Kupasuka ndi kumangidwanso kwa Tiro
1 Katundu wa Tiro. Kuwani, inu ngalawa za Tarisisi; chifukwa wapasudwa, kulibenso nyumba, kulibe polowera; kuchokera kudziko la Kitimu kwavumbulutsidwa kwa iwo.
2 Khalani chete, inu okhala m’chisumbu; iwe amene anakudzazanso amalonda a ku Sidoni, opita m’nyanja.
3 Ndi pa nyanja zazikulu anapindula ndi mbeu za ku Sihori ndizo dzinthu za ku mtsinje; ndi kumeneko kunali msika waamitundu.
4 Khala ndi manyazi, iwe Sidoni; chifukwa nyanja yanena, linga la kunyanja, ndi kuti, Ine sindinamve zowawa, kapena kubala, kapena kulera anyamata, kapena kulera anamwali.
5 Pofika mbiriyo ku Ejipito, iwo adzamva kuwawa kwambiri pa mbiri ya Tiro.
6 Olokani inu, kunka ku Tarisisi, kuwani, inu okhala m’chisumbu.
7 Kodi umene ndi mzinda wanu wokondwa, wachikhalire kale lomwe, umene mapazi ake anaunyamula kunka nao kutali kukhalako?
8 Ndani wapanga uphungu uno pa Tiro, mudzi umene upereka akorona, amalonda ake ali akalonga, ogulitsa ake ali olemekezeka padziko lapansi?
9 Yehova wa makamu wapanga uphungu uwu, kuipitsa kunyada kwa ulemerero wonse, kupepula onse olemekezeka a m’dziko lapansi.
10 Pita pakati padziko lako monga mtsinje, iwe mwana wamkazi wa Tarisisi; palibenso lamba.
11 Iye watambasula dzanja lake panyanja, wagwedeza maufumu; Yehova walamulira Kanani za amalonda, kupasula malinga ake.
12 Ndipo Iye anati, Iwe sudzakondwanso konse, iwe namwali wovutidwa, mwanawamkazi wa Sidoni; uka, oloka kunka ku Kitimu; ngakhale kumeneko iwe sudzapumai.
13 Taonani, dziko la Ababiloni; anthu awa sakhalanso; Asiriya analiika ilo likhale la zilombo zokhala m’chipululu; iwo amanga nsanja zao, nagumula nyumba za mafumu ake; nalipasula.
14 Kuwani, inu ngalawa za Tarisisi; pakuti linga lanu lapasulidwa.
15 Ndipo padzakhala tsiku limenelo, kuti Tiro adzaiwalika zaka makumi asanu ndi awiri, malinga ndi masiku a mfumu imodzi; zitapita zaka makumi asanu ndi ziwirizo, chidzakhala kwa Tiro monga m’nyimbo ya mkazi wadama.
16 Tenga mngoli, yendayenda m’mzinda, iwe mkazi wadama, amene unaiwalika; imba zokoma, chulukitsa nyimbo, kuti ukumbukiridwe.
17 Ndipo padzali, zitapita zaka makumi asanu ndi awirizo, kuti Yehova adzazonda Tiro, ndipo iye adzabwerera kumphotho yake, nadzachita dama ndi maufumu onse a dziko lapansi, okhala kunja kuno.
18 Malonda ake ndi mphotho yake zidzakhala zopatulikira Yehova; sizidzasungidwa kapena kuikidwa; chifukwa malonda ake adzakhala kwa iwo, amene akhala pamaso pa Yehova, kuti adye mokwana, navale chaulemu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/23-895e7408269b2504c3f0dc79c907271d.mp3?version_id=1068—