Tchimo la Yuda ndi losafafanizika
1 Tchimo la Yuda lalembedwa ndi peni lachitsulo, ndi nsonga ya diamondi; lalembedwa pa cholembapo cha m’mtima mwao, ndi pa nyanga za maguwa a nsembe ao.
2 Pokumbukira ana ao maguwa a nsembe ao ndi zoimiritsa zao kumitengo yaiwisi ya pa zitunda zazitali.
3 Iwe phiri langa la m’munda, ndidzapereka chuma chako ndi zosungidwa zako zikafunkhidwe, ndi misanje yako, chifukwa cha tchimo, m’malire ako onse.
4 Iwe, iwe wekha, udzaleka pa cholowa chako chimene ndinakupatsa iwe; ndipo ndidzakutumikiritsa adani ako m’dziko limene sulidziwa; pakuti wakoleza moto m’mkwiyo wanga umene udzatentha kunthawi zamuyaya.
Anthu azikhulupirira Yehova yekha
5 Atero Yehova: Wotembereredwa munthu amene akhulupirira munthu, natama mkono wanyama, nuchoka kwa Yehova mtima wake.
6 Ndipo adzakhala ngati tsanya la m’chipululu, ndipo saona pamene chifika chabwino; koma adzakhala m’malo oumitsa m’chipululu, dziko lachikungu lopanda anthu.
7 Wodala munthu amene akhulupirira Yehova, amene chikhulupiriro chake ndi Yehova.
8 Ndipo adzakhala ngati mtengo wooka kuli madzi, wotambalitsa mizu yake pamtsinje, wosaopa pofika nyengo yadzuwa, koma tsamba lake likhala laliwisi; ndipo suvutika chaka cha chilala, suleka kubala zipatso.
9 Mtima ndiwo wonyenga koposa, ndi wosachiritsika, ndani angathe kuudziwa?
10 Ine Yehova ndisanthula mtima, ndiyesa impso, kuti ndimpatse munthu yense monga mwa njira zake, monga zipatso za ntchito zake.
11 Monga nkhwali iumatira pa mazira amene sinaikire, momwemo iye amene asonkhanitsa chuma, koma mosalungama; pakati pa masiku ake chidzamsiya iye, ndipo pa chitsirizo adzakhala wopusa.
12 Malo opatulika athu ndiwo mpando wachifumu wa ulemerero, wokhazikika pamsanje chiyambire.
13 Inu Yehova, chiyembekezo cha Israele, onse amene akukusiyani Inu adzakhala ndi manyazi; onse ondichokera Ine adzalembedwa m’dothi, chifukwa asiya Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
14 Mundichiritse ine, Yehova, ndipo ndidzachiritsidwa; mundipulumutse ine, ndipo ndidzapulumutsidwa; pakuti chilemekezo changa ndinu.
15 Taonani, ati kwa ine, Mau a Yehova ali kuti? Adze tsopano.
16 Koma ine, pokhala mbusa sindinafulumire kuchokerako kuti ndikutsateni Inu; sindinakhumbe tsiku la tsoka; Inu mudziwa, chimene chinatuluka pa milomo yanga chinali pamaso panu.
17 Musakhale wondiopsetsa ine; ndinu pothawira panga tsiku la choipa.
18 Iwo akhale ndi manyazi amene andisautsa ine, koma ine ndisakhale ndi manyazi; aopsedwe iwo, koma ndisaopsedwe ine; muwatengere iwo tsiku la choipa, muwaononge ndi chionongeko chowirikiza.
Za kusunga tsiku la Sabata
19 Yehova anatero kwa ine: Pita, nuime mu Chipata cha Ana a Anthu, m’mene alowamo mafumu a Yuda, ndi m’mene atulukamo, ndi m’zipata zonse zaYerusalemu;
20 ndipo uziti kwa iwo, Tamvani mau a Yehova, inu mafumu a Yuda, ndi Ayuda onse, ndi onse okhala mu Yerusalemu, amene alowa pa zipatazi;
21 atero Yehova: Tadzayang’anirani nokha, musanyamule katundu tsiku laSabata, musalowe naye pa zipata za Yerusalemu;
22 musatulutse katundu m’nyumba zanu tsiku la Sabata, musagwire ntchito ili onse; koma mupatule tsiku la Sabata, monga ndinauza makolo anu;
23 koma sanamvere, sanatchere khutu lao, koma anaumitsa khosi lao, kuti asamve asalandire langizo.
24 Ndipo padzakhala, ngati mundimveretsa Ine, ati Yehova, kuti musalowetse katundu pa zipata za mzinda uwu tsiku la Sabata, koma mupatule tsiku la Sabata, osagwira ntchito m’menemo;
25 pamenepo padzalowa pa zipata za mzinda uwu mafumu ndi akulu okhala pa mpando wachifumu wa Davide, okwera pa magaleta ndi akavalo, iwo, ndi akulu ao, anthu a Yuda, ndi okhala mu Yerusalemu; ndipo mzinda uwu udzakhala kunthawi zamuyaya.
26 Ndipo adzachokera kumizinda ya Yuda, ndi kumalo akuzungulira Yerusalemu, ndi kudziko la Benjamini, ndi kuchidikha, ndi kumapiri, ndi kumwera, ndi kudza nazo nsembe zopsereza, ndi nsembe zophera, ndi nsembe zaufa, ndilubani, ndi kudza nazo zamayamikiro, kunyumba ya Yehova.
27 Koma ngati simudzamvera Ine kulipatula tsiku la Sabata, kusanyamula katundu ndi kulowa pa zipata za Yerusalemu tsiku la Sabata; pamenepo ndidzayatsa moto m’zipata zakezo, ndipo udzatha zinyumba za Yerusalemu, osazimidwanso.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/17-8e2b311aa4083ebce739626f64fe5aa1.mp3?version_id=1068—