Categories
YOSWA

YOSWA 8

Kupasulidwa kwa Ai

1 Pamenepo Yehova anati kwa Yoswa, Usaope, kapena kutenga nkhawa, tenga anthu onse a nkhondo apite nawe, ndipo tauka, kwera ku Ai; taona, ndapereka m’dzanja lako mfumu ya ku Ai, ndi anthu ake ndi mzinda wake ndi dziko lake;

2 ndipo uzimchitira Ai ndi mfumu yake monga umo unamchitira Yeriko ndi mfumu yake; koma zofunkha zake ndi ng’ombe zake mudzifunkhire nokha; udziikire anthu alalire kukhonde kwa mzinda.

3 Pamenepo anauka Yoswa, ndi anthu onse a nkhondo, kuti akwere ku Ai; ndipo Yoswa anasankha amuna zikwi makumi atatu, ndiwo ngwazi, nawatumiza apite usiku,

4 nawalamulira ndi kuti, Taonani, muzikhala olalira kukhonde kwa mzinda; musakhalira kutali ndi mzinda, koma mukhale okonzekeratu nonse;

5 ndipo ine, ndi anthu onse ali nane, tidzayandikira mzinda; ndipo kudzali, pamene atuluka kudzakomana nafe, monga poyamba paja, tidzathawa pamaso pao;

6 ndipo adzatuluka kutitsata mpaka tidawakokera asiyane ndi mzinda; pakuti adzanena, Atithawa pamaso pathu monga poyamba paja; nafenso tidzathawa pamaso pao;

7 pamenepo muziuka m’molalira ndi kulowa m’mzinda; pakuti Yehova Mulungu wanu; adzaupereka m’manja mwanu.

8 Ndipo kudzali, mutagwira mzinda, muzitentha mzindawo ndi moto; muzichita monga mwa mau a Yehova; taonani, ndakulamulirani.

9 Ndipo Yoswa anawatuma, namuka iwo kulowa m’molalira, nakhala pakati pa Betele ndi Ai, kumadzulo kwa Ai; koma Yoswa anakhala mwa anthu usiku uja.

10 Ndipo Yoswa analawira m’mamawa, nayesa anthu, nakwera, iye ndi akulu a Israele, pamaso pa anthu a ku Ai.

11 Ndi anthu onse a nkhondo okhala naye anakwera, nayandikira nafika pamaso pa mzinda, namanga misasa kumpoto kwa Ai; koma pakati pa iye ndi Ai panali chigwa.

12 Ndipo anatenga amuna ngati zikwi zisanu, nawaika m’molalira pakati pa Betele ndi Ai, kumadzulo kwa mzinda.

13 Momwemo anaika anthu, khamu lonse lokhala kumpoto kwa mzinda, ndi olalira ao kumadzulo kwa mzinda, ndipo usiku uja Yoswa analowa pakati pa chigwa.

14 Ndipo kunali, pamene mfumu ya ku Ai anachiona, anafulumira iwo, nalawira mamawa, natuluka amuna a m’mzinda kuthirana ndi Israele, iye ndi anthu ake onse, poikidwiratu patsogolo pa chidikha; popeza sanadziwe kuti amlalira kukhonde kwa mzinda.

15 Ndipo Yoswa ndi Aisraele onse anaoneka ngati a ku Ai alikuwathyola, nathawira njira ya kuchipululu.

16 Pamenepo anthu onse okhala m’mzinda, anaitanidwa awapirikitse, nampirikitsa Yoswa, nakokedwa kusiyana ndi mzinda.

17 Ndipo sanatsale mwamuna mmodzi yense mu Ai kapena mu Betele osatulukira kwa Israele; nasiya mzinda wapululu, napirikitsa Israele.

18 Pamenepo Yehova anati kwa Yoswa, Tambasula nthungoyo ili m’dzanja lako iloze ku Ai, pakuti ndidzaupereka m’dzanja lako. Ndipo Yoswa anatambasula nthungoyo inali m’dzanja lake kuloza mzinda.

19 Nauka msanga olalirawo m’mbuto mwao, nathamanga pamene anatambasula dzanja lake, nalowa m’mzinda, naugwira; nafulumira nayatsa mzindawo.

20 Pamene amuna a ku Ai anacheuka, anapenya, ndipo taonani, utsi wa mzinda unakwera kumwamba; nasowa mphamvu iwo kuthawa chakuno kapena chauko; ndi anthu othawira kuchipululu anatembenukira owapirikitsa.

21 Ndipo pakupenya Yoswa ndi Israele yense kuti olalirawo adagwira mzinda, ndi kuti utsi wa mzinda unakwera, anabwerera, nawapha amuna a ku Ai.

22 A kumzindanso anawatulukira; potero anakhala pakati pa Israele, ena mbali ina, ena mbali ina; ndipo anawakantha, mpaka sanatsale kapena kupulumuka wa iwo ndi mmodzi yense.

23 Koma mfumu ya ku Ai anamgwira wamoyo, nadza naye kwa Yoswa.

24 Ndipo kunali, atatha Israele kupha nzika zonse za ku Ai, kuthengo, kuchipululu kumene anawapirikitsira, natha onse kugwa ndi lupanga lakuthwa mpaka adathedwa onse, Aisraele onse anabwerera ku Ai, naukantha ndi lupanga lakuthwa.

25 Ndipo onse amene adagwa tsiku lija, amuna ndi akazi, ndiwo zikwi khumi ndi ziwiri, anthu onse a ku Ai.

26 Popeza Yoswa sanabweze dzanja lake limene anatambasula nalo nthungo, mpaka ataononga konse nzika zonse za ku Ai.

27 Koma ng’ombe ndi zofunkha za mzinda uwu Israele anadzifunkhira monga mwa mau a Yehova amene analamulira Yoswa.

28 Ndipo Yoswa anatentha Ai, nausandutsa muunda ku nthawi yonse, bwinja kufikira lero lino.

29 Ndipo mfumu ya ku Ai, anampachika pamtengo mpaka madzulo; koma polowa dzuwa Yoswa analamulira kuti atsitse mtembo wake pamtengo; ndipo anauponya polowera pa chipata cha mzinda; naunjikako mulu waukulu wamiyala, mpaka lero lino.

Apereka nsembe nawerenga Malamulo a Mose ku Ebala ndi Gerizimu

30 Pomwepo Yoswa anamangira Yehova Mulungu wa Israele guwa la nsembe m’phiri la Ebala,

31 monga Mose mtumiki wa Mulungu adalamulira ana a Israele, monga mulembedwa m’buku la chilamulo cha Mose, guwa la nsembe la miyala yosasema, yoti palibe munthu anakwezapo chitsulo; ndipo anafukizirapo Yehova nsembe zopsereza, naphera nsembe zoyamika.

32 Ndipo analembapo pa miyalayi chitsanzo cha chilamulo cha Mose, chimene analembera pamaso pa ana a Israele.

33 Ndipo Aisraele onse, ndi akulu ao, ndi akapitao ao, ndi oweruza ao anaima chakuno ndi chauko cha likasa, pamaso pa ansembe Alevi, akusenzalikasa la chipanganola Yehova, mbadwa ndi alendo omwe; ena a iwo pandunji paphiri la Gerizimu, ndi ena pandunji paphiri la Ebala; monga Mose, mtumiki wa Yehova, adalamulira poyamba paja kuti adalitse anthu a Israele.

34 Atatero, anawerenga mau onse a chilamulo, dalitso ndi temberero, monga mwa zonse zolembedwa m’buku la chilamulo.

35 Panalibe mau amodzi a zonse adazilamulira Mose osawerenga Yoswa pamaso pa msonkhano wonse wa Israele, ndi akazi ndi ana aang’ono, ndi alendo akuyenda pakati pao.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/8-1622db8fca89bda53e311bd9b5bc2076.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *