Categories
NYIMBO YA SOLOMONI

NYIMBO YA SOLOMONI 7

1 Ha, mapazi ako akongola m’zikwakwata,

mwana wamkaziwe wa mfumu!

Pozinga m’chuuno mwako pakunga zonyezimira,

ntchito ya manja a mmisiri waluso.

2 Pamchombo pako pakunga chikho choulungika,

chosasowamo vinyo wosanganika:

Pamimba pako pakunga mulu wa tirigu

wozingidwa ndi akakombo.

3 Mawere ako akunga ana awiri a nswala

anabadwa limodzi.

4 Khosi lako likunga nsanja yaminyanga;

maso ako akunga matawale a ku Hesiboni,

a pa chipata cha Batirabimu;

mphuno yako ikunga nsanja ya ku Lebanoni

imene iloza ku Damasiko.

5 Mutu wako ukunga Karimele,

ndi tsitsi la pamutu pako likunga nsalu yofiirira;

mfumu yamangidwa ndi nkhata zake ngati wam’nsinga.

6 Ha, ndiwe wokongola ndi wofunika,

bwenziwe, m’zokondweretsa!

7 Msinkhu wakowu ukunga mgwalangwa,

mawere ako akunga matsango amphesa.

8 Ndinati, Ndikakwera pa mgwalangwapo,

ndikagwira nthambi zake:

Mawere ako ange ngati matsango amphesa,

ndi kununkhira kwa mpweya wako ngati maula.

9 M’kamwa mwako munge ngati vinyo woposa,

womeza tseketseke bwenzi langa,

wolankhulitsa milomo ya ogona tulo.

10 Ndine wa wokondedwa wanga mnyamatayo,

ndine amene andifunayo.

11 Tiye, bwenzi langa, tinke kuminda;

titsotse m’midzi.

12 Tilawire kunka kuminda yamipesa;

tiyang’ane ngati mpesa waphuka, kunje ndi kuonetsa zipatso,

makangaza ndi kutuwa maluwa ake;

pompo ndidzakupatsa chikondi changa.

13 Mankhwala a chikondi anunkhira,

ndi pamakomo pathu zipatso zabwino,

za mitundumitundu, zakale ndi zatsopano,

zimene ndakukundikira iwe, wokondedwa wanga.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/SNG/7-1055d898df24daffdf8b6c36d7568e92.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *