Yeremiya aponyedwa m’dzenje muli thope
1 Ndipo Sefatiya mwana wa Matani ndi Gedaliya mwana wa Pusuri, ndi Yukala mwana wa Selemiya, ndi Pasuri mwana wa Malikiya, anamva mau amene Yeremiya ananena ndi anthu onse, kuti,
2 Yehova atero, Iye wakukhala m’mzindawu adzafa ndi lupanga, ndi njala, ndi mliri; koma iye wakutulukira kunka kwa Ababiloni adzakhala ndi moyo, ndipo adzakhala nao moyo wake ngati chofunkha, nadzakhala ndi moyo.
3 Yehova atero, Mzindawu udzapatsidwatu m’dzanja la nkhondo ya mfumu ya ku Babiloni, ndipo adzaulanda.
4 Ndipo akulu anati kwa mfumu, Munthu uyu aphedwetu; chifukwa analopetsa manja a anthu a nkhondo otsala m’mzinda muno, ndi manja a anthu onse, pakunena kwa iwo mau otero; pakuti munthu uyu safuna mtendere wa anthu awa, koma nsautso yao.
5 Ndipo mfumu Zedekiya anati, Taonani, ali m’manja mwanu; pakuti mfumu singathe kuchita kanthu kotsutsana nanu.
6 Ndipo anatenga Yeremiya, namponya iye m’dzenje la Malikiya mwana wake wa mfumu, limene linali m’bwalo la kaidi; ndipo anamtsitsa Yeremiya ndi zingwe. Koma m’dzenjemo munalibe madzi, koma thope; namira Yeremiya m’thopemo.
7 Ndipo pamene Ebedemeleki Mkusi, mdindo, anamva kuti anamuika Yeremiya m’dzenje; mfumu ilikukhala pa Chipata cha Benjamini;
8 Ebedemeleki anatuluka m’nyumba ya mfumu, nanena ndi mfumu, kuti,
9 Mbuyanga mfumu, anthu awa anachita zoipa m’zonse anachitira Yeremiyamneneri, amene anamponya m’dzenje; ndipo afuna kufa m’menemo chifukwa cha njala; pakuti mulibe chakudya china m’mzindamu.
10 Ndipo mfumu inamuuza Ebedemeleki Mkusi, kuti, Tenga anthu makumi atatu, umkweze numtulutse Yeremiya mneneri m’dzenjemo, asanafe.
11 Ndipo Ebedemeleki anatenga anthuwo, nalowa nao m’nyumba ya mfumu ya pansi pa nyumba ya chuma, natenga m’menemo nsalu zakale zotaya ndi zansanza zovunda, nazitsitsira ndi zingwe kwa Yeremiya m’dzenjemo.
12 Ndipo Ebedemeleki Mkusi anati kwa Yeremiya, Kulungatu zingwe ndi nsaluzi zotaya zakale ndi zansanza ndi kuzikwapatira. Ndipo Yeremiya anachita chomwecho.
13 Ndipo anamkweza Yeremiya ndi zingwe, namtulutsa m’dzenjemo; ndipo Yeremiya anakhalabe m’bwalo la kaidi.
14 Ndipo mfumu Zedekiya anatuma, namtenga Yeremiya mneneri nalowa naye m’khomo lachitatu la nyumba ya Yehova; ndipo mfumu inati kwa Yeremiya, Ndidzakufunsa iwe kanthu; usandibisire ine kanthu.
15 Ndipo Yeremiya anati kwa Zedekiya, Ndikakufotokozerani, kodi simudzandipha ine? Ndipo ndikakupangirani, simudzandimvera ine.
16 Ndipo mfumu Zedekiya analumbira m’tseri kwa Yeremiya, kuti, Pali Yehova, amene anatilengera ife moyo uno, sindidzakupha iwe sindidzakupereka iwe m’manja mwa anthu awa amene afuna moyo wako.
17 Ndipo Yeremiya anati kwa Zedekiya, Atero Yehova, Mulungu wa makamu, Mulungu wa Israele: Ngati mudzatulukira kwa akulu a mfumu ya ku Babiloni, mudzakhala ndi moyo, ndipo mzindawu sudzatenthedwa ndi moto; ndipo mudzakhala ndi moyo ndi banja lanu;
18 koma ngati simudzatulukira kwa akulu a mfumu ya ku Babiloni, mzindawu udzaperekedwa m’dzanja la Ababiloni, ndipo udzatenthedwa ndi moto, ndipo simudzapulumuka m’manja mwao.
19 Ndipo mfumu Zedekiya anati kwa Yeremiya, Ine ndiopa Ayuda amene anandipandukira ine kunka kwa Ababiloni, angandipereke ine m’manja mwao, angandiseke.
20 Koma Yeremiya anati, Sadzakuperekani. Mveranitu mau a Yehova, amene ndinena ndi inu, chomwecho kudzakomera inu, ndipo moyo wanu udzakhalabe.
21 Koma ngati mukana kutuluka, mau anandisonyeza Yehova ndi awa:
22 Taonani, akazi onse otsala m’nyumba ya mfumu ya Yuda adzatulutsidwa kunka kwa akulu a mfumu ya ku Babiloni, ndipo akaziwo adzati, Oyanjana nanu anakunyengani, ndi kukuposani inu, mapazi anu amire m’thope, abwerera m’mbuyo.
23 Ndipo adzatulutsira Ababiloni akazi anu onse, ndi ana anu, ndipo simudzapulumuka m’manja ao, koma mudzagwidwa ndi dzanja la mfumu ya ku Babiloni; ndipo mudzatenthetsa mzindawu ndi moto.
24 Ndipo Zedekiya anati kwa Yeremiya, Anthu asadziwe mau amene, ndipo sudzafa.
25 Koma akamva akulu kuti ndalankhula ndi iwe, nakafika kwa iwe, ndi kuti kwa iwe, Utifotokozere ife chomwe wanena kwa mfumu; osatibisira ichi, ndipo sitidzakupha iwe; ndiponso zomwe mfumu inanena kwa iwe;
26 pamenepo uziti kwa iwo, Ndinagwa ndi pembedzero langa pamaso pa mfumu, kuti asandibwezerenso kunyumba ya Yonatani ndifere komweko.
27 Ndipo akulu onse anadza kwa Yeremiya, namfunsa; ndipo iye ananena nao monga mwa mau onsewo anamuuza mfumu. Ndipo analeka kunena naye; pakuti sikunamveke mlandu.
28 Ndipo Yeremiya anakhala m’bwalo la kaidi mpaka tsiku lakugwidwaYerusalemu. Ndipo anali komweko pogwidwa Yerusalemu.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/38-e9b3304ac04a26143a3e692c9bafda54.mp3?version_id=1068—