Awulula zoipa za mtundu wao
1 Taonani, mkono wa Yehova sufupika, kuti sungathe kupulumutsa; khutu lake silili logontha, kuti silingamve;
2 koma zoipa zanu zakulekanitsani inu ndi Mulungu wanu; ndipo machimo anu abisa nkhope yake kwa inu, kuti Iye sakumva.
3 Pakuti manja anu adetsedwa ndi mwazi, ndi zala zanu ndi mphulupulu, milomo yanu yanena zonama, lilime lanu lilankhula moipa.
4 Palibe wotulutsa mlandu molungama, ndipo palibe wonena zoona; iwo akhulupirira mwachabe, nanena zonama; iwo atenga kusaweruzika ndi kubala mphulupulu.
5 Iwo afungatira mazira a mphiri aswetse, naluka ukonde wa kangaude; iye amene adya mazira ake amafa, ndi choswanyikacho chisweka ndipo chikhala songo.
6 Maukonde ao sadzakhala zovala, sadzafunda ntchito zao; ntchito zao zili ntchito zoipa, ndi chiwawa chili m’manja mwao.
7 Mapazi ao athamangira koipa, ndipo iwo afulumira kukhetsa mwazi wosachimwa; maganizo ao ali maganizo oipa; bwinja ndi chipasuko zili m’njira mwao.
8 Njira ya mtendere saidziwa, ndipo palibe chiweruziro m’mayendedwe mwao; akhotetsa njira zao; aliyense ayenda m’menemo sadziwa mtendere.
9 Chifukwa chake chiweruziro chili patali ndi ife, ndi chilungamo sichitipeza; tiyang’anira kuunika, koma taona mdima; tiyang’anira kuyera, koma tiyenda mu usiku.
10 Tiyambasira khoma ngati wakhungu, inde tiyambasa monga iwo opanda maso; tiphunthwa usana monga m’chizirezire; tili m’malo amdima ngati akufa.
11 Tonse tibangula ngati zilombo, ndi kulira maliro zolimba ngati nkhunda; tiyang’anira chiweruziro koma palibe; tiyang’anira chipulumutso koma chili patali ndi ife.
12 Pakuti zolakwa zathu zachuluka pamaso pa Inu, ndipo machimo athu atineneza ife; pakuti zolakwa zathu zili ndi ife, ndipo zoipa zathu tizidziwa;
13 ndizo kulakwabe ndi kukanabe Yehova, ndi kuleka kutsata Mulungu wathu; kulankhula zotsendereza ndi kupanduka, kuganizira ndi kunena pakamwa mau akunyenga otuluka mumtima.
14 Ndipo chiweruziro chabwerera m’mbuyo, ndi chilungamo chaima patali; pakuti choona chagwa m’khwalala, ndi kuongoka sikungalowe.
15 Inde choona chisoweka; iye amene asiya choipa, zifunkhidwa zake; ndipo Yehova anaona ichi, ndipo chidamuipira kuti palibe chiweruzo.
16 Ndipo Iye anaona kuti palibe munthu, nazizwa kuti palibe wopembedzera; chifukwa chake mkono wakewake unadzitengera yekha chipulumutso; ndi chilungamo chake chinamchirikiza.
17 Ndipo anavala chilungamo monga chida chapachifuwa, ndi chisoti cha chipulumutso pamutu pake; navala zovala zakubwezera chilango, navekedwa ndi changu monga chofunda.
18 Monga mwa ntchito zao momwemo Iye adzabwezera amaliwongo ake ukali, nadzabwezera adani ake chilango; nadzabwezeranso zisumbu chilango.
19 Chomwecho iwo adzaopa dzina la Yehova kuchokera kumadzulo, ndi ulemerero wake kumene kutulukira dzuwa; pakuti pamene mdani adzafika ngati chigumula, mzimu wa Yehova udzamkwezera mbendera yomletsa.
20 Ndipo Mombolo adzafika kuZiyoni, ndi kwa iwo amene atembenuka kusiya kulakwa mwa Yakobo, ati Yehova.
21 Ndipo kunena za Ine, ili ndi pangano langa ndi iwo, ati Yehova; mzimu wanga umene uli pa iwe, ndi mau anga amene ndaika m’kamwa mwako sadzachoka m’kamwa mwako, pena m’kamwa mwa ana ako, pena m’kamwa mwa mbeu ya mbeu yako, ati Yehova, kuyambira tsopano ndi kunthawi zonse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/59-76712e71107972788eaa66d4748a0c8f.mp3?version_id=1068—