Categories
NUMERI

NUMERI 34

Malire a dziko la Kanani

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Uza ana a Israele, nunene nao, Mutalowa m’dziko la Kanani, ndilo dziko logwera inu, likhale cholowa chanu, dziko la Kanani monga mwa malire ake,

3 dera lanu la kumwera lidzakhala lochokera ku chipululu cha Zini, kutsata m’mphepete mwa Edomu, ndi malire anu a kumwera adzakhala ochokera ku malekezero a Nyanja ya Mchere kum’mawa;

4 ndi malire anu adzapinda kuchokera kumwera kunka pokwera Akarabimu, ndi kupitirira ku Zini; ndi kutuluka kwake adzachokera kumwera ku Kadesi-Baranea, nadzatuluka kunka ku Hazara-Adara, ndi kupita kunka ku Azimoni;

5 ndipo malirewo adzapinda ku Azimoni kunka ku mtsinje wa Ejipito, ndi kutuluka kwao adzatuluka kunyanja.

6 Kunena za malire a kumadzulo Nyanja Yaikulu ndiyo malire anu; ndiyo malire anu a kumadzulo.

7 Malire anu a kumpoto ndiwo: kuyambira ku Nyanja Yaikulu mulinge kuphiri la Hori:

8 kuchokera kuphiri la Hori mulinge polowera Hamati; ndipo kutuluka kwake kwa malire kudzakhala ku Zedadi.

9 Ndipo malirewo adzatuluka kunka ku Zifuroni, ndi kutuluka kwake kudzakhala ku Hazara-Enani; ndiwo malire anu a kumpoto.

10 Ndipo mudzilembere malire a kum’mawa ochokera ku Hazara-Enani kunka ku Sefamu;

11 ndi malire adzatsika ku Sefamu kunka ku Ribula, kum’mawa kwa Aini; ndipo malire adzatsika, nadzafikira mbali ya nyanja ya Kinereti kum’mawa,

12 ndi malire adzatsika ku Yordani, ndi kutuluka kwake kudzakhala ku Nyanja ya Mchere; ili ndili dziko lanu monga mwa malire ake polizinga.

13 Ndipo Mose anauza ana a Israele, nati, Ili ndi dzikoli mudzalandira ndi kuchita maere, limene Yehova analamulira awapatse mafuko asanu ndi anai ndi hafu;

14 popeza fuko la ana a Rubeni monga mwa nyumba za makolo ao, ndi fuko la ana a Gadi monga mwa nyumba za makolo ao, adalandira, ndi hafu la fuko la Manase lalandira cholowa chao;

15 mafuko awiriwa ndi hafu adalandira cholowa chao tsidya lija la Yordani ku Yeriko, kum’mawa, kotulukira dzuwa.

16 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

17 Maina a amunawo adzakugawirani dziko likhale cholowa chanu, ndi awa: Eleazara wansembe, ndi Yoswa mwana wa Nuni.

18 Muwatengenso akalonga, kalonga mmodzi ku fuko limodzi, agawe dziko likhale cholowa chao.

19 Maina a amunawo ndiwo: wa fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune.

20 Wa fuko la ana a Simeoni, Semuele mwana wa Amihudi.

21 Wa fuko la Benjamini, Elidadi mwana wa Kisiloni.

22 Wa fuko la ana a Dani, kalonga Buki mwana wa Yogili.

23 Wa ana a Yosefe; wa fuko la ana a Manase, kalonga Haniyele mwana wa Efodi.

24 Wa fuko la ana a Efuremu, kalonga Kemuwele mwana wa Sifutani.

25 Wa fuko la ana a Zebuloni, kalonga Elizafani mwana wa Paranaki.

26 Wa fuko la ana a Isakara, kalonga Palatiele mwana wa Azani.

27 Wa fuko la ana a Asere, kalonga Ahihudi mwana wa Selomi.

28 Wa fuko la ana a Nafutali, kalonga Pedahele mwana wa Amihudi.

29 Iwo ndiwo amene Yehova analamulira agawire ana a Israele cholowa chao m’dziko la Kanani.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/34-99a32c84db1e2a56461b834f6b4fb581.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *