NEHEMIYA 13

Tobiya achotsedwa ku Kachisi

1 Tsiku lomwelo anawerenga m’buku la Mose m’makutu a anthu, napeza m’menemo kuti Aamoni ndi Amowabu asalowe mu msonkhano wa Mulungu kunthawi yonse;

2 popeza sanawachingamire ana a Israele ndi chakudya ndi madzi, koma anawalemberera Balamu awatemberere; koma Mulungu wathu anasanduliza tembererolo likhale mdalitso.

3 Ndipo kunali, atamva chilamulocho, anasiyanitsa pa Israele anthu osokonezeka onse.

4 Chinkana ichi, Eliyasibu wansembe, woikidwa asunge zipinda za nyumba ya Mulungu wathu, anachita chibale ndi Tobiya,

5 namkonzera chipinda chachikulu, kumene adasungira kale zopereka za ufa,lubani, ndi zipangizo, ndi limodzilimodzi la magawo khumi a tirigu, vinyo, ndi mafuta, zolamulidwira Alevi, ndi oimbira, ndi odikira, ndi nsembe zokweza za ansembe.

6 Koma pochitika ichi chonse sindinkakhale kuYerusalemu; pakuti chaka cha makumi atatu ndi chachiwiri cha Arita-kisereksesi mfumu ya Babiloni ndinafika kwa mfumu, ndipo atapita masiku ena ndinapempha mfumu indilole;

7 ndipo ndinafika ku Yerusalemu, ndi kuzindikira choipa anachichita Eliyasibu, chifukwa cha Tobiya, ndi kumkonzera chipinda m’mabwalo a nyumba ya Mulungu.

8 Ndipo ndinaipidwa nacho kwambiri, motero ndinataya kubwalo akatundu onse a m’nyumba ya Tobiya, kuwachotsa m’chipindamo.

9 Pamenepo ndinalamulira, ndipo anayeretsa zipindazo; ndipo ndinabwezeramonso zipangizo za nyumba ya Mulungu, pamodzi ndi zopereka za ufa ndi lubani.

10 Ndinazindikiranso kuti sanapereke kwa Alevi magawo ao; m’mwemo Alevi ndi oimbira adathawira yense kumunda wake.

11 Potero ndinatsutsana nao olamulira, ndinati, Yasiyidwiranji nyumba ya Mulungu? Ndipo ndinawasonkhanitsa, ndi kuwaika m’malo mwao.

12 Ndi Ayuda onse anabwera nalo limodzilimodzi la magawo khumi a tirigu, ndi vinyo, ndi mafuta, kunyumba za chuma.

13 Ndinaikanso osunga chuma, asunge nyumba za chuma: Selemiya wansembe, ndi Zadoki mlembi; ndi wa Alevi, Pedaya; ndi wakuwathandiza, Hanani mwana wa Zakuri, mwana wa Mataniya; popeza anayesedwa okhulupirika ndi udindo wao, ndiwo kugawira abale ao.

14 Mundikumbukire Mulungu wanga mwa ichi, nimusafafanize zokoma zanga ndinazichitira nyumba ya Mulungu wanga, ndi maudikiro ake.

Tsiku la Sabata likhalanso lopatulika

15 Masiku awa ndinaona ku Yuda ena akuponda mphesa m’choponderamo tsiku laSabata, ndi akubwera nayo mitolo ya tirigu, ndi kuisenzetsa pa abulu; momwemonso vinyo, mphesa, ndi nkhuyu, ndi zosenza zilizonse, zimene analowa nazo mu Yerusalemu tsiku la Sabata, ndipo ndinawachitira umboni wakuwatsutsa tsikuli anagulitsa zakudya.

16 Anakhalanso m’menemo a ku Tiro, obwera nazo nsomba, ndi malonda ali onse, nagulitsa tsiku la Sabata kwa ana a Yuda ndi mu Yerusalemu.

17 Pamenepo ndinatsutsana nao aufulu a Yuda, ndinanena nao, Chinthu chanji choipa ichi muchichita, ndi kuipsa nacho tsiku la Sabata?

18 Sanatero kodi makolo anu, ndipo Mulungu wathu anatifikitsira ife ndi mzinda uno choipa ichi chonse? Koma inu muonjezera Israele mkwiyo pakuipsa Sabata.

19 Ndipo kunali, kukadayamba chizirezire pa zipata za Yerusalemu, losafika Sabata, ndinawauza atseke pamakomo; ndinawauzanso kuti asatsegulepo, koma litapita Sabata ndipo; ndipo ndinaimika anyamata anga ena pazipata, kuti pasalowe katundu tsiku la Sabata.

20 Momwemo eni malonda ndi ogulitsa malonda ali onse, anagona kunja kwa Yerusalemu kamodzi kapena kawiri.

21 Koma ndinawachitira umboni wakuwatsutsa, ndinanena nao, Mugoneranji pafupi pa linga? Mukateronso ndikuthirani manja. Kuyambira pomwepo sanafikenso pa Sabata.

22 Ndipo ndinauza Alevi kuti adziyeretse, nabwere, nasunge pazipata kupatula tsiku la Sabata. Mundikumbukire ichinso, Mulungu wanga, ndi kundileka monga mwa chifundo chanu chachikulu.

Nehemiya awadzudzula pa kukwatira akazi akunja

23 Masiku aja ndinaonanso Ayudawo anadzitengera akazi a Asidodi, Aamoni, ndi Amowabu,

24 ndi ana ao analankhula mwina Chiasidodi, osadziwitsa kulankhula Chiyuda, koma monga umo amalankhula mtundu wao uliwonse.

25 Ndipo ndinatsutsana nao, ndi kuwatemberera, ndi kukantha ena a iwo, ndi kumwetula tsitsi lao, ndi kuwalumbiritsa pa Mulungu ndi kuti, Musapereke ana anu aakazi kwa ana ao aamuna, kapena kutengera ana anu aamuna, kapena a inu nokha, ana ao aakazi.

26 Nanga Solomoni mfumu ya Israele sanachimwe nazo zinthu izi? Chinkana mwaamitunduambiri panalibe mfumu ngati iye, ndi Mulungu wake anamkonda, ndi Mulungu wake anamlonga mfumu ya Aisraele onse; koma ngakhale iye, akazi achilendo anamchimwitsa.

27 Ndipo kodi tidzamvera inu, kuchita choipa ichi chachikulu chonse, kulakwira Mulungu wathu ndi kudzitengera akazi achilendo?

28 Koma wina wa ana a Yehoyada, mwana wa Eliyasibu mkulu wa ansembe, anali mkamwini wa Sanibalati Muhoroni; chifukwa chake ndinampirikitsa kumchotsa kwa ine.

29 Muwakumbukire Mulungu wanga, popeza anadetsa unsembe, ndi pangano la unsembe, ndi la Alevi.

30 Momwemo ndinawayeretsa kuwachotsera achilendo onse, ndi kuikira udikiro ansembe ndi Alevi, yense kuntchito yake;

31 ndi chopereka cha nkhuni pa nthawi zoikika, ndi wa zipatso zoyamba. Mundikumbukire, Mulungu wanga, chindikomere.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NEH/13-fea8a3addb8ee063b35c35b39c807f29.mp3?version_id=1068—

Categories
ESTERE

ESTERE Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli likukamba za Estere, mtsikana wina wachiyuda, amene ankakonda kwambiri anthu a mtundu wake, naonetsa kulimba mtima kwake pothandiza kuwapulumutsa Ayudawo kwa adani ao. Lifotokozanso za chiyambi chake komanso tanthauzo la chikondwerero cha Chiyuda chotchedwa Purimu.

Za mkatimu

Estere asankhidwa kuti akhale mfumukazi kudziko la Persiya

1.1—2.23

Hamani apanga chiwembu chofuna kuwonongeratu fuko la Ayuda

3.1—5.14

Hamani atsutsidwa naphedwa

6.1—7.10

Ayuda agonjetsa adani ao

8.1—10.3

Categories
ESTERE

ESTERE 1

Madyerero a Ahasuwero

1 Izi zinachitika masiku a Ahasuwero, ndiye Ahasuweroyo anachita ufumu kuyambira Indiya kufikira Kusi, pa maiko zana limodzi mphambu makumi awiri kudza asanu ndi awiri.

2 Masiku ajawo, pokhala Ahasuwero pa mpando wa ufumu wake uli m’chinyumba cha ku Susa,

3 chaka chachitatu cha ufumu wake, anakonzera madyerero akalonga ake onse, ndi omtumikira; amphamvu a Persiya ndi Mediya, omveka ndi akalonga a maikowo anakhala pamaso pake,

4 pamene anaonetsa zolemera za ufumu wake waulemu, ndi ulemerero wa ukulu wake woposa, masiku ambiri, ndiwo masiku zana limodzi mphambu makumi asanu ndi atatu.

5 Atatha masikuwa, mfumu inakonzera madyerero anthu onse okhala m’chinyumba cha ku Susa, aakulu ndi aang’ono, masiku asanu ndi awiri, ku bwalo la munda wa maluwa wa ku chinyumba cha mfumu;

6 panali nsalu zolenjeka zoyera, zabiriwiri, ndi zamadzi, zomangika ndi zingwe za thonje labafuta, ndi lofiirira, pa zigwinjiri zasiliva, ndi nsanamira zansangalabwi; makama anali a golide ndi siliva pa mayalidwe a miyala yofiira, ndi yoyera, ndi yoyezuka, ndi yakuda.

7 Nawapatsa chakumwa m’zomwera zagolide, zomwerazo nzosiyanasiyana, ndi vinyo wachifumu anachuluka, monga mwa ufulu wa mfumu.

8 Ndi mamwedwewo anali monga mwa lamulo; panalibe kukakamiza; pakuti mfumu idaikira akulu onse a nyumba yake motero, kuti achite monga momwe akhumba aliyense.

Vasiti akana kuoneka kumadyerero

9 Vasiti yemwe, mkazi wamkulu, anakonzera akazi madyerero m’nyumba yachifumu ya mfumu Ahasuwero.

10 Tsiku lachisanu ndi chiwiri, pokondwera mtima wa mfumu ndi vinyo, iye anauza Mehumani, Bizita, Haribona, Bigita, ndi Abagita, Zetara, ndi Karikasi, adindo asanu ndi awiriwo akutumikira pamaso pa mfumu Ahasuwero,

11 abwere naye Vasiti mkazi wamkulu pamaso pa mfumu ndi korona wachifumu, kuonetsa anthu ndi akulu kukoma kwake; popeza anali wokongola maonekedwe ake.

12 Koma Vasiti mkazi wamkuluyo anakana kudza pa mau a mfumu adamuuza adindowo; potero mfumu idapsa mtima ndithu, ndi mkwiyo wake unatentha m’kati mwake.

Vasiti achotsedwa

13 Pamenepo mfumu inanena kwa eni nzeru, akudziwa za m’tsogolo, mfumu inkatero nao onse akudziwa malamulo ndi maweruzo,

14 a pafupi naye ndiwo Karisena, Setara, Adimata, Tarisisi, Meresi, Marisena, ndi Memukana, akalonga asanu ndi awiri a Persiya ndi Mediya, openya nkhope ya mfumu ndi kukhala oyamba mu ufumu.

15 Anati, Tidzachitanji naye mkazi wamkulu Vasiti monga mwa malamulo, popeza sanachite chomuuza mfumu Ahasuwero mwa adindo?

16 Ndi Memukana anati, pamaso pa mfumu ndi akalonga, Vasiti mkazi wamkulu sanalakwire mfumu yekha, komanso akalonga onse, ndi mitundu yonse ya anthu okhala m’maiko onse a mfumu Ahasuwero.

17 Pakuti machitidwe awa a mkazi wamkuluyo adzabuka kufikira akazi onse, kupeputsa amuna ao pamaso pao; anthu akati, Mfumu Ahasuwero anati abwere naye Vasiti mkazi wamkulu pamaso pake, koma sanadze iye.

18 Inde tsiku lomwelo akazi a akulu a Persiya ndi Mediya, atamva machitidwe a mkazi wamkuluyo, adzatero nao momwemo kwa akalonga onse a mfumu. Ndi chipeputso ndi mkwiyo zidzachuluka.

19 Chikakomera mfumu, atuluke mau achifumu pakamwa pake, nalembedwe m’malamulo a Apersiya ndi Amediya, angasinthike, kuti Vasiti asalowenso pamaso pa mfumu Ahasuwero; ndi mfumu aninkhe chifumu chake kwa mnzake womposa iye.

20 Ndipo mau amene adzaika mfumu akamveka mu ufumu wake wonse, (pakuti ndiwo waukulu), akazi onse adzachitira amuna ao ulemu, aakulu ndi aang’ono.

21 Ndipo mauwo anakonda mfumu ndi akalonga; ndi mfumu inachita monga mwa mau a Memukana,

22 natumiza makalata kumaiko onse a mfumu, kudziko lililonse monga mwa chilembedwe chao, ndi kumtundu uliwonse monga mwa chinenedwe chao, kuti mwamuna aliyense akhale wamkulu m’nyumba yakeyake, nawabukitse monga mwa chinenedwe cha anthu a mtundu wake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EST/1-a9c8d8271fc50291d3b8b867bd30a7e5.mp3?version_id=1068—

Categories
ESTERE

ESTERE 2

Ahasuwero akwatira Estere

1 Zitatha izi, utaleka mkwiyo wa mfumu Ahasuwero, anakumbukira Vasiti, ndi chochita iye, ndi chomlamulidwira.

2 Pamenepo anyamata a mfumu omtumikira anati, Amfunire mfumu anamwali okongola;

3 ndi mfumu aike oyang’anira m’maiko onse a ufumu wake, kuti asonkhanitse anamwali onse okongola m’chinyumba cha ku Susa, m’nyumba ya akazi; awasunge Hegai mdindo wa mfumu wosungira akazi, nawapatse zowayeretsa;

4 ndi namwali womkonda mfumu akhale mkazi wamkulu m’malo mwa Vasiti. Ndipo chinthuchi chinamkonda mfumu, nachita chomwecho.

5 Panali Myuda m’chinyumba cha ku Susa, dzina lake ndiye Mordekai, mwana wa Yairi, mwana wa Simei, mwana wa Kisi Mbenjamini;

6 uyu anatengedwa ndende kuYerusalemu, pamodzi ndi andende anatengedwa pamodzi ndi Yekoniya mfumu ya Yuda, amene Nebukadinezara mfumu ya Babiloni adamtenga ndende.

7 Ndipo iye adalera Hadasa, ndiye Estere, mwana wamkazi wa atate wake wamng’ono; popeza iye analibe atate kapena amai; ndi namwaliyo anali wa maonekedwe okoma, ndi wokongola; ndipo atamwalira atate wake ndi mai wake, Mordekai anamtenga akhale mwana wake.

8 Ndipo kunali, atamveka mau a mfumu ndi lamulo lake, ndipo atasonkhanidwa anamwali ambiri m’chinyumba cha ku Susa, awasunge Hegai, anamtenga Estere yemwe, alowe m’nyumba ya mfumu, amsunge Hegai wosunga akazi.

9 Ndipo namwaliyo anamkomera, namchitira chifundo; ndipo anafulumira kumpatsa zake zomyeretsa, ndi magawo ake, ndi anamwali asanu ndi awiri oyenera kumpatsa ochokera m’nyumba ya mfumu; ndipo anamsuntha iye ndi anamwali ake akhale m’malo okometsetsa m’nyumba ya akazi.

10 Estere sadawulule mtundu wake ndi chibale chake; pakuti Mordekai adamuuzitsa kuti asadziwulule.

11 Ndi Mordekai akayendayenda tsiku ndi tsiku kubwalo la nyumba ya akazi, kuti adziwe umo akhalira Estere, ndi chimene chidzamchitikira.

12 Kunafika tsono kulowa kwake kwa namwali aliyense, kuti alowe kwa mfumu Ahasuwero, atamchitira monga mwa lamulo la akazi, miyezi khumi ndi iwiri; pakuti ankakwaniritsa masiku a mayeretsedwe ao motero, miyezi isanu ndi umodzi ndi mafuta amure, ndi miyezi isanu ndi umodzi ndi zonunkhira bwino, ndi zoyeretsa akazi.

13 Ndipo namwali aliyense analowa kwa mfumu motero, zilizonse anafuna anampatsa zochokera m’nyumba ya akazi, alowe nazo kunyumba ya mfumu.

14 Madzulo ake analowamo, nabwera m’mawa mwake kunka kunyumba yachiwiri ya akazi, amsunge Saasigazi mdindo wa mfumu, wosunga akazi aang’ono a mfumu; iyeyu sanalowenso kwa mfumu, koma akakondwera naye mfumu, ndi kumuitana kumtchula dzina lake, ndiko.

15 Pofika tsono kulowa kwake kwa Estere mwana wa Abihaili, atate wamng’ono wa Mordekai, amene adadzitengera akhale mwana wake, kuti alowe kwa mfumu, sanafune kanthu koma zonena Hegai mdindo wa mfumu wosunga akazi ndizo. Ndipo Estere anayamikizidwa pamaso pa onse ompenya.

16 Momwemo anatengedwa Estere kunka kwa mfumu Ahasuwero, kunyumba yake yachifumu, mwezi wakhumi, ndiwo mwezi wa Tebeti, chaka chachisanu ndi chiwiri cha ufumu wake.

17 Ndipo mfumu inakonda Estere koposa akazi onse, nalandira iye kuyanja ndi chifundo pamaso pake, koposa anamwali onse; motero anaika korona wachifumu pamutu pake, namuyesa mkazi wamkulu m’malo mwa Vasiti.

18 Pamenepo mfumu inawakonzera madyerero akulu ake onse, ndi omtumikira, ndiwo madyerero a Estere; napumulitsa maiko, naninkha zaufulu monga mwa ufulu wa mfumu.

19 Ndipo posonkhanidwa anamwali nthawi yachiwiri Mordekai anali wa m’bwalo la mfumu.

20 Estere sadawulule chibale chake kapena mtundu wake, monga Mordekai adamuuza; popeza Estere anachita mau a Mordekai monga m’mene analeredwa naye.

Mordekai awulula chiwembu chofuna kupha mfumu

21 Masiku awa pokhala Mordekai wa m’bwalo la mfumu, Bigitana ndi Teresi, adindo awiri a mfumu osunga pakhomo, anapsa mtima, nayesa kumthira manja mfumu Ahasuwero.

22 Koma chidadziwika ichi kwa Mordekai, ndiye anafotokozera Estere mkazi wamkulu; ndi Estere anamuuza mfumu, kumnenera Mordekai.

23 Ndipo atafunsira mlanduwo, anaupeza momwemo, napachikidwa onse awiri pamtengo; ndipo anachilemba m’buku la mbiri pamaso pa mfumu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EST/2-6467998a4abb2f90d80dbbdaafe464df.mp3?version_id=1068—

Categories
ESTERE

ESTERE 3

Mordekai akana kugwadira Hamani

1 Zitatha izi, mfumu Ahasuwero anamkuza Hamani mwana wa Hamedata, wa ku Agagi, namkweza, naika mpando wake upose akalonga onse okhala naye.

2 Ndipo anyamata onse a mfumu okhala m’chipata cha mfumu anamweramira, namgwadira Hamani; pakuti mfumu idalamulira chotero za iye. Koma Mordekai sanamweramire kapena kumgwadira.

3 Ndipo anyamata a mfumu okhala m’chipata cha mfumu anati kwa Mordekai, Ulakwiranji pa lamulo la mfumu?

4 Kunali tsono, pomalankhula naye tsiku ndi tsiku, osawamvera iye, anauza Hamani, kuona ngati mlandu wa Mordekai udzakoma; popeza iye adawauza kuti ali Myuda.

5 Ndipo Hamani, pakuona kuti Mordekai sanamweramire kapena kumgwadira, mtima wake unadzala mkwiyo.

6 Koma anachiyesa chopepuka kumthira manja Mordekai yekha; pakuti adamfotokozera mtundu wake wa Mordekai; potero Hamani anafuna kuononga Ayuda onse okhala mu ufumu wonse wa Ahasuwero, ndiwo a mtundu wa Mordekai.

Hamani apangira mfumu kuti uphedwe mtundu wonse wa Ayuda

7 Mwezi woyamba ndiwo mwezi wa Nisani, chaka chakhumi ndi chiwiri cha mfumu Ahasuwero, anaombeza Puri, ndiwo ula, pamaso pa Hamani tsiku ndi tsiku, mwezi ndi mwezi, mpaka mwezi wakhumi ndi chiwiri, ndiwo mwezi wa Adara.

8 Ndipo Hamani anati kwa mfumu Ahasuwero, Pali mtundu wina wa anthu obalalika ndi ogawanikana mwa mitundu ya anthu m’maiko onse a ufumu wanu, ndi malamulo ao asiyana nao a anthu onse, ndipo sasunga malamulo a mfumu; chifukwa chake mfumu siiyenera kuwaleka.

9 Chikakomera mfumu, chilembedwe kuti aonongeke iwo; ndipo ndidzapereka matalente asilivazikwi khumi m’manja a iwo akusunga ntchito ya mfumu, abwere nao kuwaika m’nyumba za chuma cha mfumu.

10 Ndipo mfumu inavula mphete yake pa chala chake, naipereka kwa Hamani mwana wa Hamedata wa ku Agagi, mdani wa Ayuda.

11 Ndipo mfumu idati kwa Hamani, siliva akhale wako, ndi anthu omwe; uchite nao monga momwe chikukomera.

12 Pamenepo anaitana alembi a mfumu mwezi woyamba, tsiku lake lakhumi ndi chitatu, nalembera monga mwa zonse Hamani analamulira akazembe ndi ziwanga zoyang’anira maiko ali onse, ndi akalonga a mitundu iliyonse ya anthu, maiko ali onse monga mwa chilembedwe chao, ndi mitundu iliyonse ya anthu monga mwa chinenedwe chao; anazilemba m’dzina la mfumu Ahasuwero, nazisindikiza ndi mphete ya mfumu.

13 Ndipo anatumiza makalata ndi amtokoma kumaiko onse a mfumu, kuti aononge, aphe, napulule Ayuda onse, ndiwo ana, ndi okalamba, makanda, ndi akazi, tsiku limodzi, ndilo tsiku lakhumi ndi chitatu la mwezi wakhumi ndi chiwiri, ndiwo mwezi wa Adara; nalande zao mofunkha.

14 Mau a cholembedwacho, ndiwo kuti lichitike lamulo m’maiko onse, analalikidwa kwa anthu onse, kuti akonzekeretu tsiku lomwelo.

15 Amtokoma anatuluka ofulumizidwa ndi mau a mfumu, ndi lamulo linabukitsidwa m’chinyumba cha ku Susa; ndipo mfumu ndi Hamani anakhala pansi kumwa; koma mzinda wa Susa unadodoma.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EST/3-eea79e6d2ebfc5a02b411ef5478a965a.mp3?version_id=1068—

Categories
ESTERE

ESTERE 4

Mordekai adandaulira Estere anenere Ayuda kwa mfumu

1 Koma podziwa Mordekai zonse zidachitikazi, Mordekai anang’amba zovala zake, navala chiguduli ndi mapulusa, natuluka pakati pa mzinda, nafuula, nalira kulira kwakukulu ndi kowawa,

2 nafika popenyana ndi chipata cha mfumu; popeza sanathe munthu kulowa kuchipata cha mfumu wovala chiguduli.

3 Ndi m’maiko monse, paliponse anafikapo mau a mfumu ndi lamulo lake, panali maliro aakulu mwa Ayuda, ndi kusala, ndi kulira misozi, ndi kubuma; nagona m’chiguduli ndi mapulusa ambiri.

4 Ndipo anamwali a Estere ndi adindo ake anadza, namuuza; ndi mkazi wamkulu anawawidwa mtima kwambiri, natumiza chovala aveke Mordekai, ndi kumchotsera chiguduli chake; koma sanachilandire.

5 Pamenepo Estere anaitana Hataki mdindo wina wa mfumu, amene idamuika amtumikire, namuuza amuke kwa Mordekai, kuti adziwe ichi nchiyani ndi chifukwa chake ninji.

6 Natuluka Hataki kunka kwa Mordekai kukhwalala la mzinda linali popenyana ndi chipata cha mfumu.

7 Ndipo Mordekai anamfotokozera zonse zidamgwera, ndi mtengo wake wa ndalama adati Hamani adzapereka m’nyumba ya chuma cha mfumu pa Ayuda, kuwaononga.

8 Anampatsanso chitsanzo cha lamulo lolembedwa adalibukitsa mu Susa, kuwaononga, achionetse kwa Estere, ndi kumfotokozera, ndi kumlangiza alowe kwa mfumu, kumpembedza, ndi kupempherera anthu ake kwa iye.

9 Nadza Hataki, namuuza Estere mau a Mordekai.

10 Pamenepo Estere ananena ndi Hataki, namtuma akauze Mordekai, ndi kuti,

11 Akapolo onse a mfumu ndi anthu a m’maiko a mfumu adziwa kuti aliyense, ngakhale wamwamuna kapena wamkazi, akalowa kwa mfumu kubwalo la m’katimo wosaitanidwa, lamulo la pa iye ndi limodzi, ndilo kuti amuphe, akapanda mfumu kumloza ndi ndodo yachifumu yagolide kuti akhale ndi moyo; koma ine sanandiitane ndilowe kwa mfumu masiku awa makumi atatu.

12 Ndipo anamuuza Mordekai mau a Estere.

13 Koma Mordekai anawauza ambwezere mau Estere, kuti, Usamayesa m’mtima mwako kuti udzapulumuka m’nyumba ya mfumu koposa Ayuda ena onse.

14 Pakuti ukakhala chete konse tsopano lino, chithandizo ndi chipulumutso kwa Ayuda zidzafuma kwina; koma iwe ndi nyumba ya atate wako mudzaonongeka; ndipo kaya, kapena walowera ufumu chifukwa cha nyengo yonga iyi.

15 Pamenepo Estere anati ambwezere mau Mordekai,

16 Muka, sonkhanitsa Ayuda onse opezeka mu Susa, nimundisalire, osadya osamwa masiku atatu, usiku ndi usana, ine ndemwe ndi anamwali anga tidzasala momwemo, ndipo motero ndidzalowa kwa mfumu, ndiko kosalingana ndi lamulo; ndikaonongeka tsono ndionongeke.

17 Napita Mordekai, nachita monga mwa zonse adamlamulira Estere.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EST/4-cb926a6a03089c2fc13f8f1f62a652de.mp3?version_id=1068—

Categories
ESTERE

ESTERE 5

Estere alowa kwa mfumu nampempha iye ndi Hamani azidya naye

1 Ndipo kunali tsiku lachitatu, Estere anavala zovala zake zachifumu, nakaimirira m’bwalo la m’kati la nyumba ya mfumu, popenyana pa nyumba ya mfumu; ndi mfumu inakhala pa mpando wake wachifumu m’nyumba yachifumu, pandunji polowera m’nyumba.

2 Ndipo kunali, pamene mfumu inaona Estere mkazi wamkuluyo alikuima m’bwalo, inamkomera mtima; ndi mfumu inamloza Estere ndi ndodo yachifumu yagolide inali m’dzanja lake. Nayandikira Estere, nakhudza nsonga ya ndodoyo.

3 Ninena naye mfumu, Mufunanji, Estere mkazi wamkulu? Pempho lanu nchiyani? Lidzaperekedwa kwa inu, kufikira limodzi la magawo awiri a ufumuwo.

4 Ndipo Estere anati, Chikakomera mfumu, adze mfumu ndi Hamani lero ku madyerero ndinawakonzera.

5 Niti mfumu, Mumfulumize Hamani, achitike mau a Estere. Nidza mfumu ndi Hamani ku madyerero adawakonzera Estere.

6 Ndipo mfumu inati kwa Estere pa madyerero a vinyo, Pempho lanu nchiyani? Lidzaperekedwa kwa inu; mufunanji? Chidzachitika, kufikira limodzi la magawo awiri a ufumuwo.

7 Nayankha Estere, nati, Pempho langa ndi kufuna kwanga ndiko,

8 ngati mfumu indikomera mtima, ngatinso chakomera mfumu kupereka pempho langa ndi kuchita chofuna ine, adze mfumu ndi Hamani ku madyerero ndidzawakonzera; ndipo mawa ndidzachita monga yanena mfumu.

Hamani amangitsa popachika Mordekai

9 Ndipo Hamani anatuluka tsiku lomwelo wosekerera ndi wokondwera mtima; koma pamene Hamani anapenya Mordekai kuchipata cha mfumu, osamnyamukira kapena kumfumukira, Hamani anadzazidwa ndi mkwiyo pa Mordekai.

10 Koma Hamani anadziletsa, namuka kwao, natumiza munthu kukatenga mabwenzi ake, ndi Zeresi mkazi wake.

11 Nawawerengera Hamani kulemera kwake kwakukulu, ndi ana ake ochuluka, ndi zonse mfumu idamkuza nazo, ndi umo adamkweza koposa akalonga ndi anyamata a mfumu.

12 Hamani anatinso, Ndiponso Estere mkazi wamkulu sanalole mmodzi yense alowe pamodzi ndi mfumu ku madyerero adakonzawo, koma ine ndekha; nandiitana mawanso pamodzi ndi mfumu.

13 Koma zonsezi sindipindula nazo kanthu konse, pokhala ndilikuona Mordekai Myudayo alikukhala kuchipata cha mfumu.

14 Pamenepo Zeresi mkazi wake, ndi mabwenzi ake onse ananena naye, Apange mtengo, msinkhu wake mikono makumi asanu, ndi mawa mukanene nayo mfumu kuti ampachike Mordekai pamenepo; nimulowe pamodzi ndi mfumu kumadyerero wokondwera. Ndipo ichi chidakomera Hamani, napangitsa anthu mtengowo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EST/5-e7a4c7f6f71f6e042737b74502072b00.mp3?version_id=1068—

Categories
ESTERE

ESTERE 6

Ahasuwero aona chifukwa cha kuchitira Mordekai ulemu

1 Usiku uja tulo tidamwazikira mfumu, niti abwere nalo buku la mbiri, naliwerenga pamaso pa mfumu.

2 Napeza mudalembedwa kuti Mordekai adawulula za Bigitana ndi Teresi, awiri a adindo a mfumu osunga pakhomo, amene adayesa kumthira manja mfumu Ahasuwero.

3 Niti mfumu, Anamchitira Mordekai ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha ichi? Ndipo anyamata a mfumu akuitumikira ananena nayo, Sanamchitire kanthu.

4 Niti mfumu, Ali kubwalo ndani? Koma Hamani adalowa m’bwalo lakunja la nyumba ya mfumu kulankhula ndi mfumu za kupachika Mordekai pamtengo adaukonzeratu.

5 Ndipo anyamata a mfumu ananena nayo, Taonani, Hamani alikuima pabwalo. Niti mfumu, Alowe.

6 Nalowa Hamani. Ndipo mfumu inati kwa iye, Kodi amchitire chiyani munthu amene mfumu ikondwera kumchitira ulemu? Ndipo Hamani anati mumtima mwake, Ndaniyo mfumu ikondwera kumchitira ulemu koposa ine?

