Categories
NYIMBO YA SOLOMONI

NYIMBO YA SOLOMONI 4

Mkwati alemekeza mkwatibwi

1 Taona, wakongola, bwenzi langa,

namwaliwe, taona, wakongola;

maso ako akunga a nkhunda patseri pa chophimba chako.

Tsitsi lako likunga gulu la mbuzi,

zooneka paphiri la Giliyadi.

2 Mano ako akunga gulu la nkhosa zosengasenga,

zokwera kuchokera kosamba;

yonse ili ndi ana awiri,

palibe imodzi yopoloza.

3 Milomo yako ikunga mbota yofiira,

m’kamwa mwako ndi kukoma:

Palitsipa pako pakunga phande la khangaza

paseri pa chophimba chako.

4 Khosi lako likunga nsanja ya Davide anaimangira zida,

apachikapo zikopa zikwi,

ngakhale zikopa zonse za amuna amphamvu.

5 Mawere ako awiri akunga ana awiri a nswala obadwa limodzi,

akudya pakati pa akakombo.

6 Mpaka dzuwa litapepa, mithunzi ndi kutanimpha,

ndikamuka kuphiri lamure,

ndi kuchitunda chalubani.

7 Wakongola monsemonse, wokondedwa wanga, namwaliwe,

mulibe chilema mwa iwe.

8 Idza nane kuchokera ku Lebanoni, mkwatibwi,

kuchokera nane ku Lebanoni:

Unguza pamwamba pa Amana,

pansonga ya Seniri ndi Heremoni,

pa ngaka za mikango,

pa mapiri a anyalugwe.

9 Walanda mtima wanga, mlongo wanga, mkwatibwi;

walanda mtima wanga ndi diso lako limodzi,

ndi chinganga chimodzi cha pakhosi pako.

10 Ha, chikondi chako nchokongola, mlongo wanga, mkwatibwi!

Kodi chikondi chako sichiposa vinyo?

Kununkhira kwa mphoka yako

ndi kuposa zonunkhiritsa za mitundumitundu!

11 M’milomo yako, mkwatibwi, mukukha uchi,

uchi ndi mkaka zili pansi pa lilime lako;

kununkhira kwa zovala zako

ndi kunga kununkhira kwa Lebanoni.

12 Mlongo wanga, mkwatibwi ndiye munda wotsekedwa;

ngati kasupe wotsekedwa, ndi chitsime chopikiza.

13 Mphukira zako ndi munda wamakangaza,

ndi zipatso zofunika, bonongwe ndinarido.

14 Narido ndi chikasu,

nzimbe ndi sinamoni, ndi mitengo yonse ya lubani;

mure ndi khonje, ndi zonunkhiritsa zonse zomveka.

15 Ndiwe kasupe wa m’minda,

chitsime cha madzi amoyo,

ndi mitsinje yoyenda yochokera ku Lebanoni.

Ayankha mkwatibwi

16 Galamuka, mphepo ya kumpoto iwe,

nudze, mphepo iwe ya kumwera;

nuombe pamunda panga, kuti zonunkhiritsa zake zitulukemo.

Bwenzi langa mnyamatayo, alowe m’munda mwake,

nadye zipatso zake zofunika.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/SNG/4-81cf6194500e89d5b7e58635224e8862.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *