Mkwatibwi apeza mkwati
1 Usiku pamphasa panga ndinamfunafuna amene moyo wanga umkonda:
Ndinamfunafuna, koma osampeza.
2 Ndinati, Ndiuketu, ndiyendeyende m’mzinda,
m’makwalala ndi m’mabwalo ake,
ndimfunefune amene moyo wanga umkonda:
Ndimfunafuna, koma osampeza.
3 Alonda akuyendayenda m’mzinda anandipeza:
Ndinati, Kodi munamuona amene moyo wanga umkonda?
4 Nditawapitirira pang’ono,
ndinampeza amene moyo wanga umkonda:
Ndinamgwiritsitsa, osamfumbatula,
mpaka nditamlowetsa m’nyumba ya amai,
ngakhale m’chipinda cha wondibala.
5 Ndikulumbirirani, ana aakazi inu a kuYerusalemu,
pali mphoyo, ndi mbawala yakuthengo,
kuti musautse, ngakhale kugalamutsa chikondi,
mpaka chikafuna mwini.
Ulendo wa ukwati
6 Ndaniyu akwera kutuluka m’chipululu ngati utsi wa tolo,
wonunkhira ndimurendilubani,
ndi zonunkhiritsa zonse za wogulitsa?
7 Taonani, ndi machira a Solomoni;
pazingapo amuna amphamvu makumi asanu ndi limodzi,
a mwa ngwazi za Israele.
8 Onsewo agwira lupanga, nazolowera nkhondo:
Yense ali ndi lupanga lake pantchafu pake,
chifukwa cha upandu wa usiku.
9 Solomoni mfumu anadzipangira machira okhalamo tsonga
ndi matabwa a ku Lebanoni.
10 Anapanga timilongoti take ndisiliva,
cha pansi pake ndi golide, mpando wake ndi nsalu yofiirira,
pakati pake panayalidwa za chikondi
cha ana aakazi a ku Yerusalemu.
11 Tulukani, ana aakazi inu aZiyoni,
mupenye Solomoni mfumu,
ndi korona amake amamveka naye tsiku la ukwati wake,
ngakhale tsiku lakukondwera mtima wake.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/SNG/3-1a31c7bcd35df394c8dc95d3a80502bc.mp3?version_id=1068—