Aneneratu za chitsutso cha Afilisti
1 Mau a Yehova amene anadza kwa Yeremiyamnenerionena za Afilisti,Faraoasanakanthe Gaza.
2 Yehova atero: Taonani, madzi adzakwera kutuluka kumpoto, nadzakhala mtsinje wosefuka, nadzasefukira padziko ndi pa zonse zili m’mwemo, pamzinda ndi pa onse okhalamo; ndipo amuna adzalira, ndi onse okhala m’dziko adzakuwa.
3 Pomveka migugu ya ziboda za olimba ake, pogumukira magaleta ake, ndi pophokosera njinga zake, atate sadzacheukira ana ao chifukwa cha kulefuka kwa manja ao;
4 chifukwa cha tsiku lakudzafunkha Afilisti onse, kuphera Tiro ndi Sidoni othangata onse akutsala; pakuti Yehova adzafunkha Afilisti, otsala a chisumbu cha Kafitori.
5 Dazi lafikira a Gaza; Asikeloni wathedwa, otsala m’chidikha chao; udzadzicheka masiku angati?
6 Iwe lupanga la Yehova, atsala masiku angati osakhala chete iwe? Dzilonge wekha m’chimake; puma, nukhale chete.
7 Udzakhala chete bwanji, popeza Yehova anakulangiza? Za Asikeloni, ndi za m’mphepete mwa nyanja, pamenepo analiika.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/47-efc82fcd73fad87d54951dff763e4861.mp3?version_id=1068—