Categories
ZEKARIYA

ZEKARIYA 7

Kusala kosalamulidwa ndi Yehova

1 Ndipo kunachitika chaka chachinai cha mfumu Dariusi, mau a Yehova anadza kwa Zekariya tsiku lachinai la mwezi wachisanu ndi chinai, ndiwo Kisilevi.

2 Ndipo a ku Betele anatuma Sarezere ndi Regemumeleke ndi anthu ao, apepeze Yehova,

3 nanene kwa ansembe a nyumba ya Yehova wa makamu, ndi kwa aneneri, ndi kuti, Kodi ndilire mwezi wachisanu, ndi kudzipatula, monga umo ndikachitira zaka izi zambiri?

4 Ndipo mau a Yehova wa makamu anadza kwa ine, ndi kuti,

5 Nena kwa anthu onse a m’dziko, ndi kwa ansembe, kuti, Muja mukasala ndi kulira mwezi wachisanu, ndi wachisanu ndi chitatu, zaka izi makumi asanu ndi awiri, kodi mukasalira Ine, Inedi?

6 Ndipo pamene mukadya si ndinu, mukamwa si ndinu kodi?

7 Si ndiwo mau Yehova anawalalikira mwa aneneri oyamba aja, mujaYerusalemuanali nao okhalamo, ndi wokhazikika; ndi m’mizinda mwake pozungulira pake, ndi m’dziko la kumwera, ndi m’chidikha munali anthu okhalamo?

8 Ndipo mau a Yehova anadza kwa Zekariya, ndi kuti,

9 Watero Yehova wa makamu, kuti, Weruzani chiweruzo choona, nimuchitire yense mnzake chifundo ndi ukoma mtima;

10 musazunza mkazi wamasiye, kapena ana amasiye, mlendo kapena waumphawi; ndipo nnena mmodzi wa inu alingirire m’mtima mwake kumchitira choipa munthu mnzake.

11 Koma anakana kumvera, nakaniza phewa lao, natseka makutu ao, kuti asamve.

12 Inde, anasanduliza mitima yao ikhale ngati mwala woti gwaa, kuti angamve chilamulo, ndi mau amene Yehova wa makamu anatumiza ndi Mzimu wake mwa aneneri oyamba aja; m’menemo munafuma mkwiyo waukulu wochokera kwa Yehova wa makamu.

13 Ndipo kunachitika, monga Iye anafuula, koma iwo sanamvere; momwemo iwo adzafuula, koma Ine sindidzamva, ati Yehova wa makamu;

14 koma ndidzawabalalitsa ndi kamvulumvulu mwaamitunduonse amene sanawadziwe. Motero dziko linakhala bwinja, m’mbuyo mwao; palibe munthu wopitapo ndi kubwererako; pakuti adaika dziko lofunikalo labwinja.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ZEC/7-6fa61a3e094bb34955944e7cfd5d72b2.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *