Categories
NUMERI

NUMERI 17

Ndodo ya Aroni iphuka

1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,

2 Nena ndi ana a Israele, nulandire kwa yense ndodo, banja lililonse la makolo ndodo imodzi, mtsogoleri wa mafuko ao onse monga mwa mabanja a makolo ao azipereka ndodo, zikhale khumi ndi ziwiri; nulembe dzina la yense pa ndodo yake.

3 Ndipo ulembe dzina la Aroni pa ndodo ya Levi; pakuti pakhale ndodo imodzi pa mkulu yense wa nyumba za makolo ao.

4 Ndipo uziike m’chihema chokomanako, chakuno cha mboni, kumene ndikomana ndi inu.

5 Ndipo kudzali, kuti ndodo ya munthu ndimsankheyo, idzaphuka; ndipo ndidzadziletsera madandaulo a ana a Israele amene adandaula nao pa inu.

6 Ndipo Mose ananena ndi ana a Israele, ndipo akalonga ao onse anapereka, yense ndodo imodzi, monga mwa mabanja a makolo ao, ndodo khumi ndi ziwiri; ndi ndodo ya Aroni inakhala pakati pa ndodo zao.

7 Ndipo Mose anaika ndodozo pamaso pa Yehova m’chihema cha mboni.

8 Ndipo kunali m’mawa mwake, kuti Mose analowa m’chihema cha mboni; ndipo taonani, ndodo ya Aroni, ya pa banja la Levi, inaphuka, n’kutulutsa timaani, ndi kuchita maluwa, n’kubereka akatungurume.

9 Ndipo Mose anatulutsa ndodo zonse kuzichotsa pamaso pa Yehova, azione ana onse a Israele; ndipo anapenya, natenga yense ndodo yake.

10 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Bweza ndodo ya Aroni kuiika chakuno cha mboni, isungike ikhale chizindikiro cha pa ana opikisana; kuti unditsirizire madandaulo ao, kuti ungafe.

11 Ndipo Mose anachita monga Yehova adamuuza, momwemo anachita.

12 Pamenepo ana a Israele ananena ndi Mose, nati, Taonani, tikufa, tionongeka, tionongeka tonse.

13 Yense wakuyandikiza chihema cha Yehova amwalira; kodi tidzatha nkufa?

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/17-125ef890b3b305f0d60f69a097cacfce.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *