Categories
YOHANE

YOHANE 2

Yesu asandutsa madzi vinyo ku Kana

1 Ndipo tsiku lachitatu panali ukwati mu Kana wa mu Galileya; ndipo amake wa Yesu anali komweko.

2 Ndipo Yesu yemwe ndiophunziraake anaitanidwa kuukwatiwo.

3 Ndipo pakutha vinyo, amake wa Yesu ananena naye, Alibe vinyo.

4 Yesu nanena naye, Mkazi, ndili ndi chiyani ndi inu? Nthawi yanga siinafike.

5 Amake ananena kwa atumiki, Chimene chilichonse akanena kwa inu, chitani.

6 Ndipo panali pamenepo mitsuko yamiyala isanu ndi umodzi yoikidwako monga mwa mayeretsedwe a Ayuda, yonse ya miyeso iwiri kapena itatu.

7 Yesu ananena nao, Dzazani mitsukoyo ndi madzi. Naidzaza, ndendende.

8 Ndipo ananena nao, Tungani tsopano, mupite nao kwa mkulu wa phwando. Ndipo anapita nao.

9 Koma pamene mkuluyo analawa madzi osanduka vinyowo, ndipo sanadziwe kumene anachokera (koma atumiki amene adatunga madzi anadziwa), mkuluyo anaitana mkwati,

10 nanena naye, Munthu aliyense amayamba kuika vinyo wokoma; ndipo anthu atamwatu, pamenepo wina wosakoma; koma iwe wasunga vinyo wokoma kufikira tsopano lino.

11 Chiyambi ichi cha zizindikiro zake Yesu anachita mu Kana wa mu Galileya naonetsera ulemerero wake; ndipo ophunzira ake anakhulupirira Iye.

12 Zitapita izi anatsikira ku Kapernao, Iye ndi amake, ndi abale ake, ndi ophunzira ake; nakhala komweko masiku owerengeka.

Yesu ayeretsa Kachisi poyamba paja

13 NdipoPaskawa Ayuda unayandikira, ndipo Yesu anakwera kunka kuYerusalemu.

14 Ndipo anapeza mu Kachisi iwo akugulitsa ng’ombe ndi nkhosa ndi nkhunda, ndi akusinthana ndalama alikukhala pansi.

15 Ndipo pamene adapanga mkwapulo wazingwe, anatulutsa onse mu Kachisimo, ndi nkhosa ndi ng’ombe; nakhuthula ndalama za osinthanawo, nagubuduza magome;

16 nati kwa iwo akugulitsa nkhunda, Chotsani izi muno; musamayesa nyumba ya Atate wanga nyumba ya malonda.

17 Ophunzira ake anakumbukira kuti kunalembedwa, Changu cha pa nyumba yanu chandidya ine.

18 Chifukwa chake Ayuda anayankha nati kwa Iye, Mutionetsera ife chizindikiro chanji, pakuti muchita izi?

19 Yesu anayankha nati kwa iwo, Pasulani Kachisi uyu, ndipo masiku atatu ndidzamuutsa.

20 Pamenepo Ayuda anati, Zaka makumi anai ndi zisanu ndi chimodzi analimkumanga Kachisiyu, kodi inu mudzamuutsa masiku atatu?

21 Koma Iye analikunena za Kachisi wa thupi lake.

22 Chifukwa chake atauka kwa akufa, ophunzira ake anakumbukira kuti ananena ichi; ndipo anakhulupirira cholemba, ndi mau amene Yesu ananena.

23 Koma pamene anali mu Yerusalemu pa Paska pachikondwerero, ambiri anakhulupirira dzina lake, pakuona zizindikiro zake zimene anachitazi.

24 Koma Yesu sanakhulupirire iwo kuti akhale nao, chifukwa Iye anadziwa anthu onse,

25 ndipo sanasowe wina achite umboni za munthu; pakuti anadziwa Iye yekha chimene chinali mwa munthu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/2-401de3e8118c949bd7ea12771518a49f.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *