Yehova yekha ndiye Mulungu, Israele amkhulupirire Iye yekhayekha
1 Khalani chete pamaso pa Ine, zisumbu inu, anthu atengenso mphamvu; ayandikire; pamenepo alankhule; tiyeni tiyandikire pamodzi kuchiweruziro.
2 Ndani anautsa wina wochokera kum’mawa, amene amuitana m’chilungamo, afike pa phazi lake? Iye aperekaamitundupatsogolo pake, namlamuliritsa mafumu; nawapereka monga fumbi kulupanga lake, monga chiputu chouluzidwa ku uta wake.
3 Iye awathamangitsa, napitirira mwamtendere; panjira imene asanapitemo ndi mapazi ake.
4 Ndani wachipanga, nachimaliza icho, kutchula mibadwo chiyambire? Ine Yehova, ndine woyamba, ndi pachimaliziro ndine ndemwe.
5 Zisumbu zinaona ndipo zinaopa; malekezero a dziko lapansi ananthunthumira; anayandikira, nafika.
6 Iwo anathangata yense mnansi wake, ndi yense anati kwa mbale wake, Khala wolimba mtima.
7 Chotero mmisiri wa mitengo analimbikitsa wosula golide, ndi iye amene asalaza ndi nyundo anamlimbikitsa iye amene amenya posulira, nanena za kulumikiza ndi ntovu, Kuli kwabwino; ndipo iye akhomera fanolo misomali kuti lisasunthike.
8 Koma iwe, Israele, mtumiki wanga, Yakobo, amene ndinakusankha, mbeu ya Abrahamu bwenzi langa;
9 iwe amene ndinakuwira iwe zolimba kuchokera ku malekezero a dziko lapansi, ndi kukuitana iwe kuchokera m’ngodya zake, ndipo ndinati kwa iwe, Ndiwe mtumiki wanga ndakusankha, sindinakutaye kunja;
10 usaope, pakuti Ine ndili pamodzi ndi iwe; usaopsedwe, pakuti Ine ndine Mulungu wako; ndidzakulimbitsa; inde, ndidzakuthangata; inde, ndidzakuchirikiza ndi dzanja langa lamanja la chilungamo.
11 Taona, onse amene akukwiyira iwe adzakhala ndi manyazi, nasokonezedwa; iwo amene akangana ndi iwe adzakhala ngati chabe, nadzaonongeka.
12 Iwe udzawafuna osawapeza, ngakhale iwo amene akangana ndi iwe; ochita nkhondo ndi iwe, adzakhala ngati chabe, ndi monga kanthu kopanda pake.
13 Pakuti Ine Yehova Mulungu wako ndidzagwira dzanja lako lamanja, ndi kunena kwa iwe, Usaope ndidzakuthandiza iwe.
14 Usaope, Yakobo, nyongolotsi iwe, ndi anthu inu a Israele; ndidzakuthangata iwe, ati Yehova, ndiye Mombolo wako, Woyera wa Israele.
15 Taona, ndidzakuyesa iwe choombera tirigu chatsopano chakuthwa chokhala ndi mano; iwe udzaomba mapiri ndi kuwapera asalale, ndi kusandutsa zitunda mungu.
16 Iwe udzawapeta, ndi mphepo idzawauluza; ndipo kamvulumvulu adzawamwaza; ndipo iwe udzasangalala mwa Yehova, udzadzikuza mwa Woyera wa Israele.
17 Wosauka ndi wosowa afuna madzi, ndipo palibe, ndi lilime lao lilephera, chifukwa cha ludzu; Ine Yehova ndidzawayankha, Ine Mulungu wa Israele sindidzawasiya.
18 Ndidzagwetsa mitsinje pazitunda zoti see, ndi akasupe pakati pa zigwa; ndidzasandutsa chipululu, chikhale thamanda lamadzi, ndi mtunda wouma ukhale magwero a madzi.
19 Ndidzabzala m’chipululu mkungudza, ndi msangu, ndi kasiya, ndi mtengo waazitona; ndidzaika m’chipululu pamodzi mlombwa, ndi mkuyu, ndi naphini;
20 kuti iwo aone ndi kudziwa, ndi kulingalira, ndi kumvetsa pamodzi, kuti dzanja la Yehova lachita ichi, ndipo Woyera wa Israele wachilenga ichi.
21 Onetsani mlandu wanu, ati Yehova; tulutsani zifukwa zanu zolimba, ati mfumu ya Yakobo.
22 Azitulutse, atitchulire ife, chimene chidzaoneka; tchulani inu zinthu zakale, zinali zotani, kuti ife tiganizire pamenepo, ndi kudziwa mamaliziro ao; kapena tionetseni ife zinthu zimene zilinkudza.
23 Tchulani zinthu zimene zilinkudza m’tsogolo, kuti ife tidziwe kuti inu ndinu milungu; inde, chitani zabwino, kapena chitani zoipa, kuti ife tiopsedwe, ndi kuona pamodzi.
24 Taonani, inu muli achabe, ndi ntchito yanu yachabe; wonyansa ali iye amene asankha inu.
25 Ndautsa wina wakuchokera kumpoto; ndipo iye wafika wakuchokera potuluka dzuwa, amene atchula dzina langa; ndipo iye adzafika pa olamulira, monga matope, ndi monga muumbi aponda dothi la mbiya.
26 Ndani watchula icho chiyambire, kuti ife tichidziwe? Ndi nthawi zakale, kuti ife tinene, Iye ali wolungama? Inde, palibe wina amene atchula, inde, palibe wina amene asonyeza, inde palibe wina amene amvetsa mau anu.
27 Poyamba Ine ndidzati kwaZiyoni, Taona, taona iwo; ndipo ndidzapereka kwaYerusalemuwina, amene adza ndi mau abwino.
28 Ndipo pamene ndayang’ana, palibe munthu; ngakhale mwa iwo, palibe phungu, amene angathe kuyankha mau, pamene ndiwafunsa.
29 Taona, iwo onse, ntchito zao zikhala zopanda pake ndi zachabe; mafano ao osungunula ndiwo mphepo ndi masokonezo.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/41-70ae944896603c7438991f50b02c861b.mp3?version_id=1068—