Categories
YESAYA

YESAYA 3

1 Ndipo onani, Ambuye, Yehova wa makamu, wachotsa kuYerusalemundi ku Yuda mchirikizo wochirikiza chakudya chonse ndi madzi onse, zimene zinali mchirikizo;

2 munthu wamphamvu, ndi munthu wankhondo; woweruza ndimneneri, ndi waula, ndi nkhalamba;

3 kapitao wa makumi asanu, ndi munthu wolemekezeka, ndi phungu, ndi mmisiri waluso, ndi wodziwa matsenga.

4 Ndipo ndidzapereka ana, kuti akhale akulu ao, mwachibwana adzawalamulira.

5 Ndi anthu adzavutidwa, yense ndi wina, yense ndi mnansi wake; mwana adzadzinyaditsa yekha pa akulu, ndi onyozeka pa olemekezedwa.

6 Pamene mwamuna adzamgwira mbale wake m’nyumba ya atate wake, nadzati, Iwe uli ndi chovala, khala wolamulira wathu, ndi kupasula kumeneku kukhale m’dzanja lako;

7 tsiku limenelo adzakweza mau ake, kuti, Sindine wochiritsa, chifukwa kuti m’nyumba mwanga mulibe chakudya kapena chovala; inu simudzandiyesa ine wolamulira anthu.

8 Chifukwa kuti Yerusalemu wapasulidwa, ndi Yuda wagwa; chifukwa kuti lilime lao ndi machitidwe ao akana Yehova, kuti autse mkwiyo wa m’maso a ulemerero wake.

9 Maonekedwe a nkhope zao awachitira iwo mboni; ndipo amaonetsa uchimo wao monga Sodomu, saubisa. Tsoka kwa moyo wao! Chifukwa iwo anadzichitira zoipa iwo okha.

10 Nenani za wolungama, kuti kudzamkomera iye; chifukwa oterowo adzadya zipatso za machitidwe ao.

11 Tsoka kwa woipa! Kudzamuipira; chifukwa kuti mphotho ya manja ake idzapatsidwa kwa iye.

12 Anthu anga awavuta ndi ana, awalamulira ndi akazi. Anthu anga inu, iwo amene akutsogolerani, ndiwo akuchimwitsani, naononga njira zanu zoyendamo.

13 Yehova aimirira kuti atsutsane, naimiriranso kuti aweruze mitundu ya anthu.

14 Yehova adzalowa m’bwalo la milandu ndi okalamba a anthu ake, ndi akulu ake: Ndinu amene mwadya munda wampesa, zofunkha za waumphawi zili m’nyumba zanu;

15 muti bwanji inu, amene mupsinja anthu anga, ndi kupera nkhope ya wosauka? Ati Ambuye, Yehova wa makamu.

16 Komanso Yehova ati, Chifukwa kuti ana aakazi aZiyoniangodzikuza atakweza makosi ao, ndi maso ao adama nayenda nanyang’ama poyenda pao naliza zigwinjiri za mapazi ao;

17 chifukwa chake Ambuye adzachita nkanambo pa liwombo la ana aakazi a Ziyoni, ndipo Yehova adzavundukula m’chuuno mwao.

18 Tsiku limenelo Ambuye adzachotsa zigwinjiri zao zokoma, ndi zitunga, ndi mphande;

19 mbera, ndi makoza, ndi nsalu za pankhope;

20 ndi zisada, ndi maunyolo a kumwendo, ndi mipango, ndi nsupa zonunkhira, ndi mphinjiri;

21 mphete, ndi zipini;

22 malaya a paphwando, ndi zofunda, ndi zimbwi, ndi timatumba;

23 akalirole, ndi nsalu zabafuta, ndi nduwira, ndi zophimba.

24 Ndipo padzakhala m’malo mwa zonunkhiritsa mudzakhala zovunda; ndi m’malo mwa lamba chingwe; ndipo m’malo mwa tsitsi labwino dazi; m’malo mwa chovala chapachifuwa mpango wachiguduli; zipsera m’malo mwa ukoma.

25 Amuna ako adzagwa ndi lupanga, ndi wamphamvu wako m’nkhondo.

26 Ndipo zipata zake zidzalira maliro; ndipo iye adzakhala bwinja, nadzakhala pansi.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/3-0f0fea617de1baa0146875a316f43ade.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *