Categories
TITO

TITO 2

Machenjezedwe a okalamba ndi anyamata ndi akapolo. Akhale chitsanzo yekha Tito

1 Koma iwe, lankhula zimene ziyenera chiphunzitso cholamitsa:

2 okalamba akhale odzisunga, olemekezeka, odziletsa, olama m’chikhulupiriro, m’chikondi, m’chipiriro.

3 Momwemonso akazi okalamba akhale nao makhalidwe oyenera anthu oyera, osadierekeza, osakodwa nacho chikondi cha pavinyo, akuphunzitsa zokoma;

4 kuti akalangize akazi aang’ono akonde amuna ao, akonde ana ao,

5 akhale odziletsa, odekha, ochita m’nyumba mwao, okoma, akumvera amuna a iwo okha, kuti mau a Mulungu angachitidwe mwano.

6 Momwemonso anyamata uwadandaulire akhale odziletsa;

7 m’zonse udzionetsere wekha chitsanzo cha ntchito zabwino; m’chiphunzitso chako uonetsere chosavunda, ulemekezeko,

8 mau olama osatsutsika; kuti iye wakutsutsana achite manyazi, posakhala nako kanthu koipa kakutinenera ife.

9 Akapolo amvere ambuye ao a iwo okha, nawakondweretse m’zonse; osakana mau ao;

10 osatapa pa zao, komatu aonetsere chikhulupiriko chonse chabwino; kuti akakometsere chiphunzitso cha Mpulumutsi wathu Mulungu m’zinthu zonse.

11 Pakuti chaonekera chisomo cha Mulungu chakupulumutsa anthu onse,

12 ndi kutiphunzitsa ife kuti, pokana chisapembedzo ndi zilakolako za dziko lapansi, tikhale ndi moyo m’dziko lino odziletsa, ndi olungama, ndi opembedza;

13 akulindira chiyembekezo chodala, ndi maonekedwe a ulemerero wa Mulungu wamkulu ndi Mpulumutsi wathu YesuKhristu;

14 amene anadzipereka yekha m’malo mwa ife, kuti akatiombole ife kuzoipa zonse, nakadziyeretsere yekha anthu akhale ake enieni, achangu pa ntchito zokoma.

15 Izi lankhula, ndipo uchenjeze, nudzudzule ndi ulamuliro wonse. Munthu asakupeputse.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/TIT/2-d63b8b5db3d7ce3073bd5a624611247e.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *