Malire a Efuremu
1 Ndipo gawo la ana a Yosefe linatuluka kuchokera ku Yordani ku Yeriko, ku madzi a Yeriko kum’mawa, kuchipululu, nakwera kuchokera ku Yeriko kunka kumapiri ku Betele;
2 natuluka ku Betele kunka ku Luzi, napitirira kunka ku malire a Aariki, ku Ataroti;
3 natsikira kumadzulo kunka ku malire a Ayafileti, ku malire a Betehoroni wa kunsi, ndi ku Gezere; ndi matulukiro ake anali kunyanja.
4 Motero ana a Yosefe, Manase ndi Efuremu analandira cholowa chao,
5 Ndipo malire a ana a Efuremu, monga mwa mabanja ao, ndiwo: malire a cholowa chao kum’mawa ndiwo Ataroti-Adara, mpaka Betehoroni wa kumtunda;
6 natuluka malire kumadzulo ku Mikametati kumpoto; nazungulira malire kum’mawa kunka ku Taanatisilo, naupitirira kum’mawa kwake kwa Yanowa:
7 natsika kuchokera ku Yanowa, kunka ku Ataroti, ndi ku Naara, nafika ku Yeriko, natuluka ku Yordani.
8 Kuyambira ku Tapuwa malire anamuka kumadzulo ku mtsinje wa Kana; ndi matulukiro ake anali kunyanja. Ichi ndi cholowa cha fuko la ana a Efuremu monga mwa mabanja ao;
9 pamodzi ndi mizinda adaipatulira ana a Efuremu pakati pa cholowa cha ana a Manase, mizinda yonse pamodzi ndi midzi yao.
10 Ndipo sanaingitse Akanani akukhala mu Gezere; koma Akanani anakhala pakati pa Efuremu, kufikira lero lino, nawaumiriza kugwira ntchito yathangata.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOS/16-c28510d9b513a4592e152d301ab60b4c.mp3?version_id=1068—