Categories
NYIMBO YA SOLOMONI

NYIMBO YA SOLOMONI 6

1 Bwenzi lako wapita kuti,

mkaziwe woposa kukongola?

Bwenzi lako wapatukira kuti,

tikamfunefune pamodzi nawe?

2 Bwenzi langa watsikira kumunda kwake,

kuzitipula za mphoka,

kukadya kumunda kwake, ndi kutchera akakombo.

3 Ndine wake wa wokondedwa wanga,

wokondedwa wanganso ndiye wa ine;

aweta zake pakati pa akakombo.

Mkwati ndi mkwatibwi alemekezana

4 Wakongola, bwenzi langa, namwaliwe ngati Tiriza,

wokoma ngatiYerusalemu,

woopsa ngati nkhondo ndi mbendera.

5 Undipatutsire maso ako,

pakuti andiopetsa.

Tsitsi lako likunga gulu la mbuzi,

zigona pambali pa Giliyadi.

6 Mano ako akunga gulu la nkhosa zazikazi,

zikwera kuchokera kosamba;

yonse ili ndi ana awiri,

palibe imodzi yopoloza.

7 Palitsipa pako pakunga phande la khangaza

paseri pa chophimba chako.

8 Alipo akazi aakulu a mfumu makumi asanu ndi limodzi,

kudza akazi aang’ono makumi asanu ndi atatu,

ndi anamwali osawerengeka.

9 Nkhunda yanga, wangwiro wangayu, ndiye mmodzi;

ndiye wobadwa yekha wa amake;

ndiye wosankhika wa wombala.

Ana aakazi anamuona, namutcha wodala;

ngakhale akazi aakulu a mfumu,

ndi akazi aang’ono namtamanda.

10 Nati, Ndaniyo atuluka ngati mbandakucha,

wokongola ngati mwezi,

woyera ngati dzuwa,

woopsa ngati nkhondo ndi mbendera?

11 Ndinatsikira kumunda wa mtedza,

kukapenya msipu wa m’chigwa,

kukapenya ngati pamipesa paphuka,

ngati pamakangaza patuwa maluwa.

12 Ndisanazindikire, moyo wanga unandiimika

pakati pa magaleta a anthu anga aufulu.

13 Anati, Bwera, bwera, Msulamiwe;

bwera, bwera, tiyang’ane pa iwe.

Muyang’aniranji pa Msulami,

ngati pa masewero akuguba?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/SNG/6-0164c8d0b6458e7aab941d11404b254f.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *