Categories
NYIMBO YA SOLOMONI

NYIMBO YA SOLOMONI 3

Mkwatibwi apeza mkwati

1 Usiku pamphasa panga ndinamfunafuna amene moyo wanga umkonda:

Ndinamfunafuna, koma osampeza.

2 Ndinati, Ndiuketu, ndiyendeyende m’mzinda,

m’makwalala ndi m’mabwalo ake,

ndimfunefune amene moyo wanga umkonda:

Ndimfunafuna, koma osampeza.

3 Alonda akuyendayenda m’mzinda anandipeza:

Ndinati, Kodi munamuona amene moyo wanga umkonda?

4 Nditawapitirira pang’ono,

ndinampeza amene moyo wanga umkonda:

Ndinamgwiritsitsa, osamfumbatula,

mpaka nditamlowetsa m’nyumba ya amai,

ngakhale m’chipinda cha wondibala.

5 Ndikulumbirirani, ana aakazi inu a kuYerusalemu,

pali mphoyo, ndi mbawala yakuthengo,

kuti musautse, ngakhale kugalamutsa chikondi,

mpaka chikafuna mwini.

Ulendo wa ukwati

6 Ndaniyu akwera kutuluka m’chipululu ngati utsi wa tolo,

wonunkhira ndimurendilubani,

ndi zonunkhiritsa zonse za wogulitsa?

7 Taonani, ndi machira a Solomoni;

pazingapo amuna amphamvu makumi asanu ndi limodzi,

a mwa ngwazi za Israele.

8 Onsewo agwira lupanga, nazolowera nkhondo:

Yense ali ndi lupanga lake pantchafu pake,

chifukwa cha upandu wa usiku.

9 Solomoni mfumu anadzipangira machira okhalamo tsonga

ndi matabwa a ku Lebanoni.

10 Anapanga timilongoti take ndisiliva,

cha pansi pake ndi golide, mpando wake ndi nsalu yofiirira,

pakati pake panayalidwa za chikondi

cha ana aakazi a ku Yerusalemu.

11 Tulukani, ana aakazi inu aZiyoni,

mupenye Solomoni mfumu,

ndi korona amake amamveka naye tsiku la ukwati wake,

ngakhale tsiku lakukondwera mtima wake.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/SNG/3-1a31c7bcd35df394c8dc95d3a80502bc.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *