Categories
YESAYA

YESAYA 64

1 Mwenzi mutang’amba kumwamba ndi kutsikira pansi, kuti mapiri agwedezeke pamaso panu;

2 monga pamene moto uyatsa zitsamba, ndi moto uwiritsa madzi; kudziwitsa kwa amaliwongo anu dzina lanu, kutiamitunduanthunthumire pamaso panu.

3 Pamene Inu munachita zinthu zoopsa, zimene ife sitinayang’anira, Inu munatsika, mapiri anagwedezeka pamaso panu.

4 Pakuti kuyambira kale anthu sanamve pena kumvetsa ndi khutu, ngakhale diso silinaone Mulungu wina popanda Inu, amene amgwirira ntchito iye amene amlindirira Iye.

5 Inu mukomana ndi iye amene akondwerera, nachita chilungamo, iwo amene akumbukira Inu m’njira zanu; taonani Inu munakwiya, ndipo ife tinachimwa; takhala momwemo nthawi yambiri, kodi tidzapulumutsidwa?

6 Pakuti ife tonse takhala ngati wina amene ali wosakonzeka; ndi zolungama zathu zonse zili ngati chovala chodetsedwa; ndipo ife tonse tifota monga tsamba, ndi zoipa zathu zitiuluza monga mphepo.

7 Ndipo palibe amene aitana dzina lanu, amene adzikakamiza yekha kugwiritsa Inu; pakuti Inu mwatibisira nkhope yanu, ndipo mwatinyeketsa ndi zoipa zathu.

8 Koma tsopano, Yehova, Inu ndinu Atate wathu; ife tili dongo, ndipo Inu ndinu Muumbi wathu; ndipo ife tonse tili ntchito ya dzanja lanu.

9 Musakwiye kopambana, Yehova, musakumbukire zoipa nthawi zonse; taonani, yang’anani ife, tikupembedzani Inu, ife tonse tili anthu anu.

10 Mizinda yanu yopatulika yasanduka chipululu,Ziyoniwasanduka chipululu,Yerusalemuwasanduka bwinja.

11 Nyumba yathu yopatulika ndi yokongola, m’mene makolo athu anakutamandani Inu, yatenthedwa ndi moto; ndi zinthu zathu zonse zokondweretsa zapasuka.

12 Kodi mudzadziletsa pa zinthuzi, Yehova? Kodi Inu mudzakhala chete ndi kutivutitsa ife zolimba?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/64-4fcfcf02b1855f41d807edad8c8cc4db.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *