1 Yakobo, kapolo wa Mulungu ndi wa Ambuye YesuKhristu, kwa mafuko khumi ndi awiri a m’chibalaliko: ndikupatsani moni.
Za mayesero
2 Muchiyese chimwemwe chokha, abale anga, m’mene mukugwa m’mayesero a mitundumitundu;
3 pozindikira kuti chiyesedwe cha chikhulupiriro chanu chichita chipiriro.
4 Koma chipiriro chikhale nayo ntchito yake yangwiro, kuti mukakhale angwiro ndi opanda chilema, osasowa kanthu konse.
5 Koma wina wa inu ikamsowa nzeru, apemphe kwa Mulungu, amene apatsa kwa onse modzala manja, niwosatonza; ndipo adzampatsa iye.
6 Koma apemphe ndi chikhulupiriro, wosakayika konse; pakuti wokayikayo afanana ndi funde la nyanja lotengeka ndi mphepo ndi kuwinduka nayo.
7 Pakuti asayese munthu uyu kuti adzalandira kanthu kwa Ambuye;
8 munthu wa mitima iwiri akhala wosinkhasinkha panjira zake zonse.
9 Koma mbale woluluka adzitamandire pa ukulu wake;
10 ndipo mbale wolemera anyadire pamene atsitsidwa, pakuti adzapita monga duwa la udzu.
11 Pakuti latuluka dzuwa ndi kutentha kwake, ndipo laumitsa udzu; ndipo lathothoka duwa lake, ndi ukoma wa maonekedwe ake waonongeka; koteronso wachuma adzafota m’mayendedwe ake.
12 Wodala munthu wakupirira poyesedwa; pakuti pamene wavomerezeka, adzalandira korona wa moyo, amene Ambuye adalonjezera iwo akumkonda Iye.
13 Munthu poyesedwa, asanena, Ndiyesedwa ndi Mulungu; pakuti Mulungu sangathe kuyesedwa ndi zoipa, ndipo Iye mwini sayesa munthu:
14 koma munthu aliyense ayesedwa pamene chilakolako chake cha iye mwini chimkokera, ndikumnyenga.
15 Pamenepo chilakolakocho chitaima, chibala uchimo; ndipo uchimo, utakula msinkhu, ubala imfa.
16 Musanyengedwe, abale anga okondedwa.
17 Mphatso iliyonse yabwino, ndi chininkho chilichonse changwiro zichokera Kumwamba, zotsika kwa Atate wa mauniko, amene alibe chisanduliko, kapena mthunzi wa chitembenukiro.
18 Mwa chifuniro chake mwini anatibala ife ndi mau a choonadi, kuti tikhale ife ngati zipatso zoyamba za zolengedwa zake.
Tikhale akuchita a mau
19 Mudziwa, abale anga okondedwa, kuti munthu aliyense akhale wotchera khutu, wodekha polankhula, wodekha pakupsa mtima.
20 Pakuti mkwiyo wa munthu suchita chilungamo cha Mulungu.
21 Mwa ichi, mutavula chinyanso chonse ndi chisefukiro cha choipa, landirani ndi chifatso mau ookedwa mwa inu, okhoza kupulumutsa moyo wanu.
22 Khalani akuchita mau, osati akumva okha, ndi kudzinyenga nokha.
23 Pakuti ngati munthu ali wakumva mau, wosati wakuchita, iyeyu afanana ndi munthu wakuyang’anira nkhope yake ya chibadwidwe chake m’kalirole;
24 pakuti wadziyang’anira yekha, nachoka, naiwala pompaja nali wotani.
25 Koma iye wakupenyerera m’lamulo langwiro, ndilo laufulu, natero chipenyerere, ameneyo, posakhala wakumva wakuiwala, komatu wakuchita ntchito, adzakhala wodala m’kuchita kwake.
26 Ngati wina adziyesera ali wopembedza Mulungu, ndiye wosamanga lilime lake, koma adzinyenga mtima wake, kupembedza kwake kwa munthuyu nkopanda pake.
27 Mapembedzedwe oyera ndi osadetsa pamaso pa Mulungu ndi Atate ndiwo: kucheza ndi ana amasiye ndi akazi amasiye m’chisautso chao, ndi kudzisungira mwini wosachitidwa mawanga ndi dziko lapansi.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JAS/1-2befdb6b7b5e71c1747b0e4d1087eeb5.mp3?version_id=1068—