Nsembe yopsereza yosalekeza
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Uza ana a Israele, nuti nao, Muzisamalira kubwera nacho kwa Ine chopereka changa, chakudya changa cha nsembe zanga zamoto, cha fungo lokoma, pa nyengo yake yoikika.
3 Ndipo unene nao, Nsembe yamoto imene muzibwera nayo kwa Yehova ndiyi: anaankhosa awiri a chaka chimodzi opanda chilema, tsiku ndi tsiku, nsembe yamoto yosalekeza.
4 Mwanawankhosammodziyo umpereke m’mawa, ndi mwanawankhosa winayo umpereke madzulo;
5 ndi limodzi la magawo khumi la efa wa ufa wosalala ukhale nsembe yaufa, wosakaniza ndi limodzi la magawo anai la hini wa mafuta opera.
6 Ndiyo nsembe yopsereza kosalekeza, yoikika kuphiri la Sinai, ichite fungo lokoma, nsembe yamoto ya Yehova.
7 Ndi nsembe yake yothira ya mwanawankhosa mmodziyo ndiyo limodzi la magawo anai la hini; m’malo opatulika uthirire Yehova nsembe yothira ya chakumwa cholimba.
8 Ndi mwanawankhosa winayo umpereke madzulo; monga nsembe yaufa ya m’mawa, ndi nsembe yothira yake, umpereke; ndiyo nsembe yamoto ya fungo lokoma la Yehova.
Nsembe yopsereza ya pa tsiku la Sabata
9 Ndipo tsiku laSabataanaankhosa awiri a chaka chimodzi, opanda chilema, ndi awiri a magawo khumi a efa wa ufa wosalala, ukhale nsembe yaufa, wosakaniza ndi mafuta, ndi nsembe yake yothira;
10 ndiyo nsembe yopsereza ya tsiku la Sabata lililonse, pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yake yothira.
11 Ndipo poyamba miyezi yanu muzibwera nayo nsembe yopsereza ya Yehova: ng’ombe zamphongo ziwiri, ndi nkhosa yamphongo imodzi, ndi anaankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi opanda chilema;
12 ndi atatu a magawo khumi a efa wa ufa wosalala, ikhale nsembe yaufa, wosakaniza ndi mafuta, ndiwo wa ng’ombe iliyonse; ndi awiri a magawo khumi a ufa wosalala, ikhale nsembe yaufa, wosakaniza ndi mafuta, ndiwo wa nkhosa yamphongo imodziyo;
13 ndi limodzi la magawo khumi la ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, ikhale nsembe yaufa, ndiwo wa mwanawankhosa yense; ndiyo nsembe yopsereza ya fungo lokoma, nsembe yamoto ya Yehova.
14 Ndipo nsembe zake zothira ndizo: limodzi la magawo khumi la hini wa vinyo ndiwo wa ng’ombe imodzi, ndi limodzi la magawo atatu la hini likhale la nkhosa yamphongo, ndi limodzi la magawo anai a hini likhale la mwanawankhosa; ndiyo nsembe yopsereza ya mwezi uliwonse kunena miyezi yonse ya chaka.
15 Ndi tonde mmodzi, akhale nsembe yauchimo ya Yehova; aikonze pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yake yothira.
Za zikondwerero zomveka
16 Ndipo mwezi woyamba, tsiku lakhumi ndi chinai la mwezi paliPaskawa Yehova.
17 Ndipo tsiku lakhumi ndi chisanu la mwezi uwu pali zikondwerero; masiku asanu ndi awiri azidya mkate wopanda chotupitsa.
18 Tsiku loyamba pali kusonkhana kopatulika; musamachita ntchito ya masiku ena;
19 koma mubwere nayo nsembe yamoto, nsembe yopsereza ya Yehova; ng’ombe ziwiri zamphongo, ndi nkhosa yamphongo imodzi, ndi anaankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi; akhale kwa inu opanda chilema;
20 ndi nsembe yao ya efa wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; mupereke atatu a magawo khumi akhale a ng’ombe, ndi awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo;
21 upereke limodzi la magawo khumi likhale la mwanawankhosa mmodzi; uzitero ndi anaankhosa asanu ndi awiri;
22 ndi tonde mmodzi akhale nsembe yauchimo, yakutetezera inu.
23 Mupereke izi pamodzi ndi nsembe yopsereza ya m’mawa, ndiyo ya nsembe yopsereza kosalekeza.
24 Momwemo mupereke chakudya cha nsembe yamoto cha fungo lokoma la Yehova, tsiku ndi tsiku, masiku asanu ndi awiri, chakupereka pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yake yothira.
25 Ndipo tsiku lachisanu ndi chiwiri mukhale nako kusonkhana kopatulika; musamachita ntchito ya masiku ena.
26 Momwemonso tsiku la zipatso zoyamba, pobwera nayo nsembe ya ufa watsopano kwa Yehova, m’chikondwerero chanu cha Masabata, muzikhala nako kusonkhana kopatulika; musamachita ntchito ya masiku ena.
27 Pamenepo muzipereka nsembe yopsereza ya fungo lokoma kwa Yehova; ng’ombe zamphongo ziwiri, nkhosa yamphongo imodzi, anaankhosa asanu ndi awiri a chaka chimodzi;
28 ndi nsembe yake ya efa wa ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, atatu a magawo khumi akhale a ng’ombe imodzi, awiri a magawo khumi akhale a nkhosa yamphongo imodzi,
29 limodzi la magawo khumi likhale la mwanawankhosa mmodzi, momwemo ndi anaankhosa asanu ndi awiri;
30 tonde mmodzi wakutetezera inu.
31 Mupereke izi pamodzi ndi nsembe yopsereza yosalekeza, ndi nsembe yake yaufa, zikhale kwa inu zopanda chilema, ndi nsembe zake zothira.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/28-21a6f970c777b93732f80fd6033619d1.mp3?version_id=1068—