Categories
NUMERI

NUMERI 33

Za ulendo wa Aisraele pakati pa Ramsesi ndi Sitimu

1 Maulendo a ana a Israele amene anatuluka m’dziko la Ejipito monga mwa makamu ao, ndi dzanja la Mose ndi Aroni, ndi awa.

2 Ndipo Mose analembera matulukidwe ao monga mwa maulendo ao, monga mwa mau a Yehova; ndipo maulendo ao ndi awa monga mwa matulukidwe ao.

3 Ndipo anachokera ku Ramsesi mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi woyamba; atachitaPaskam’mawa mwake ana a Israele, anatuluka ndi dzanja lokwezeka pamaso pa Aejipito onse,

4 pamene Aejipito analikuika oyamba kubadwa ao onse, amene Yehova adawakantha; Yehova adaweruzanso milungu yao.

5 Ndipo ana a Israele anachokera ku Ramsesi, nayenda namanga ku Sukoti.

6 Nachokera ku Sukoti, nayenda namanga mu Etamu, ndiko ku malekezero a chipululu.

7 Ndipo anachokera ku Etamu, nayenda nabwerera ku Pihahiroti, ndiko kutsogolo kwake kwa Baala-Zefoni; namanga iwo patsogolo pa Migidoli.

8 Ndipo anachokera ku Pihahiroti, naoloka pakati pa nyanja nalowa m’chipululu; nayenda ulendo wa masiku atatu m’chipululu cha Etamu, namanga mu Mara.

9 Ndipo anachokera ku Mara, nayenda nafika ku Elimu, ku Elimu ndiko kuli akasupe khumi ndi awiri a madzi, ndi akanjedza makumi asanu ndi awiri; namanga iwo komweko.

10 Ndipo anachokera ku Elimu, nayenda namanga ku Nyanja Yofiira.

11 Nachokera ku Nyanja Yofiira, nayenda namanga m’chipululu cha Sini.

12 Nachokera ku chipululu cha Sini, nayenda namanga mu Dofika.

13 Nachokera ku Dofika, nayenda namanga mu Alusi.

14 Nachokera ku Alusi, nayenda namanga mu Refidimu; kumeneko kunalibe madzi kuti anthu amwe.

15 Ndipo anachokera ku Refidimu, nayenda namanga m’chipululu cha Sinai.

16 Nachokera ku chipululu cha Sinai, nayenda namanga mu Kibroti-Hatava.

17 Nachokera ku Kibroti-Hatava, nayenda namanga mu Hazeroti.

18 Nachokera ku Hazeroti, nayenda namanga mu Ritima.

19 Nachokera ku Ritima, nayenda namanga mu Rimoni-Perezi.

20 Nachokera ku Rimoni-Perezi, nayenda namanga mu Libina.

21 Nachokera ku Libina, nayenda namanga mu Risa.

22 Nachokera Risa, nayenda namanga mu Kehelata.

23 Nachokera ku Kehelata, nayenda namanga m’phiri la Sefera.

24 Nachokera kuphiri la Sefera, nayenda namanga mu Harada.

25 Nachokera ku Harada, nayenda namanga mu Makeloti.

26 Nachokera ku Makeloti, nayenda namanga mu Tahata.

27 Nachokera ku Tahata, nayenda namanga mu Tera.

28 Nachokera ku Tera, nayenda namanga mu Mitika.

29 Nachokera ku Mitika, nayenda namanga mu Hasimona.

30 Nachokera ku Hasimona, nayenda namanga mu Meseroti.

31 Nachokera ku Meseroti, nayenda namanga mu Bene-Yaakani.

32 Nachokera ku Bene-Yaakani, nayenda namanga mu Hori Hagidigadi.

33 Nachokera ku Hori Hagidigadi, nayenda namanga mu Yotibata.

34 Nachokera ku Yotibata, nayenda namanga mu Aborona.

35 Nachokera ku Aborona, nayenda namanga mu Eziyoni-Gebere.

36 Nachokera ku Eziyoni-Gebere, nayenda namanga m’chipululu cha Zini (ndiko Kadesi).

37 Nachokera ku Kadesi, nayenda namanga m’phiri la Hori, ku malekezero a dziko la Edomu.

38 Ndipo Aroni wansembe anakwera m’phiri la Hori pa mau a Yehova, nafa komweko, atatuluka ana a Israele m’dziko la Ejipito zaka makumi anai, mwezi wachisanu, tsiku loyamba la mwezi.

39 Ndipo Aroni ndiye wa zaka zana limodzi mphambu makumi awiri kudza zitatu pakufa iye m’phiri la Hori.

40 Ndipo Mkanani, mfumu ya Aradi, wakukhala kumwera m’dziko la Kanani, anamva za kudza kwao kwa ana a Israele.

41 Ndipo anachokera kuphiri la Hori, nayenda namanga mu Zalimona.

42 Nachokera ku Zalimona, nayenda namanga mu Punoni.

43 Nachokera ku Punoni, nayenda namanga mu Oboti.

44 Nachokera ku Oboti, nayenda namanga mu Iyeabarimu, m’malire a Mowabu.

45 Nachokera ku Iyimu, nayenda namanga mu Diboni Gadi.

46 Nachokera ku Diboni Gadi, nayenda namanga mu Alimoni-Dibulataimu.

47 Nachokera ku Alimoni-Dibulataimu, nayenda namanga m’mapiri a Abarimu, chakuno cha Nebo.

48 Nachokera ku mapiri a Abarimu, nayenda namanga m’zidikha za Mowabu pa Yordani ku Yeriko.

49 Ndipo anamanga pa Yordani, kuyambira ku Beteyesimoti kufikira ku Abele-Sitimu m’zidikha za Mowabu.

Aisraele azipirikitsa eni dziko la Kanani

50 Ndipo Yehova ananena ndi Mose m’zidikha za Mowabu pa Yordani ku Yeriko, nati,

51 Nena ndi ana a Israele, nuti nao, Mutaoloka Yordani kulowa m’dziko la Kanani,

52 mupirikitse onse okhala m’dziko pamaso panu, ndi kuononga mafano ao onse a miyala, ndi kuononga mafano ao onse oyenga, ndi kupasula misanje yao yonse;

53 ndipo mulande dziko, ndi kukhala m’mwemo, pakuti ndinakupatsani inu dzikoli likhale lanulanu.

54 Ndipo mulandire dzikoli ndi kuchita maere monga mwa mabanja anu; cholowa chao chichulukire ochulukawo, cholowa chao chichepere ochepawo; kumene maere amgwera munthu, kumeneko nkwake; mulandire cholowa chanu monga mwa mafuko a makolo anu.

55 Koma mukapanda kupirikitsa okhala m’dziko pamaso panu, pamenepo iwo amene muwalola atsale adzakhala ngati zotwikira m’maso mwanu, ndi minga m’mbali zanu, nadzakuvutani m’dziko limene mukhalamo.

56 Ndipo kudzakhala kuti monga ndinayesa kuchitira iwowa, ndidzakuchitirani inu.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/33-5d44ba383ca6b0af402a9568cc0760ca.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *