Mau Oyamba
Bukuli likamba nkhani ya Rute, mkazi wachimowabu amene adakwatiwa ndi mwamuna wa ku Israele. Mwamuna wake atamwalira, iye atsatira mpongozi wake Naomi ku Betelehemu kwao chifukwa chokhulupirira Mulungu wa Aisraele.
Nkhani yabwinoyi yochitika panthawi ija yankhanza ya
Oweruza
, iwonetsa kuti ngakhale amitundu nawonso adzalandira madalitso a Mulungu, akakhulupirira Mulungu wa Israele ndi kusanduka anthu ake.
Za mkatimu
Naomi abwerera ku Betelehemu pamodzi ndi Rute
1.1-22
Rute akumana ndi Bowazi
2.1—3.18
Rute akwatiwa ndi Bowazi Davide
4.1-22