Yeremiya apempherera anthu
1 Mau a Yehova amene anadza kwa Yeremiya onena za chilala.
2 Yuda alira, ndipo zipata zake zilefuka, zikhala pansi zovekedwa ndi zakuda; mfuu waYerusalemuwakwera.
3 Akulu ao atuma ang’ono ao kumadzi; afika kumaenje, osapeza madzi; abwera ndi mitsuko yao yopanda kanthu; ali ndi manyazi, athedwa nzeru, afunda mitu yao.
4 Chifukwa cha nthaka yochita ming’alu, pakuti panalibe mvula padziko, olima ali ndi manyazi, afunda mitu yao.
5 Inde, mbawalanso ya m’thengo ibala nisiya ana ake, chifukwa mulibe udzu.
6 Mbidzi zinaima pamapiri oti see, zipumira mphepo wefuwefu ngati ankhandwe; maso ao alema, chifukwa palibe udzu.
7 Zingakhale zoipa zathu zititsutsa ife, chitani Inu chifukwa cha dzina lanu, Yehova; pakuti zobwerera zathu zachuluka; takuchimwirani Inu.
8 Inu, chiyembekezo cha Israele, Mpulumutsi wake nthawi ya msauko, bwanji mukhala ngati mlendo m’dziko, ngati woyendayenda amene apatuka usiku?
9 Bwanji mukhala ngati munthu wodabwa, ngati munthu wamphamvu wosatha kupulumutsa? Koma Inu, Yehova, muli pakati pathu, titchedwa ndi dzina lanu; musatisiye.
Yehova osamvera pempherolo
10 Atero Yehova kwa anthu awa, Chomwecho akonda kusocherera; sanakanize mapazi ao; chifukwa chake Yehova sawalandira; tsopano adzakumbukira choipa chao, nadzalanga zochimwa zao.
11 Ndipo Yehova anati kwa ine, Usapempherere anthu awa zabwino.
12 Pamene asala chakudya, sindidzamva kufuula kwao; ndipo pamene apereka nsembe yopsereza, ndi nsembe yaufa sindidzawalandira; koma ndidzawatha ndi lupanga, ndi chilala, ndi mliri.
13 Ndipo ndinati, Ha, Ambuye Yehova! Taonani, aneneri ati kwa iwo, Simudzaona lupanga, simudzakhala ndi chilala; koma ndidzakupatsani mtendere weniweni mommuno.
14 Ndipo Yehova anati kwa ine, Aneneri anenera zonama m’dzina langa; sindinatume iwo, sindinauze iwo, sindinanene nao; anenera kwa inu masomphenya onama, ndi ula, ndi chinthu chachabe, ndi chinyengo cha mtima wao.
15 Chifukwa chake atero Yehova za aneneri onenera m’dzina langa, ndipo sindinawatume, koma ati, Lupanga ndi chilala sizidzakhala m’dziko muno; ndi lupanga ndi chilala aneneriwo adzathedwa.
16 Ndipo anthu amene adzanenera kwa inu adzaponyedwa kunja m’miseu ya Yerusalemu chifukwa cha chilala ndi lupanga; ndipo adzasowa akuwaika, ndi akazi ao, ndi ana ao aamuna ndi aakazi; ndipo ndidzatsanulira pa iwo zoipa zao.
17 Ndipo udzati kwa iwo mau awa, Maso anga agwe misozi usana ndi usiku, asaleke; pakuti namwali mwana wa anthu anga wasweka ndi kusweka kwakukulu, ndi bala lopweteka kwambiri.
18 Ndikatulukira kumunda, taonani ophedwa ndi lupanga! Ndikalowa m’mzinda, taonani odwala ndi njala! Pakutimnenerindi wansembe ayendayenda m’dziko osadziwa kanthu.
19 Kodi mwakanadi Yuda? Kodi mtima wanu wanyansidwa ndiZiyoni? Bwanji mwatipanda ife, ndipo tilibe kuchira? Tinayembekeza mtendere, koma sizinafike zabwino; tinayembekeza nthawi yakuchira, ndipo taonani mantha!
20 Tivomereza, Yehova, chisalungamo chathu, ndi choipa cha makolo athu; pakuti takuchimwirani Inu.
21 Musatinyoze ife, chifukwa cha dzina lanu; musanyazitse mpando wachifumu wa ulemerero wanu; mukumbukire musasiye pangano lanu lopangana ndi ife.
22 Mwa zachabe za mitundu ya anthu zilipo kodi, zimene zingathe kuvumbitsa mvula? Kapena miyamba kubweretsa mivumbi? Kodi si ndinu, Yehova, Mulungu wathu? Ndipo tidzakudikirani Inu; pakuti munalenga zonse zimenezi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JER/14-501b372628aa936d39973ae106cd13d7.mp3?version_id=1068—