Categories
YOBU

YOBU 26

Yobu atsutsa Bilidadi kuti sanamthandize; yekha nalemekeza ukulu wa Mulungu

1 Koma Yobu anayankha, nati,

2 Wamthandiza bwanji wopanda mphamvu.

Kulipulumutsa dzanja losalimba!

3 Wampangira bwanji wopanda nzeruyu!

Ndi kudziwitsa nzeru zenizeni mochuluka!

4 Wafotokozera yani mau?

Ndi mzimu wa yani unatuluka mwa iwe?

5 Adafawo anjenjemera

pansi pamadzi ndi zokhalamo.

6 Kumanda kuli padagu pamaso pake,

ndi kuchionongeko kusowa chophimbako.

7 Ayala kumpoto popanda kanthu,

nalenjeka dziko pachabe.

8 Amanga madzi m’mitambo yake yochindikira;

ndi mtambo sung’ambika pansi pake.

9 Atchingira pa mpando wake wachifumu,

nayalapo mtambo wake.

10 Analembera madziwo malire,

mpaka polekeza kuunika ndi mdima.

11 Mizati ya thambo injenjemera,

ndi kudabwa pa kudzudzula kwake.

12 Mwa mphamvu yake agwetsa nyanja bata;

ndipo mwa luntha lake akantha kudzikuza kwake.

13 Mwa mzimu wake anyezimiritsa thambo;

dzanja lake linapyoza njoka yothawayo.

14 Taonani, awa ndi malekezero a njira zake;

ndi chimene tikumva za Iye ndi chinong’onezo chaching’ono;

koma kugunda kwa mphamvu yake akuzindikiritsa ndani?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/26-db742895a2bb224dcb871d6449c6d54e.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *