Malire a dziko la Kanani
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Uza ana a Israele, nunene nao, Mutalowa m’dziko la Kanani, ndilo dziko logwera inu, likhale cholowa chanu, dziko la Kanani monga mwa malire ake,
3 dera lanu la kumwera lidzakhala lochokera ku chipululu cha Zini, kutsata m’mphepete mwa Edomu, ndi malire anu a kumwera adzakhala ochokera ku malekezero a Nyanja ya Mchere kum’mawa;
4 ndi malire anu adzapinda kuchokera kumwera kunka pokwera Akarabimu, ndi kupitirira ku Zini; ndi kutuluka kwake adzachokera kumwera ku Kadesi-Baranea, nadzatuluka kunka ku Hazara-Adara, ndi kupita kunka ku Azimoni;
5 ndipo malirewo adzapinda ku Azimoni kunka ku mtsinje wa Ejipito, ndi kutuluka kwao adzatuluka kunyanja.
6 Kunena za malire a kumadzulo Nyanja Yaikulu ndiyo malire anu; ndiyo malire anu a kumadzulo.
7 Malire anu a kumpoto ndiwo: kuyambira ku Nyanja Yaikulu mulinge kuphiri la Hori:
8 kuchokera kuphiri la Hori mulinge polowera Hamati; ndipo kutuluka kwake kwa malire kudzakhala ku Zedadi.
9 Ndipo malirewo adzatuluka kunka ku Zifuroni, ndi kutuluka kwake kudzakhala ku Hazara-Enani; ndiwo malire anu a kumpoto.
10 Ndipo mudzilembere malire a kum’mawa ochokera ku Hazara-Enani kunka ku Sefamu;
11 ndi malire adzatsika ku Sefamu kunka ku Ribula, kum’mawa kwa Aini; ndipo malire adzatsika, nadzafikira mbali ya nyanja ya Kinereti kum’mawa,
12 ndi malire adzatsika ku Yordani, ndi kutuluka kwake kudzakhala ku Nyanja ya Mchere; ili ndili dziko lanu monga mwa malire ake polizinga.
13 Ndipo Mose anauza ana a Israele, nati, Ili ndi dzikoli mudzalandira ndi kuchita maere, limene Yehova analamulira awapatse mafuko asanu ndi anai ndi hafu;
14 popeza fuko la ana a Rubeni monga mwa nyumba za makolo ao, ndi fuko la ana a Gadi monga mwa nyumba za makolo ao, adalandira, ndi hafu la fuko la Manase lalandira cholowa chao;
15 mafuko awiriwa ndi hafu adalandira cholowa chao tsidya lija la Yordani ku Yeriko, kum’mawa, kotulukira dzuwa.
16 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
17 Maina a amunawo adzakugawirani dziko likhale cholowa chanu, ndi awa: Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni.
18 Muwatengenso akalonga, kalonga mmodzi ku fuko limodzi, agawe dziko likhale cholowa chao.
19 Maina a amunawo ndiwo: wa fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune.
20 Wa fuko la ana a Simeoni, Semuele mwana wa Amihudi.
21 Wa fuko la Benjamini, Elidadi mwana wa Kisiloni.
22 Wa fuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.
23 Wa ana a Yosefe; wa fuko la ana a Manase, kalonga Haniyele mwana wa Efodi.
24 Wa fuko la ana a Efuremu, kalonga Kemuwele mwana wa Sifutani.
25 Wa fuko la ana a Zebuloni, kalonga Elizafani mwana wa Paranaki.
26 Wa fuko la ana a Isakara, kalonga Palatiele mwana wa Azani.
27 Wa fuko la ana a Asere, kalonga Ahihudi mwana wa Selomi.
28 Wa fuko la ana a Nafutali, kalonga Pedahele mwana wa Amihudi.
29 Iwo ndiwo amene Yehova analamulira agawire ana a Israele cholowa chao m’dziko la Kanani.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/34-99a32c84db1e2a56461b834f6b4fb581.mp3?version_id=1068—