7 Nati Hamani kwa mfumu, Munthu amene mfumu ikondwera kumchitira ulemu,

8 amtengere chovala chachifumu amachivala mfumu, ndi kavalo amakwerapo mfumu, naike korona wachifumu pamutu pake,

9 napereke chovala ndi kavalo m’dzanja la wina womveketsa wa akalonga a mfumu, naveke nacho munthu amene mfumu ikondwera kumchitira ulemu, namuyendetse pa kavaloyo m’khwalala la m’mzinda, nafuule pamaso pake, Azitero naye munthu amene mfumu ikondwera kumchitira ulemu.

10 Pamenepo mfumu inati kwa Hamani, Fulumira, tenga chovala ndi kavalo monga umo wanenera, nuchitire chotero Mordekai Myudayo, wokhala pa chipata cha mfumu; kasasowepo kanthu ka zonse wazinena.

11 Ndipo Hamani anatenga chovala ndi kavalo, naveka Mordekai, namuyendetsa pa kavalo m’khwalala la m’mzinda, nafuula pamaso pake, Azitero naye munthu amene mfumu ikondwera kumchitira ulemu.

12 Ndipo Mordekai anabweranso kuchipata cha mfumu. Koma Hamani anafulumira kunka kwao, wachisoni ndi wofunda mutu wake.

13 Ndipo Hamani anafotokozera Zeresi mkazi wake, ndi mabwenzi ake onse, zonse zidamgwera. Nanena naye anzeru ake, ndi Zeresi mkazi wake, Mordekai amene wayamba kutsika pamaso pake, akakhala wa mbumba ya Ayuda, sudzamgonjetsa; koma udzagwada pamaso pake.

14 Akali chilankhulire naye, anafika adindo a mfumu, nafulumira kumtenga Hamani kunka naye kumadyerero adawakonzera Estere.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EST/6-27c76f2781e0383f3aede7a9a2152c0f.mp3?version_id=1068—

Categories
ESTERE

ESTERE 7

Hamani aululidwa napachikidwa

1 Motero inadza mfumu ndi Hamani kumwa naye mkazi wamkulu Estere.

2 Nitinso mfumu kwa Estere tsiku lachiwirili pa madyerero a vinyo, Pempho lanu nchiyani, mkazi wamkulu Estere? Lidzapatsidwa kwa inu; mufunanji? Chidzachitika, kufikira limodzi la magawo awiri a ufumu wanga.

3 Nayankha mkazi wamkulu Estere, nati, Ngati mwandikomera mtima, mfumu, ndipo chikakomera mfumu, andilekere moyo wanga pa kupempha kwanga, ndi wa anthu a mtundu wanga pa pempho langa;

4 pakuti tagulitsidwa; ine ndi anthu a mtundu wanga, kuti ationonge, atiphe, natipulule. Koma tikadagulitsidwa tikhale akapolo ndi adzakazi, ndikadakhala chete; chinkana wosautsa sakadatha kubwezera kusowa kwa mfumu.

5 Pamenepo mfumu Ahasuwero inalankhula, niti kwa mkazi wamkulu Estere, Ndani uyu, ali kuti iyeyu wadzazidwa mtima wake kuti azitero?

6 Nati Estere, Munthu wosautsa ndi mdani ndiye Hamani woipa uyu. Pamenepo Hamani anagwidwa mantha pamaso pa mfumu ndi mkazi wamkulu.

7 Ninyamuka mfumu mu mkwiyo wake ku madyerero a vinyo, nimka kumunda wa maluwa wa kuchinyumba; koma Hamani anatsalira kudzipempherera moyo kwa mkazi wamkulu Estere; popeza anapenya kuti mfumu inatsimikiza mtima kumchitira choipa.

8 Nibwera mfumu kumunda wa maluwa wa kuchinyumba kulowanso m’nyumba munali madyerero a vinyo, napeza Hamani atagwa pa kama wokhalapo Estere. Niti mfumu, Kodi aumiriza mkazi wamkulu pamaso panga m’nyumba? Potuluka mau pakamwa pa mfumu anamphimba Hamani nkhope.

9 Nati Haribona wina wa adindo okhala pamaso pa mfumu, Taonaninso, mtengowo msinkhu wake mikono makumi asanu, umene Hamani anaupangira Mordekai wonenera mfumu zokoma, uimiritsidwa m’nyumba ya Hamani. Niti mfumu, Mpachike pomwepo.

10 Nampachika Hamani pa mtengo adaukonzera Mordekai. Pamenepo mkwiyo wa mfumu unatsika.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/EST/7-efd0056250ce2adcc1446396331db1d9.mp3?version_id=1068—