Categories
YESAYA

YESAYA 12

Chiyamiko cha anthu a Mulungu atalangidwa

1 Tsiku lomwelo udzati, Ndikuyamikani inu Yehova; pakuti ngakhale munandikwiyira, mkwiyo wanu wachoka, ndipo mutonthoza mtima wanga.

2 Taonani, Mulungu ndiye chipulumutso changa; ndidzakhulupirira, sindidzaopa; pakuti Yehova Mwini ndiye mphamvu yanga ndi nyimbo yanga, Iye ndiye chipulumutso changa.

3 Chifukwa chake mudzakondwera pakutunga madzi m’zitsime za chipulumutso.

4 Tsiku lomwelo mudzati, Muyamikire Yehova, bukitsani dzina lake, mulalikire machitidwe ake mwa mitundu ya anthu, munene kuti dzina lake lakwezedwa.

5 Muimbire Yehova; pakuti wachita zaulemerero; chidziwike ichi m’dziko lonse.

6 Tafuula, takuwa iwe, wokhala muZiyoni, chifukwa Woyera wa Israele wa m’kati mwako ali wamkulu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/ISA/12-d28253e143a6794a72cd81207ff577eb.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *