Categories
NUMERI

NUMERI 14

Aisraele afuna kubwerera kunka ku Ejipito

1 Pamenepo khamu lonse linakweza mau ao, nafuula; ndipo anthuwo analira usikuwo.

2 Ndipo ana onse a Israele anadandaulira Mose ndi Aroni; ndi khamu lonse linanena nao, Mwenzi tikadafa m’dziko la Ejipito; kapena mwenzi tikadafa m’chipululu muno!

3 Ndipo Yehova atitengeranji kudza nafe kudziko kuno, kuti tigwe nalo lupanga? Akazi athu ndi makanda athu adzakhala chakudya chao; kodi sikuli bwino tibwerere ku Ejipito?

4 Ndipo anati wina ndi mnzake, Tiike mtsogoleri, tibwerere ku Ejipito.

5 Pamenepo Mose ndi Aroni anagwa nkhope pansi pamaso pa msonkhano wonse wa khamu la ana a Israele.

6 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, ndi Kalebe mwana wa Yefune, ndiwo a iwo aja adazonda dzikolo, anang’amba zovala zao;

7 nanena ndi khamu lonse la ana a Israele, nati, Dziko tapitamo kulizonda, ndilo dziko lokometsetsa ndithu.

8 Yehova akakondwera nafe, adzatilowetsa m’dzikomo, ndi kutipatsa ilo; ndilo dziko moyenda mkaka ndi uchi ngati madzi.

9 Chokhachi musamapikisana naye Yehova, musamaopa anthu a m’dzikomo; pakuti ndiwo mkate wathu; mthunzi wao wawachokera, ndipo Yehova ali nafe; musamawaopa.

10 Koma khamu lonse lidati liwaponye miyala. Ndipo ulemerero wa Yehova unaoneka m’chihema chokomanakokwa ana onse a Israele.

Mose atetezera anthu kwa Mulungu

11 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Anthu awa adzaleka liti kundinyoza? Ndipo adzayamba liti kundikhulupirira, chinkana zizindikiro zonse ndinazichita pakati pao?

12 Ndidzawakantha ndi mliri, ndi kuwachotsera cholowa chao, ndipo ndidzakusandutsa iwe mtundu wa anthu waukulu ndi wamphamvu koposa iwowa.

13 Ndipo Mose anati kwa Yehova, Pamenepo Aejipito adzamva; popeza munakweza anthu awa ndi mphamvu yanu kuwachotsa pakati pao;

14 ndipo adzawauza okhala m’dziko muno; adamva kuti inu Yehova muli pakati pa anthu awa; pakuti muoneka mopenyana, Yehova ndi mtambo wanu umaima pamwamba pao, ndipo muwatsogolera, ndi mtambo njo msana, ndi moto njo usiku.

15 Ndipo mukapha anthu awa ngati munthu mmodzi, pamenepoamitunduamene adamva mbiri yanu adzanena, ndi kuti,

16 Popeza Yehova sanakhoze kuwalowetsa anthu awa m’dziko limene anawalumbirira, chifukwa chake anawapha m’chipululu.

17 Ndipo tsopano, ikuletu mphamvu ya Mbuye wanga, monga mudanena, ndi kuti,

18 Yehova ndiye wolekereza, ndi wa chifundo chochuluka, wokhululukira mphulupulu ndi kulakwa, koma wosamasula wopalamula; wakuwalanga ana chifukwa cha mphulupulu ya atate ao, kufikira mbadwo wachitatu ndi wachinai.

19 Khululukiranitu mphulupulu ya anthu awa, monga mwa chifundo chanu chachikulu, ndi monga mudalekerera anthu awa, kuyambira Ejipito kufikira tsopano.

20 Ndipo Yehova anati, Ndakhululukira monga mwa mau ako:

21 koma ndithu, pali Ine, dziko lonse lapansi lidzadzazidwa ndi ulemerero wa Yehova;

22 popeza anthu onse awa amene adaona ulemerero wanga, ndi zizindikiro zanga, ndidazichita mu Ejipito ndi m’chipululu, koma anandiyesa Ine kakhumi aka, osamvera mau anga;

23 sadzaona dzikoli ndidalumbirira makolo ao, ngakhale mmodzi wa iwo akundinyoza Ine, sadzaliona;

24 koma mtumiki wanga Kalebe, popeza anali nao mzimu wina, nanditsata monsemo, ndidzamlowetsa iyeyu m’dziko muja analowamo; ndi mbeu zake zidzakhala nalo.

25 Koma Aamaleke ndi Akanani akhala m’chigwamo; tembenukani mawa, nimunke ulendo wanu kuchipululu, njira ya ku Nyanja Yofiira.

Odandaulawo saloledwa kulowa dziko la Kanani

26 Ndipo Yehova ananena kwa Mose ndi Aroni, nati,

27 Ndileke khamu loipa ili lakudandaula pa Ine kufikira liti? Ndidamva madandaulo a ana a Israele, amene amandidandaulira.

28 Nunene nao, Pali Ine ati Yehova, ndidzachitira inu ndithu monga mwanena m’makutu mwanga;

29 mitembo yanu idzagwa m’chipululu muno; ndi owerengedwa anu onse, monga mwa kuwerenga kwani konse, kuyambira a zaka makumi awiri ndi mphambu, akudandaula pa Ine;

30 simudzalowa inu m’dzikolo, ndinakwezapo dzanja langa kukukhalitsani m’mwemo, koma Kalebe mwana wa Yefune, ndi Yoswa mwana wa Nuni ndiwo.

31 Koma makanda anu, amene munanena za iwowa kuti adzakhala chakudya, amenewo ndidzawalowetsa, ndipo adzadziwa dzikolo mudalikana.

32 Koma inu, mitembo yanu idzagwa m’chipululu muno.

33 Ndipo ana anu adzakhala oyendayenda m’chipululu zaka makumi anai, nadzasenza kupulukira kwanu, kufikira mitembo yanu yatha m’chipululu.

34 Monga mwa kuwerenga kwa masiku amene munazonda dziko, masiku makumi anai, tsiku limodzi kuwerenga chaka chimodzi, mudzasenza mphulupulu zanu, zaka makumi anai, ndipo mudzadziwa kuti ndaleka lonjezano langa.

35 Ine Yehova ndanena, ndidzachitira ndithu ichi khamu ili lonse loipa lakusonkhana kutsutsana nane; adzatha m’chipululu muno, nadzafamo.

36 Ndipo amunawo, amene Mose anawatumiza kukazonda dziko, amene anabwera nadandaulitsa khamu lonse pa iye, poipsa mbiri ya dziko,

37 amuna amene anaipsa mbiri ya dziko, anafa ndi mliri pamaso pa Yehova.

38 Koma Yoswa mwana wa Nuni, ndi Kalebe mwana wa Yefune, anakhala ndi moyo mwa amuna aja adamukawo kukazonda dziko.

39 Ndipo Mose anauza ana a Israele mau onse awa; ndipo anthu anamva chisoni chambiri.

40 Ndipo anauka mamawa, nakwera pamwamba paphiri, nati, Tili pano, tidzakwera kunka ku malo amene Yehova ananena; popeza tachimwa.

41 Ndipo Mose anati, Mutero chifukwa ninji kulakwira mau a Yehova, popeza simudzapindula nako?

42 Musakwereko, pakuti Yehova sali pakati pa inu; kuti angakukantheni adani anu.

43 Pakuti Aamaleke ndi Akanani ali komweko patsogolo panu, ndipo mudzagwa ndi lupanga; popeza mwabwerera m’mbuyo osatsata Yehova, chifukwa chake Yehova sadzakhala nanu.

44 Koma anakwera pamwamba paphiri modzikuza; koma likasa la chipangano la Yehova, ndi Mose, sanachoke kuchigono.

45 Pamenepo anatsika Aamaleke, ndi Akanani, akukhala m’phirimo nawakantha, nawapha kufikira ku Horoma.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/14-ca3ac19e86ab15a442ff559dac38bf5c.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *