Categories
OWERUZA

OWERUZA 6

Midiyani agonjetsa Aisraele

1 Koma ana a Israele anachita choipa pamaso pa Yehova; ndipo Yehova anawapereka m’dzanja la Midiyani zaka zisanu ndi ziwiri.

2 Pamene dzanja la Midiyani linagonjetsa Israele, ana a Israele anadzikonzera ming’ang’ala ya m’mapiri, ndi mapanga, ndi malinga chifukwa cha Midiyani.

3 Ndipo kunali, akabzala Israele, amakwera Amidiyani, ndi Amaleke, ndi ana a kum’mawa, inde amawakwerera;

4 nawamangira misasa, namaononga zipatso za m’dziko mpaka ufika ku Gaza, osawasiyira chochirira njala mu Israele, ngakhale nkhosa, kapena ng’ombe, kapena bulu.

5 Pakuti anakwera nazo zoweta zao ndi mahema ao, analowa ngati dzombe kuchuluka kwao; iwowa ndingamirazao zomwe nzosawerengeka; ndipo analowa m’dziko kuliononga.

6 Ndipo Israele anafooka kwambiri chifukwa cha Midiyani; ndipo ana a Israele anafuula kwa Yehova.

7 Ndipo kunali, pamene ana a Israele anafuula kwa Yehova chifukwa cha Midiyani,

8 Yehova anatuma munthumnenerikwa ana a Israele, nanena nao, Atero Yehova Mulungu wa Israele, Ine ndinakukwezani kuchokera mu Ejipito, ndi kukutulutsani m’nyumba ya ukapolo;

9 ndipo ndinakulanditsani m’dzanja la Aejipito, ndi m’dzanja la onse akupsinja inu, ndi kuwaingitsa pamaso panu, ndi kukupatsani dziko lao;

10 ndipo ndinati kwa inu, Ine ndine Yehova Mulungu wanu; musamaopa milungu ya Aamori amene mukhala m’dziko lao; koma simunamvere mau anga.

Mngelo wa Mulungu amdzera Gideoni

11 Pamenepo anadza mthenga wa Yehova, nakhala patsinde pa thundu wokhala mu Ofura, wa Yowasi Mwabiyezere; ndi mwana wake Gideoni analikuomba tirigu m’mopondera mphesa, awabisire Amidiyani.

12 Ndipo mthenga wa Yehova anamuonekera, nati kwa iye, Yehova ali nawe, ngwazi iwe, wamphamvu iwe.

13 Ndipo Gideoni ananena naye, Mbuye wanga, ngati Yehova ali nafe chatigwera ife bwanji chonsechi? Ndipo zili kuti zodabwitsa zake zonse zimene makolo athu anatiwerengera, ndi kuti, Sanatikweze kodi Yehova kuchokera mu Ejipito? Koma tsopano Yehova watitaya natipereka m’dzanja la Midiyani.

14 Pamenepo Yehova anamtembenukira, nati, Muka nayo mphamvu yako iyi, nupulumutse Israele m’dzanja la Midiyani. Sindinakutume ndi Ine kodi?

15 Ndipo anati kwa Iye, Ha! Mbuye, ndidzapulumutsa Israele ndi chiyani? Taonani, banja langa lili loluluka mu Manase, ndipo ine ndine wamng’ono m’nyumba ya atate wanga.

16 Ndipo Yehova ananena naye, Popeza Ine ndidzakhala nawe udzakantha Amidiyani ngati munthu mmodzi.

17 Ndipo anati kwa Iye, Ngati mundikomera mtima mundionetse chizindikiro tsopano chakuti ndi Inu wakunena nane.

18 Musachoke pano, ndikupemphani, mpaka ndikudzerani ndi kutulutsa chopereka changa ndi kuchiika pamaso panu. Ndipo anati, Ndidzalinda mpaka ubwera.

19 Ndipo Gideoni analowa, nakonza kambuzi ndi mikate yopanda chotupitsa ya efa wa ufa; nyamayi anaiika m’lichero, ndi msuzi anauthira mumbale, natuluka nazo kwa Iye ali patsinde pa thundu, nazipereka.

20 Koma mthenga wa Mulungu ananena naye, Tenga nyamayi ndi mikate yopanda chotupitsa ndi kuziika pathanthwe pano ndi kutsanula msuzi. Ndipo anatero.

21 Pamenepo mthenga wa Yehova anatambasula nsonga ya ndodo inali m’dzanja lake, nakhudza nyamayi ndi mikate yopanda chotupitsa; ndipo unatuluka moto m’thanthwe nunyeketsa nyama ndi mikate yopanda chotupitsa; ndi mthenga wa Yehova anakanganuka pamaso pake.

22 Pamenepo Gideoni anaona kuti ndiye mthenga wa Yehova, nati Gideoni, Tsoka ine, Yehova Mulungu! Popeza ndaona mthenga wa Yehova maso ndi maso.

23 Ndipo Yehova anati kwa iye, Mtendere ukhale ndi iwe, usaope, sudzafa.

24 Pamenepo Gideoni anammangira Yehova guwa la nsembe pomwepo; nalitcha Yehova-ndiye-mtendere; likali mu Ofura wa Aabiyezere ndi pano pomwe.

Gideoni agamula guwa la nsembe la Baala

25 Ndipo kunali, usiku womwe uja Yehova ananena naye, Tenga ng’ombe ya atate wako, ndiyo ng’ombe yachiwiri ya zaka zisanu ndi ziwiri, nugamule guwa la nsembe laBaalandilo la atate wako, nulikhe chifanizo chili pomwepo;

26 numangire Yehova Mulungu wako guwa la nsembe pamwamba pa lingali, monga kuyenera; nutenge ng’ombe yachiwiriyo, nufukize nsembe yopsereza; nkhuni zake uyese chifanizo walikhacho.

27 Pamenepo Gideoni anatenga amuna khumi mwa anyamata ake, nachita monga Yehova adanena naye; ndipo kunali, popeza anaopa akunyumba ya atate wake, ndi amuna akumudziwo, sanachichite msana, koma usiku.

28 Ndipo pakuuka mamawa amuna akumudziwo, taonani, guwa la nsembe la Baala litagamuka, ndi chifanizo chinali pomwepo chitalikhidwa ndi ng’ombe yachiwiri yoperekedwa paguwa la nsembe adalimanga.

29 Nanenana wina ndi mnzake, Wachita ichi ndani? Ndipo atafunafuna nafunsafunsa, anati, Gideoni, mwana wa Yowasi wachita ichi.

30 Pamenepo amuna akumudziwo anati kwa Yowasi, Umtulutse mwana wako kuti afe; pakuti anagamula guwa la nsembe la Baala, pakutinso analikha chifanizo chinali pomwepo.

31 Koma Yowasi anati kwa onse akumuimirira, Kodi inu mumnenera Baala mlandu? Kapena kodi mudzampulumutsa iye? Iye amene amnenera mlandu aphedwe kukali m’mawa; akakhala mulungu adzinenere yekha mlandu, popeza wina wamgamulira guwa lake la nsembe.

32 Chifukwa chake anamutcha tsiku lija Yerubaala, ndi kuti, Amnenere mlandu Baala popeza anamgamulira guwa lake la nsembe.

33 Pamenepo Amidiyani onse ndi Aamaleke ndi ana a kum’mawa anasonkhana pamodzi naoloka, namanga misasa m’chigwa cha Yezireele.

34 Koma mzimu wa Yehova unavala Gideoni; naomba lipenga iye, ndi a banja la Abiyezere analalikidwa kumtsata iye.

35 Ndipo anatuma mithenga kwa Manase konse; ndi iwonso analalikidwa kumtsata iye; natuma mithenga kwa Asere, ndi kwa Zebuloni, ndi kwa Nafutali; iwo nadzakomana nao.

36 Ndipo Gideoni anati kwa Mulungu, Mukadzapulumutsa Israele ndi dzanja langa monga mwanena,

37 taonani, ndidzaika chikopa cha ubweya popunthira tirigu; pakakhala mame pachikopa pokha, ndi panthaka ponse pouma, pamenepo ndidzadziwa kuti mudzapulumutsa Israele ndi dzanja langa monga mwanena.

38 Ndipo kunatero; pakuti anauka mamawa, nafinya chikopacho, nakamula mame a pachikopa, madzi ake odzala mbale.

39 Ndipo Gideoni ananena ndi Mulungu, Mkwiyo wanu usandiyakire, ndinene kamodzi kokha: ndikuyeseni kamodzi kokha ndi chikopa; paume pachikopa pokha, ndi panthaka ponse pakhale mame.

40 Ndipo Mulungu anatero usiku uja; pakuti panauma pachikopa pokha, ndi panthaka ponse panali mame.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/JDG/6-afa12d2564e06808671f6e2a4c8f0504.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *