Categories
YESAYA

YESAYA 4

Tsiku la Mulungu, kuyeretsedwa kwa Yerusalemu

1 Ndipo akazi asanu ndi awiri adzagwira mwamuna mmodzi tsiku limenelo, nati, Ife tidzadya chakudya chathuchathu ndi kuvala zovala zathuzathu; koma titchedwe dzina lako; chotsa chitonzo chathu.

2 Tsiku limenelo mphukira ya Yehova idzakhala yokongola ndi ya ulemerero, chipatso cha nthaka chidzakhala chokometsetsa ndi chokongola, kwa iwo amene adzapulumuka a Israele.

3 Ndipo padzakhala, kuti iye amene asiyidwa muZiyoni, ndi iye amene atsala muYerusalemuadzatchedwa woyera; ngakhale yense amene walembedwa mwa amoyo mu Yerusalemu;

4 pamene Ambuye adzasambitsa litsiro la ana aakazi a Ziyoni, nadzatsuka mwazi wa Yerusalemu, kuchokera pakatipo, ndi mzimu wa chiweruziro, ndi mzimu wakutentha.

5 Ndipo Yehova adzalenga pokhala ponse paphiri la Ziyoni, ndi pa misonkhano yake, mtambo ndi utsi usana, ndi kung’azimira kwa malawi a moto usiku; chifukwa kuti pa ulemerero wonse padzayalidwa chophimba.

6 Ndipo padzakhala chihema cha mthunzi, nthawi ya usana yopewera kutentha, pothawira ndi pousa mvula ndi mphepo.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/4-5a266abaab2ef364b095e3a844987b45.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *