Categories
YESAYA

YESAYA 40

Lonjezo la chipulumutso cha Israele

1 Mutonthoze, mutonthoze mtima wa anthu anga, ati Mulungu wanu.

2 Munene inu zotonthoza mtima kwaYerusalemu, nimufuulire kwa iye, kuti nkhondo yake yatha, kuti kuipa kwake kwakhululukidwa; kuti iye walandira mowirikiza m’dzanja la Yehova, chifukwa cha machimo ake onse.

3 Mau a wofuula m’chipululu, Konzani njira ya Yehova, lungamitsani m’dziko loti see khwalala la Mulungu wathu.

4 Chigwa chilichonse chidzadzazidwa, ndipo phiri lililonse ndi chitunda chilichonse zidzachepetsedwa, ndipo zokhota zidzaongoledwa, ndipo zamakolokoto zidzasalala;

5 ndipo ulemerero wa Yehova udzavumbulutsidwa, ndipo anthu onse adzauona pamodzi, pakuti pakamwa pa Yehova panena chomwecho.

6 Mau a wina ati, Fuula. Ndipo ndinati, Kodi ndifuule chiyani? Anthu onse ndi udzu, ndi kukoma kwao konse kunga duwa la m’thengo;

7 udzu unyala, duwa lifota; chifukwa mpweya wa Yehova waombapo; zoonadi anthu ndi udzu.

8 Udzu unyala, duwa lifota, koma mau a Mulungu wathu adzakhala nthawi zachikhalire.

9 Iwe amene utengera mau abwino kuZiyoni, kwera iwe pamwamba paphiri lalitali; iwe amene utengera mau abwino ku Yerusalemu, kweza mau ako ndi mphamvu, kwezetsa usaope, nena kumizinda ya Yuda, Taonani, Mulungu wanu!

10 Taonani, Ambuye Yehova adzadza ngati wamphamvu, ndipo mkono wake udzalamulira; taonani, mphotho yake ili ndi Iye, ndipo chobwezera chake chili patsogolo pa Iye.

11 Iye adzadyetsa zoweta zake ngati mbusa, nadzasonkhanitsa anaankhosa m’manja mwake, nadzawatengera pa chifuwa chake, ndipo adzatsogolera bwinobwino zimene ziyamwitsa.

Mulungu ndi wamphamvuyonse, mafano ndi achabe

12 Ndani wayesa madzi m’dzanja lake, nayesa thambo ndi chikhato, ndi kudzaza fumbi la nthaka m’nsengwa, ndi kuyesa mapiri m’mbale zoyesera, ndi zitunda m’mulingo?

13 Ndani anapangira mzimu wa Yehova, kapena kukhala phungu lake, ndi kumphunzitsa Iye?

14 Iye anakhala upo ndi yani, ndipo ndani analangiza Iye ndi kumphunzitsa m’njira ya chiweruzo, ndi kumphunzitsa nzeru ndi kumuonetsa njira ya luntha?

15 Taonani,amitunduakunga dontho la m’mtsuko, nawerengedwa ngati fumbi losalala la m’muyeso; taonani atukula zisumbu ngati kanthu kakang’ono.

16 Ndipo Lebanoni sakwanira kutentha, ngakhale nyama zake sizikwanira nsembe yopsereza.

17 Amitundu onse ali chabe pamaso pa Iye; awayesa ngati chinthu chachabe, ndi chopanda pake.

18 Mudzafanizira Mulungu ndi yani tsopano, kapena kumyerekeza ndi chithunzithunzi chotani?

19 Fano losema mmisiri analisungunula, ndipo wosula golide analikuta ndi golide, naliyengera maunyolo asiliva.

20 Wosowa nsembe yoteroyo asankha mtengo umene sungavunde, iye adzisankhira yekha munthu mmisiri waluso, akonze fano losema, limene silisunthika.

21 Kodi inu simunadziwe? Kodi inu simunamve? Kodi sanakuuzeni inu chiyambire? Kodi inu simunadziwitse chiyambire mayambiro a dziko lapansi?

22 Ndi Iye amene akhala pamwamba pa malekezero a dziko lapansi, ndipo okhalamo akunga ziwala; amene afutukula thambo ngati chinsalu, naliyala monga hema wakukhalamo;

23 amene asandutsa akalonga kuti akhale achabe, nasandutsa oweruza a dziko lapansi akhale opanda pake.

24 Inde sanaokedwe, inde sanafesedwe; inde, muzu wao sunazike pansi; koma Iye anawaombetsera mphepo, ndipo afota, ndipo kamvulumvulu awachotsa monga chiputu.

25 Mudzandifanizira Ine ndi yani tsono, kuti ndilingane naye, ati Woyerayo.

26 Kwezani maso anu kumwamba, muone amene analenga izo, amene atulutsa khamu lao ndi kuziwerenga; azitcha zonse maina ao, ndi mphamvu zake zazikulu, ndi popeza ali wolimba mphamvu, palibe imodzi isoweka.

27 Bwanji iwe, Yakobo, umati, ndi bwanji umanena iwe, Israele, Njira yanga yabisika kwa Yehova; ndipo chiweruzo cha Mulungu wanga chandipitirira?

28 Kodi iwe sunadziwe? Kodi sunamve? Mulungu wachikhalire, Yehova, Mlengi wa malekezero a dziko lapansi, salefuka konse, salema; nzeru zake sizisanthulika.

29 Iye alimbitsa olefuka, naonjezera mphamvu iye ameme alibe mphamvu.

30 Ngakhale anyamata adzalefuka ndi kulema ndi amisinkhu adzagwa ndithu:

31 koma iwo amene alindira Yehova adzatenganso mphamvu; adzauluka pamwamba ndi mapiko monga ziombankhanga; adzathamanga koma osalema; adzayenda koma osalefuka.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/40-06c7b9729727923956d9c325b3ee5a65.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *