Categories
YESAYA

YESAYA 24

Chilango cha Mulungu cha padziko la Israele, ndi padziko lonse lapansi

1 Taonani, Yehova apululutsa dziko, nalipasula, nalitembenuza dodolido, nabalalitsa okhalamo ake.

2 Ndipo padzakhala monga ndi anthu, moteronso ndi ansembe; monga ndi mtumiki, moteronso ndi mbuyake; monga ndi mdzakazi, moteronso ndi mbuyake wamkazi; monga ndi wogula, moteronso ndi wogulitsa; monga ndi wobwereka, moteronso ndi wombwereka; monga ndi wotenga phindu, moteronso ndi wombwezera phindu kwa iye.

3 Dziko lidzapululuka konse, ndi kupasulidwa ndithu; pakuti Yehova anenana mau amenewa.

4 Dziko lirira nilifota, dziko lilefuka nilifota, anthu omveka a padziko alefuka.

5 Dzikonso laipitsidwa ndi okhalamo ake omwe, chifukwa iwo alakwa pamalamulo nasinthanitsa malemba, nathyolachipanganocha nthawi zonse.

6 Chifukwa chake chitemberero chadya dziko, ndi amene akhala m’menemo apezedwa ochimwa, chifukwa chake okhalamo a padziko atenthedwa, ndipo anthu owerengeka atsala.

7 Vinyo watsopano alira, mpesa ulefuka, mitima yonse yokondwa iusa moyo.

8 Kusangalala kwa mangaka kwalekeka, phokoso la iwo amene asekera litha, kukondwa kwa mngoli kwalekeka.

9 Iwo sadzamwa vinyo ndi kuimba nyimbo; chakumwa chaukali chidzawawa kwa iwo amene achimwa.

10 Mzinda wosokonezeka wagwetsedwa pansi; nyumba zonse zatsekedwa, kuti asalowemo munthu.

11 Muli mfuu m’makwalala chifukwa cha vinyo; kukondwa konse kwadetsedwa, kusangalala kwa dziko kwatha.

12 M’mzinda mwatsala bwinja, ndi chipata chamenyedwa ndi chipasuko.

13 Chifukwa chake padzakhala chotero pakati padziko mwa anthu, ngati kugwedeza kwa mtengo waazitona, ngati khunkha la mphesa, pakutha masika ake.

14 Amenewa adzakweza mau ao, nadzafuula; chifukwa cha chifumu cha Yehova, iwo adzafuula zolimba panyanja.

15 Chifukwa chake lemekezani inu Yehova kum’mawa, ngakhale dzina la Yehova, Mulungu wa Israele, m’zisumbu za m’nyanja.

16 Kuchokera ku malekezero a dziko ife tamva nyimbo zolemekeza wolungama. Koma ine ndinati, Ndaonda ine, ndaonda ine, tsoka kwa Ine! Amalonda onyenga amangonyenga; inde ogulitsa onyenga apambana kunyenga.

17 Mantha ndi dzenje ndi msampha zili pa iwe, wokhala m’dziko.

18 Ndipo padzali, kuti iye amene athawa mbiri yoopsa, adzagwa m’dzenje; ndi iye amene atuluka m’kati mwa dzenje, adzakodwa mumsampha, pakuti mazenera a kuthambo atsegudwa, ndi maziko a dziko agwedezeka.

19 Dziko lapansi lasweka ndithu, dziko lapansi lasungunukadi, dziko lapansi lili kugwedezeka kopambana.

20 Dziko lapansi lidzachita dzandidzandi, ngati munthu woledzera, ndi kunjenjemera, ngati chilindo; ndi kulakwa kwake kudzalilemera, ndipo lidzagwa losaukanso.

21 Ndipo padzali tsiku limenelo, kuti Yehova adzazonda kumwamba khamu lakumwamba, ndi mafumu a dziko lapansi.

22 Ndipo iwo adzasonkhanitsidwa pamodzi, monga ndende zimasonkhanitsidwa m’dzenje, ndi kutsekeredwa m’kaidi, ndipo atapita masiku ambiri adzawazonda.

23 Pompo mwezi udzanyazitsidwa, ndi dzuwa lidzakhala ndi manyazi, pakuti Yehova wa makamu adzalamulira chaulemerero m’phiri laZiyoni, ndi muYerusalemu, ndi pamaso pa akuluakulu ake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/24-4102f916f0c33adcae3b5c4c5ed8d854.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *