Categories
YAKOBO

YAKOBO Mau Oyamba

Mau Oyamba

Wolemba kalatayi alembera Akhristu achiyuda obalalika kumaiko osiyanasiyana. Apereka malangizo amitundumitundu owathandiza kuwongolera moyo wao wa masiku onse mwa njira ya Chikhristu. Aziwonetsa makhalidwe abwino pa zochita zao zonse, pakuti “chikhulupiriro, chikapanda kukhala nacho ntchito, chikhala chakufa m’kati mwakemo.” (2.17)

Za mkatimu

Mau oyamba 1.1

Za chikhulupiriro ndi nzeru 1.2-8

Za umphawi ndi chuma 1.9-11

Za kuyesedwa ndi zovuta kapena zinyengo 1.12-18

Za kumva ndi kuchita zimene Mulungu anena 1.19-27

Awachenjeza kuti asamachite tsankho 2.1-13

Za chikhulupiriro ndi ntchito zake 2.14-26

Za kuwongolera lilime potsata nzeru zochokera kumwamba 3.1-18

Za kuchita chibwenzi ndi pansi pano 4.1—5.6

Za kuyembekeza mopirira ndi kupempherera odwala 5.7-20

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *