Mau Oyamba
Bukuli likukamba za m’mene Aisraele adalowera m’dziko la Kanani nkulilanda, Yoswa akuwatsogolera. Kenaka adagawana dzikolo.
Nkhani zodziwika bwino m’bukuli ndizo kuoloka Yordani, kugwa kwa Yeriko, kugonjetsedwa kwa Ai, ndi kukonzanso kwa chipangano pakati pa Mulungu ndi anthu ake.
Mau odziwika bwino ndi awa: “mudzisankhire lero amene mudzamtumikira…koma ine, ndi a m’nyumba yanga, tidzatumikira Yehova” (24.15).
Za mkatimu
Aisraele atenga dziko la Kanani
1.1—12.24
a. Aoloka mtsinje wa Yordani
1.1—5.15
b. Agonjetsa mzinda la Yeriko
6.1—7.26
c. Agonjetsa mzinda wa Ai ndi mizinda ina
8.1—12.24
Aisraele agawana dziko
13.1—22.34
a. Dziko la kum’mawa kwa Yordani
13.1-33
b. Dziko la kuzambwe kwa Yordani
14.1—19.51
c. Mizinda yopulumukirako
20.1-9
d. Mafuko awiri akum’mawa abwerera ku dziko lao
22.1-34
Mau a Yoswa otsanzikana nawo
23.1-16
Abwereza kuchita chipangano ku Sekemu
24.1-33