Atumidwa amuna 12 kukazonda Kanani
1 Ndipo Yehova ananena ndi Mose, nati,
2 Udzitumire amuna, kuti azonde dziko la Kanani, limene ndilikupatsa ana a Israele; utumize munthu mmodzi wa fuko lililonse la makolo ao, yense kalonga pakati pa anzake.
3 Ndipo Mose anawatumiza kuchokera ku chipululu cha Parani monga mwa mau a Yehova; amuna onsewa ndiwo akulu a ana a Israele.
4 Maina ao ndi awa: wa fuko la Rubeni, Samuwa mwana wa Zakuri.
5 Wa fuko la Simeoni, Safati mwana wa Hori.
6 Wa fuko la Yuda, Kalebe mwana wa Yefune.
7 Wa fuko la Isakara, Igala mwana wa Yosefe.
8 Wa fuko la Efuremu, Hoseya mwana wa Nuni.
9 Wa fuko la Benjamini, Paliti mwana wa Rafu.
10 Wa fuko la Zebuloni, Gadiele mwana wa Sodi.
11 Wa fuko la Yosefe, wa fuko la Manase, Gadi mwana wa Susi.
12 Wa fuko la Dani, Amiyele mwana wa Gemali.
13 Wa fuko la Asere, Seturi mwana wa Mikaele.
14 Wa fuko la Nafutali, Nabi mwana wa Vofusi.
15 Wa fuko la Gadi, Geuwele mwana wa Maki.
16 Awa ndi maina a amunawo Mose anawatumira azonde dziko. Ndipo Mose anamutcha Hoseya mwana wa Nuni Yoswa.
17 Potero Mose anawatuma azonde dziko la Kanani, nanena nao, Kwerani uko kumwera, nimukwere kumapiri;
18 mukaone dziko umo liliri; ndi anthu akukhala m’mwemo, ngati ali amphamvu kapena ofooka, ngati achepa kapena achuluka;
19 ndi umo liliri dzikoli lokhalamo iwo, ngati lokoma, kapena loipa; ndi umo iliri mizindayo akhalamo iwo, ngati akhala poyera kapena m’malinga;
20 ndi umo iliri nthaka, ngati yopatsa, kapena yosuka, ngati pali mitengo, kapena palibe. Ndipo limbikani mtima, nimubwere nazo zipatso za m’dzikomo. Koma nyengoyi ndiyo nyengo yoyamba kupsa mphesa.
21 Pamenepo anakwerako, nazonda dziko kuyambira chipululu za Zini kufikira Rehobu, polowa ku Hamati.
22 Ndipo anakwera njira ya kumwera nafika ku Hebroni; ndi apa panali Ahimani, Sesai, ndi Talimai, ana a Anaki. (Koma atamanga Hebroni zaka zisanu ndi ziwiri ndipo anamanga Zowani mu Ejipito.)
23 Ndipo anadza ku chigwa cha Esikolo, nachekako tsango limodzi la mphesa, nalisenza awiri mopika; anabwera nazonso makangaza ndi nkhuyu.
24 Malowa anawatcha chigwa cha Esikolo, chifukwa cha tsangolo ana a Israele analichekako.
25 Pamenepo anabwerera atazonda dziko, atatha masiku makumi anai.
26 Ndipo anamuka, nadza kwa Mose, ndi Aroni, ndi khamu lonse la ana a Israele, ku chipululu cha Parani ku Kadesi; ndipo anabwezera mau iwowa, ndi khamu lonse, nawaonetsa zipatso za dzikoli.
27 Ndipo anafotokozera, nati Tinakafika ku dziko limene munatitumirako, ndilo ndithu moyenda mkaka ndi uchi ngati madzi; ndi zipatso zake siizi.
28 Komatu anthu okhala m’dzikomo ngamphamvu; ndi mizindayo nja malinga, yaikulu ndithu; ndipo tinaonakonso ana a Anaki.
29 Aamaleke akhala m’dziko la kumwera; ndi Ahiti, ndi Ayebusi, ndi Aamori, akhala ku mapiri, ndi Akanani akhala kunyanja, ndi m’mphepete mwa Yordani.
30 Koma Kalebe anatontholetsa anthu pamaso pa Mose, nati, Tikwere ndithu ndi kulilandira lathulathu; popeza tikhozadi kuchita kumene.
31 Koma anthu adakwera nayewo anati, Sitingathe kuwakwerera anthuwo; popeza atiposa mphamvu.
32 Ndipo anaipsira ana a Israele mbiri ya dziko adalizonda, nati, Dzikoli tapitamo kulizonda, ndilo dziko lakutheramo anthu okhalamo; ndi anthu onse tidaona pakati pake ndiwo anthu aatali misinkhu.
33 Tinaonakonso Anefili, ana a Anaki, obadwa ndi Anefili; ndipo tinaoneka m’maso mwathu ngati ziwala; momwemonso tinaoneka m’maso mwao.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/13-d620e29d0c4d84a342462225540f9556.mp3?version_id=1068—