1 Mwenzi utakhala ngati mlongo wanga,
woyamwa pa bere la amai!
Ndikadakupeza panja, ndikadakupsompsona;
osandinyoza munthu.
2 Ndikadakutsogolera, kukulowetsa m’nyumba ya amai,
kuti andilange mwambo;
ndikadakumwetsa vinyo wokoleretsa,
ndi madzi a makangaza anga.
3 Dzanja lamanzere lake akadanditsamiritsa kumutu,
lamanja lake ndi kundifungatira.
4 Ndikulumbirirani, ana aakazi inu a kuYerusalemu,
muutsiranji, mugalamutsiranji chikondi,
chisanafune mwini.
5 Ndaniyu achokera kuchipululu,
alikutsamira bwenzi lake?
Pa tsinde la muula ndinakugalamutsa mnyamatawe:
Pomwepo amai ako anali mkusauka nawe,
pomwepo wakukubala anali m’pakati pa iwe.
6 Undilembe pamtima pako, mokhoma chizindikiro,
nundikhomenso chizindikiro pamkono pako;
pakuti chikondi chilimba ngati imfa;
njiru imangouma ngati manda:
Kung’anima kwake ndi kung’anima kwa moto,
ngati mphezi ya Yehova.
7 Madzi ambiri sangazimitse chikondi,
ngakhale mitsinje yodzala kuchikokolola:
Mwamuna akapereka katundu yense wa m’nyumba yake
ngati sintho la chikondi,
akanyozedwa ndithu.
8 Tili ndi mlongo wathu wamng’ono,
alibe mawere;
timchitirenji mlongo wathu
tsiku lokhoma unkhoswe wake?
9 Ngati ndiye khoma, tidzamanga pa iye nsanja yasiliva:
Ngati ndiye chitseko tidzamtsekereza ndi matabwa amikungudza.
10 Ndine khoma, mawere anga akunga nsanja zake:
Pamaso pa mnyamatayo ndinafanana ngati wopeza mtendere.
11 Solomoni anali ndi munda wamipesa ku Baala-Hamoni;
nabwereka alimi mundawo;
yense ambwezere ndalama chikwi chifukwa cha zipatso zake.
12 Koma munda wanga wamipesa,
uli pamaso panga ndiwo wangatu;
nacho chikwicho, Solomoni iwe,
koma olima zipatso zake azilandira mazana awiri.
13 Namwaliwe wokhala m’minda,
anzako amvera mau ako:
Nanenanso undimvetse.
14 Dzifulumira, mnyamatawe wokondedwa wanga,
dzifanane ngati mphoyo pena mwana wa mbawala
pa mapiri a mphoka.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/SNG/8-2edcd607c87b9c7f04e8ec5a0bb46e37.mp3?version_id=1068—