Masomphenya achinai: Satana atsutsana ndi Yoswa, Mulungu amuyesa wolungama
1 Pamenepo anandionetsa Yoswa mkulu wa ansembe alikuima pamaso pa mthenga wa Yehova, ndiSatanaalikuima padzanja lake lamanja, atsutsana naye.
2 Ndipo Yehova anati kwa Satana, Yehova akudzudzula, Satana iwe; inde Yehova amene anasankhaYerusalemuakudzudzula; uyu sindiye muuni wofumulidwa kumoto?
3 Koma Yoswa analikuvala nsalu zonyansa naima pamaso pa mthenga.
4 Ndipo Iye anayankha nanena ndi iwo akuima pamaso pake, ndi kuti, Mumvule nsalu zonyansazi. Nati kwa iye, Taona, ndakuchotsera mphulupulu zako, ndipo ndidzakuveka zovala za mtengo wake.
5 Ndipo ndinati, Amuike nduwira yoyera pamutu pake. Naika nduwira yoyera pamutu pake, namveka ndi zovala; ndi mthenga wa Yehova anaimirirapo.
6 Ndipo mthenga wa Yehova anamchitira Yoswa umboni, ndi kuti,
7 Atero Yehova wa makamu: Ukadzayenda m’njira zanga, ndi kusunga udikiro wanga, pamenepo udzaweruza nyumba yanga, ndi kusunga mabwalo anga, ndipo ndidzakupatsa malo oyendamo mwa awa oimirirapo.
8 Tamvera tsono, Yoswa mkulu wa ansembe, iwe ndi anzako akukhala pansi pamaso pako; pakuti iwo ndiwo chizindikiro; pakuti taonani, ndidzafikitsa mtumiki wanga, ndiye Mphukira.
9 Pakuti taona mwalawo ndinauika pamaso pa Yoswa; pamwala umodzi pali maso asanu ndi awiri; taonani, ndidzalocha malochedwe ake, ati Yehova wa makamu, ndipo ndidzachotsa mphulupulu ya dziko lija tsiku limodzi.
10 Tsiku lomwelo, ati Yehova wa makamu, mudzaitanizana yense mnansi wake patsinde pa mpesa ndi patsinde pa mkuyu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ZEC/3-6e416660f40a36224188901a3941cce1.mp3?version_id=1068—