1 Uwakumbutse iwo agonje kwa akulu, ndi aulamuliro, akhale omvera, okonzeka pa ntchito iliyonse yabwino;
2 asachitire mwano munthu aliyense, asakhale andeu, akhale aulere, naonetsere chifatso chonse pa anthu onse.
3 Pakuti kale ifenso tinali opusa, osamvera, onyengeka, akuchitira ukapolo zilakolako ndi zokondweretsa za mitundumitundu, okhala m’dumbo ndi njiru, odanidwa, odana wina ndi mnzake.
4 Koma pamene kukoma mtima, ndi chikondi cha pa anthu, cha Mpulumutsi wathu Mulungu zidanoneka,
5 zosati zochokera m’ntchito za m’chilungamo, zimene tidazichita ife, komatu monga mwa chifundo chake anatipulumutsa ife, mwa kutsuka kwa kubadwanso ndi makonzedwe a Mzimu Woyera,
6 amene anatsanulira pa ife mochulukira, mwa YesuKhristuMpulumutsi wathu;
7 kuti poyesedwa olungama ndi chisomo cha Iyetu, tikayesedwe olowa nyumba monga mwa chiyembekezo cha moyo wosatha.
8 Okhulupirika mauwa, ndipo za izi ndifuna kuti ulimbitse mau, kuti iwo akukhulupirira Mulungu asamalire akhalebe atsogoleri a ntchito zabwino. Izi nzokoma ndi zopindulitsa anthu;
9 koma pewa mafunso opusa, ndi mawerengedwe a mibadwo, ndi ndeu, ndi makani a pamalamulo; pakuti sizipindulitsa, ndipo zili zachabe.
10 Munthu wopatukira chikhulupiriro, utamchenjeza kamodzi ndi kawiri, umkanize,
11 podziwa kuti wotereyo wasandulika konse, nachimwa, nakhala wodzitsutsa yekha.
12 Pamene ndikatuma Aritema kwa iwe, kapena Tikiko, chita changu kudza kwa ine ku Nikopoli: pakuti ndatsimikiza mtima kugonerako nyengo yachisanu.
13 Zena nkhoswe ya milandu, ndi Apolo ufulumire kuwakonzera zaulendo, kuti asasowe kanthu,
14 Ndipo anthu athu aphunzirenso asunge ntchito zabwino zofunika, kuti asakhale osabala zipatso.
15 Akukupatsa moni onse akukhala pamodzi ndi ine. Pereka moni kwa otikondawo m’chikhulupiriro. Chisomo chikhale ndi inu nonse.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/TIT/3-cfcb0f893943058a29a045b40318586f.mp3?version_id=1068—