Categories
YOBU

YOBU 24

1 Wamphamvuyonse alekeranji kuikiratu nyengo?

Ndi iwo omdziwa alekeranji kudziwa masiku ake?

2 Alipo akusendeza malire;

alanda gulu la zoweta, nazidyetsa.

3 Akankhizira kwao bulu wa amasiye,

atenga ng’ombe ya mfedwa ikhale chikole.

4 Apatukitsa aumphawi m’njira;

osauka a padziko abisala pamodzi.

5 Taonani, ngati mbidzi za m’chipululu

atulukira kuntchito zao, nalawirira nkufuna chakudya;

chipululu chiwaonetsera chakudya cha ana ao.

6 Atema dzinthu zao m’munda;

natola khunkha m’munda wampesa wa woipa.

7 Agona amaliseche usiku wonse opanda chovala,

alibe chofunda pachisanu.

8 Avumbwa ndi mvula kumapiri,

nafukata thanthwe posowa pousapo.

9 Akwatula wamasiye kubere,

natenga chikole chovala cha osauka;

10 momwemo ayenda amaliseche opanda chovala,

nasenza mtolo wa dzinthu ali ndi njala.

11 M’kati mwa malinga a iwo aja ayenga mafuta;

aponda mphesa moponderamo, namva ludzu.

12 M’mzinda waukulu anthu abuula alinkufa;

ndi moyo wa iwo olasidwa ufuula;

koma Mulungu sasamalira choipacho.

13 Iwo ndiwo amene apikisana nako kuunika,

sadziwa njira zake, Sasunga mayendedwe ake.

14 Kukacha auka wambanda, napha wosauka ndi waumphawi;

ndi usiku asanduka mbala.

15 Ndipo diso la wachigololo liyembekezera chisisira,

ndi kuti, Palibe diso lidzandiona;

navala chophimba pankhope pake.

16 Kuli mdima aboola nyumba,

usana adzitsekera,

osadziwa kuunika.

17 Pakuti iwo onse auyesa m’mawa mthunzi wa imfa;

pakuti adziwa zoopsa za mthunzi wa imfa.

18 Atengedwa ngati choyandama pamadzi;

gawo lao litembereredwa padziko;

sadzalunjikanso njira ya minda yampesa.

19 Chilala ndi dzuwa zitha madzi a chipale chofewa,

momwemo manda achita nao ochimwa.

20 M’mimba mudzamuiwala;

mphutsi zidzamudya mokondwera.

Sadzamkumbukiranso;

ndipo chosalungama chidzathyoledwa ngati mtengo.

21 Alusira chumba wosabala,

osamchitira wamasiye chokoma.

22 Mulungu awakhalitsa amphamvu mwa mphamvu yake;

iwo aukanso m’mene anayesa kuti sadzakhala ndi moyo.

23 Awalola akhale osatekeseka, ndipo alimbikapo;

koma maso ake ali panjira zao.

24 Akwezeka; m’kamphindi kuli zii;

inde atsitsidwa, achotsedwa monga ena onse,

adulidwa ngati tirigu ngala zake.

25 Ndipo ngati si kutero, anditsutsa ndani kuti ndili wabodza,

ndi kuyesa mau anga opanda pake?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JOB/24-0ebef2528ceab784f33c50d5003ebd31.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *