Categories
YESAYA

YESAYA 6

Masomphenya a Yesaya

1 Chaka chimene mfumu Uziya anafa, ndinaona Ambuye atakhala pa mpando wachifumu wautali, ndi wotukulidwa, ndi zovala zake zinadzala mu Kachisi.

2 Pamwamba pa Iye panaima aserafi; yense anali ndi mapiko asanu ndi limodzi; awiri anaphimba nao nkhope yake, awiri naphimba nao mapazi ake, awiri nauluka nao.

3 Ndipo wina anafuula kwa mnzake, nati, Woyera, Woyera, Woyera, Yehova wa makamu; dziko lonse lapansi ladzala ulemerero wake.

4 Ndipo maziko a ziundo anasunthika ndi mau amene anafuula, ndipo nyumba inadzazidwa ndi utsi.

5 Ndipo ine ndinati, Tsoka kwa ine! Chifukwa ndathedwa; chifukwa ndili munthu wa milomo yonyansa, ndikhala pakati pa anthu a milomo yonyansa; chifukwa kuti maso anga aona Mfumu, Yehova wa makamu.

Yesaya akonzedwa akhale mneneri

6 Pompo anaulukira kwa ine mmodzi wa aserafi, ali nalo khala lamoto m’dzanja mwake, limene analichotsa ndi mbaniro paguwa la nsembe;

7 nakhudza nalo kukamwa kwanga nati, Taona ichi chakhudza milomo yako; ndipo mphulupulu zako zachotsedwa, zochimwa zako zaomboledwa.

8 Ndipo ndinamva mau a Ambuye akuti, Ndidzatumiza yani, ndipo ndani adzatimukira ife? Ndipo ine ndinati, Ndine pano; munditumize ine.

9 Ndipo Iye anati, Kauze anthu awa, Imvani inu ndithu, koma osazindikira; yang’anani inu ndithu, koma osadziwitsa.

10 Nenepetsa mtima wa anthu awa, lemeretsa makutu ao, nutseke maso ao; angaone ndi maso ao, angamve ndi makutu ao, angazindikire ndi mtima wao, nakabwerenso, nachiritsidwe.

11 Pompo ndinati ine, Ambuye mpaka liti? Ndipo anayankha, Mpaka mizinda ikhala bwinja, yopanda wokhalamo, ndi nyumba zopanda munthu, ndi dziko likhala bwinja ndithu,

12 ndipo Yehova wasunthira anthu kutali, ndi mabwinja adzachuluka pakati padziko.

13 Ndipo likatsala limodzi la magawo khumi m’menemo, lidzadyedwanso; monga kachere, ndi monganso thundu, imene tsinde lake likhalabe ataigwetsa; chotero mbeu yopatulika ndiyo tsinde lake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/6-b492e6e88ad14ff2d3e138b46f065721.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *