Categories
YOHANE

YOHANE 15

Mpesa ndi nthambi zake

1 Ine ndine mpesa weniweni, ndipo Atate wanga ndiye wam’munda.

2 Nthambi iliyonse ya mwa Ine yosabala chipatso, aichotsa; ndi iliyonse yakubala chipatso, aisadza, kuti ikabale chipatso chochuluka.

3 Mwakhala okonzeka tsopano inu chifukwa cha mau amene ndalankhula ndi inu.

4 Khalani mwa Ine, ndi Ine mwa inu. Monga nthambi siingathe kubala chipatso pa yokha, ngati siikhala mwampesa; motere mulibe inunso ngati simukhala mwa Ine.

5 Ine ndine mpesa, inu ndinu nthambi zake: wakukhala mwa Ine, ndi Ine mwa iye, ameneyo abala chipatso chambiri; pakuti kopanda Ine simungathe kuchita kanthu.

6 Ngati wina sakhala mwa Ine, watayika kunja monga nthambi, nafota; ndipo azisonkhanitsa nazitaya kumoto, nazitentha.

7 Ngati mukhala mwa Ine, ndi mau anga akhala mwa inu, pemphani chilichonse chimene muchifuna ndipo chidzachitika kwa inu.

8 Mwa ichi alemekezedwa Atate wanga, kuti mubale chipatso chambiri; ndipo mudzakhalaophunziraanga.

9 Monga momwe Atate wandikonda Ine, Inenso ndakonda inu; khalani m’chikondi changa.

10 Ngati musunga malamulo anga mudzakhala m’chikondi changa; monga Ine ndasunga malamulo a Atate wanga, ndipo ndikhala m’chikondi chake.

11 Izi ndalankhula ndi inu, kuti chimwemwe changa chikhale mwa inu, ndi kuti chimwemwe chanu chidzale.

12 Lamulo langa ndi ili, kuti mukondane wina ndi mnzake, monga ndakonda inu.

13 Palibe munthu ali nacho chikondi choposa ichi, chakuti munthu ataya moyo wake chifukwa cha abwenzi ake.

14 Muli abwenzi anga inu, ngati muzichita zimene ndikulamulani inu.

Chiyanjano chatsopano

15 Sinditchanso inu akapolo; chifukwa kapolo sadziwa chimene mbuye wake achita; koma ndatcha inu abwenzi; chifukwa zonse zimene ndazimva kwa Atate wanga ndakudziwitsani.

16 Inu simunandisankhe Ine, koma Ine ndinakusankhani inu, ndipo ndinakuikani, kuti mukamuke inu ndi kubala chipatso, ndi kuti chipatso chanu chikhale; kuti chimene chilichonse mukapempha Atate m’dzina langa akakupatseni inu.

17 Zinthu izi ndilamula inu, kuti mukondane wina ndi mnzake.

Wokhulupirira pokhala padziko lapansi

18 Ngati dziko lapansi lida inu, mudziwa kuti lidada Ine lisanayambe kuda inu.

19 Mukadakhala a dziko lapansi, dziko lapansi likadakonda zake za lokha; koma popeza simuli a dziko lapansi, koma Ine ndinakusankhani inu mwa dziko lapansi, chifukwa cha ichi likudani inu.

20 Kumbukirani mau amene Ine ndinanena kwa inu, Kapolo sali wamkulu ndi mbuye wake. Ngati anandilondalonda Ine, adzakulondalondani inunso; ngati anasunga mau anga, adzasunga anunso.

21 Koma izi zonse adzakuchitirani chifukwa cha dzina langa, chifukwa sadziwa wondituma Ine.

22 Sindikadadza ndi kulankhula nao sakadakhala nalo tchimo; koma tsopano alibe chowiringula pa machimo ao.

23 Iye wondida Ine, adanso Atate wanga.

24 Sindikadachita mwa iwo ntchito zosachita wina, sakadakhala nalo tchimo; koma tsopano anaona, nada Ine ndi Atate wanganso.

25 Koma chitero, kuti mau olembedwa m’chilamulo chao akwaniridwe, kuti, Anandida Ine kopanda chifukwa.

Mzimu Woyera ndi ophunzira omwe adzachita umboni

26 Koma pamene wafika Nkhoswe, amene Ine ndidzamtuma kwa inu kuchokera kwa Atate, ndiye Mzimu wa choonadi, amene atuluka kwa Atate, Iyeyu adzandichitira Ine umboni.

27 Ndipo inunso muchita umboni, pakuti muli ndi Ine kuyambira chiyambi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JHN/15-f08f4f9e4665b53fdfb7ae3efac92b5f.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *