Bilidadi akuti munthu sayenera kudziyesa wolungama pamaso pa Mulungu
1 Pamenepo Bilidadi wa ku Suki anayankha, nati,
2 Kulamulira ndi kuopsa kuli ndi Iye;
achita mtendere pa zam’mwamba zake.
3 Ngati awerengedwa makamu ake?
Ndipo ndaniyo, kuunika kwake sikumtulukira?
4 Potero munthu akhala bwanji wolungama kwa Mulungu?
Kapena wobadwa ndi mkazi akhala woyera bwanji?
5 Taonani, ngakhale mwezi ulibe kuwala;
ndi nyenyezi siziyera pamaso pake;
6 kopambana kotani nanga munthu, ndiye mphutsi!
Ndi wobadwa ndi munthu, ndiye nyongolotsi!
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/25-f6bb25ba6efb11ddaf8650d6fe9dea13.mp3?version_id=1068—