1 Ha, mapazi ako akongola m’zikwakwata,
mwana wamkaziwe wa mfumu!
Pozinga m’chuuno mwako pakunga zonyezimira,
ntchito ya manja a mmisiri waluso.
2 Pamchombo pako pakunga chikho choulungika,
chosasowamo vinyo wosanganika:
Pamimba pako pakunga mulu wa tirigu
wozingidwa ndi akakombo.
3 Mawere ako akunga ana awiri a nswala
anabadwa limodzi.
4 Khosi lako likunga nsanja yaminyanga;
maso ako akunga matawale a ku Hesiboni,
a pa chipata cha Batirabimu;
mphuno yako ikunga nsanja ya ku Lebanoni
imene iloza ku Damasiko.
5 Mutu wako ukunga Karimele,
ndi tsitsi la pamutu pako likunga nsalu yofiirira;
mfumu yamangidwa ndi nkhata zake ngati wam’nsinga.
6 Ha, ndiwe wokongola ndi wofunika,
bwenziwe, m’zokondweretsa!
7 Msinkhu wakowu ukunga mgwalangwa,
mawere ako akunga matsango amphesa.
8 Ndinati, Ndikakwera pa mgwalangwapo,
ndikagwira nthambi zake:
Mawere ako ange ngati matsango amphesa,
ndi kununkhira kwa mpweya wako ngati maula.
9 M’kamwa mwako munge ngati vinyo woposa,
womeza tseketseke bwenzi langa,
wolankhulitsa milomo ya ogona tulo.
10 Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo,
ndine amene andifunayo.
11 Tiye, bwenzi langa, tinke kuminda;
titsotse m’midzi.
12 Tilawire kunka kuminda yamipesa;
tiyang’ane ngati mpesa waphuka, kunje ndi kuonetsa zipatso,
makangaza ndi kutuwa maluwa ake;
pompo ndidzakupatsa chikondi changa.
13 Mankhwala a chikondi anunkhira,
ndi pamakomo pathu zipatso zabwino,
za mitundumitundu, zakale ndi zatsopano,
zimene ndakukundikira iwe, wokondedwa wanga.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/SNG/7-1055d898df24daffdf8b6c36d7568e92.mp3?version_id=1068—