Categories
ZEKARIYA

ZEKARIYA Mau Oyamba

Mau Oyamba

Bukuli lili ndi zigawo ziwiri: Gawo loyamba ndi mau amene mneneri adalalikira kuyambira chaka cha 520 BC. Zekariya akulongosola zimene adaziwona m’masomphenya ndipo akuwachenjeza anthuwo nawalimbitsa mtima kuti akonzenso Kachisi komanso mzinda wa Yerusalemu. Iwo ayenera adziyeretsa popeza Yehova adzawadalitsa (1—8). Gawo lachiwiri ndi kaundula wa mauneneri osiyanasiyana onena za kubwera kwa Mesiya ndipo tsiku la chiweruzo (9—14).

Za mkatimu

Mau oyamba

1.1—8.23

Mau a Yehova aimba mlandu mitundu ina ya anthu

9.1-8

Mau ena olonjeza zabwino

9.9—14.21

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *