Mau Oyamba
Nyimbo ya Solomoni
ndi mndandanda wa ndakatulo za chikondi, ndipo zambiri mwa izo zili ngati nyimbo zimene mwamuna amalankhula kwa mkazi, kapena mkazi kwa mwamuna. Ambiri amakhulupirira kuti Solomoni ndiye analemba nyimboyi.
Ayuda amakhulupirira kuti nyimbozi zikuonetsa za ubale wa Mulungu ndi anthu ake, pamene Akhristu amakhulupirira kuti zikuonetsa za ubale wa Yesu ndi mpingo. Nyimbo zake zilipo zisanu ndi imodzi.
Za mkatimu
Nyimbo yoyamba
1.1—2.7
Nyimbo yachiwiri
2.8—3.5
Nyimbo yachitatu
3.6—5.1
Nyimbo yachinai
5.2—6.3
Nyimbo yachisanu
6.4—8.4
Nyimbo yachisanu ndi chimodzi
8.5-14