Nyimbo yakulemekeza chifundo cha Mulungu
1 Yehova, Inu ndinu Mulungu wanga, ndidzakukuzani Inu, ndidzatamanda dzina lanu, chifukwa mwachita zinthu zodabwitsa, ngakhale zauphungu zakale, mokhulupirika ndi m’zoonadi.
2 Chifukwa Inu mwasandutsa mzinda muunda; mzinda walinga bwinja; nyumba ya alendo kuti isakhale mzinda; sudzamangidwa konse.
3 Chifukwa chake anthu amphamvu adzakulemekezani Inu, mzinda wa mitundu yakuopsa udzakuopani Inu.
4 Chifukwa Inu mwakhala linga la aumphawi, linga la osowa m’kuvutidwa kwake, pobisalira chimphepo, mthunzi wa pa dzuwa, pamene kuomba kwa akuopsa kufanana ndi chimphepo chakuomba tchemba.
5 Monga kutentha m’malo ouma, Inu mudzaletsa phokoso la alendo; nyimbo ya akuopsa idzaletseka, monga mthunzi uletsa dzuwa.
6 Ndipo m’phiri limeneli Yehova wa makamu adzakonzera anthu ake onse phwando la zinthu zonona, phwando la vinyo wa pamitsokwe, la zinthu zonona za mafuta okhaokha, la vinyo wansenga wokuntha bwino.
7 Ndipo Iye adzaononga m’phiri limeneli chophimba nkhope chovundikira mitundu yonse ya anthu, ndi nsalu yokutaamitunduonse.
8 Iye wameza imfa kunthawi yonse; ndipo Ambuye Mulungu adzapukuta misozi pa nkhope zonse; ndipo chitonzo cha anthu ake adzachichotsa padziko lonse lapansi; chifukwa Yehova wanena.
9 Ndipo adzanena tsiku limenelo, Taonani, uyu ndiye Mulungu wathu; tamlindirira Iye, adzatipulumutsa; uyu ndiye Yehova, tamlindirira Iye, tidzakondwa ndi kusekerera m’chipulumutso chake.
10 Chifukwa m’phiri limeneli dzanja la Yehova lidzakhalamo, ndipo Mowabu adzaponderezedwa pansi m’malo ake, monga udzu uponderezedwa padzala.
11 Ndipo iye adzatambasula manja ake pakati pamenepo, monga wosambira atambasula manja ake posambira; koma Iye adzagwetsa pansi kunyada kwake, pamodzi ndi kunyenga kwa manja ake.
12 Ndipo linga la pamsanje la machemba ako Iye waligwetsa, naligonetsa pansi, nalifikitsa padothi, ngakhale pafumbi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/25-416977ead7ae23b08dab2880ac5803c0.mp3?version_id=1068—