Categories
NUMERI

NUMERI 11

Kudandaula kwa Aisraele

1 Ndipo anthu anaipa, namadandaula m’makutu a Yehova; ndipo pamene Yehova anamva anapsa mtima; ndi moto wa Yehova unayaka pakati pao, nunyeketsa ku chilekezero cha chigono.

2 Pamenepo anthu anafuulira kwa Mose; ndi Mose anapemphera kwa Yehova, ndi motowo unazima.

3 Ndipo anatcha malowo dzina lake Tabera; popeza moto wa Yehova udayaka pakati pao.

4 Ndipo anthu osokonezeka ali pakati pao anagwidwa nacho chilakolako; ndi ana a Israele omwe analiranso, nati, Adzatipatsa nyama ndani?

5 Tikumbukira nsomba tinazidya mu Ejipito chabe, minkhaka, ndi mavwende, ndi anyezi wa mitundu itatu;

6 koma tsopano moyo wathu waphwa; tilibe kanthu pamaso pathu komamanaawa.

7 Ndipo mana ananga zipatso zampasa, ndi maonekedwe ake ngati maonekedwe a bedola.

8 Anthu amanka, nawaola, nawapera ndi mphero, kapena kuwasinja mumtondo, nawaphika m’mphika, nawaumba timitanda; ndi powalawa anali ngati timitanda tokazinga ndi mafuta.

9 Ndipo pakugwa mame pachigono usiku, mana anagwapo.

Mose adandaula pa katundu wake

10 Ndipo Mose anamva anthu alikulira m’mabanja ao, yense pakhomo pa hema wake; ndipo Yehova anapsa mtima ndithu, ndipo kudamuipira Mose.

11 Ndipo Mose anati kwa Yehova, Munachitiranji choipa mtumiki wanu? Ndalekeranji kupeza ufulu pamaso panu, kuti muika pa ine katundu wa anthu awa onse?

12 Kodi ndinaima nao anthu awa onse? Kodi ndinawabala, kuti munene nane, Uwayangate ngati mlezi afukata khanda, kunka nao ku dzikolo mudalumbirira makolo ao?

13 Ndidzaiona kuti nyama yakuwapatsa anthu awa onse? Pakuti amalirira ine, ndi kuti, Tipatseni nyama, tidye.

14 Sinditha kuwasenza anthu awa onse ndekha, pakuti andilemera ine.

15 Ndipo ngati mundichitira chotero, mundiphetu tsopano apa, ngati ndapeza ufulu pamaso panu, ndisayang’ane tsoka langa.

16 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Undisonkhanitsire amuna makumi asanu ndi awiri mwa akulu a Israele, amene uwadziwa kuti ndiwo akulu a anthu, ndi akapitao ao; nubwere nao kuchihema chokomanako, kuti aimeko pamodzi ndi iwe.

17 Pamenepo ndidzatsika ndi kulankhula nawe komweko; ndipo ndidzatengako mzimu uli pa iwe, ndi kuika pa iwowa; adzakuthandiza kusenza katundu wa anthu awa, kuti usasenze wekha.

18 Ndipo unene ndi anthu, Mudzipatuliretu, mawa mudzadya nyama; popeza mwalira m’makutu a Yehova, ndi kuti, Adzatipatsa nyama ndani? Popeza tinakhala bwino mu Ejipito. Potero Yehova adzakupatsani nyama, ndipo mudzadya.

19 Simudzadya tsiku limodzi, kapena masiku awiri, kapena masiku asanu, kapena masiku khumi, kapena masiku makumi awiri;

20 koma mwezi wamphumphu, kufikira ibwera m’mphuno mwako, ndi kuti ufukidwa nayo, pakuti mwakaniza Yehova wakukhala pakati pa inu, ndi kulira pamaso pake, ndi kuti, Tinatulukiranji mu Ejipito?

21 Ndipo Mose anati, Anthu amene ndili pakati pao, ndiwo zikwi mazana asanu ndi limodzi oyenda pansi, ndipo Inu mwanena, Ndidzawapatsa nyama, kuti adye mwezi wamphumphu.

22 Kodi adzawaphera magulu a nkhosa ndi ng’ombe, kuwakwanira? Kapena kodi nsomba zonse za m’nyanja zidzawasonkhanira pamodzi, kuwakwanira?

23 Ndipo Yehova anati kwa Mose, Kodi dzanja la Mulungu lafupikira? Tsopano udzapenya ngati mau anga adzakuchitikira kapena iai.

24 Ndipo Mose anatuluka, nauza anthu mau a Yehova; nasonkhanitsa akulu a anthu makumi asanu ndi awiri, nawaimika pozungulira pa chihema.

25 Ndipo Yehova anatsika mumtambo, nanena naye, natengako mzimu uli pa iye, nauika pa akulu makumi asanu ndi awiri; ndipo kunali kuti pokhala mzimu pa iwowa, ananenera; koma osabwerezanso.

26 Koma amuna awiri anatsalira m’chigono, dzina la wina ndiye Elidadi, dzina la mnzake ndiye Medadi; ndipo mzimuwo unakhala pa iwo; iwo ndiwo mwa oitanidwawo, koma sanatuluke kunka kuchihema; ndipo ananenera m’chigono.

27 Ndipo anathamanga anyamata, nauza Mose, nati, Elidadi ndi Medadi alikunenera m’chigono.

28 Ndipo Yoswa mwana wa Nuni, mtumiki wa Mose kuyambira ubwana wake, anayankha nati, Mose, mfumu yanga, aletseni.

29 Koma Mose anati kwa iye, Kodi uchita nsanje nao chifukwa cha ine? Mwenzi anthu onse a Yehova atakhala aneneri? Mwenzi Yehova atawaikira mzimu wake!

30 Ndipo Mose ndi akulu onse a Israele anasonkhana kuchigono.

31 Ndipo kudachokera mphepo kwa Yehova, n’kudza nazo zinziri zochokera kunyanja, ndipo zidagwa kuchigono, ulendo wa tsiku limodzi dera lino, ndi ulendo wa tsiku limodzi dera lina, pozungulira pa chigono, ndipo zinabisa nthaka ngati muyeso wa mikono iwiri.

32 Ndipo anthu anauka tsiku lonselo, ndi usiku wake wonse, ndi mawa lake lonse, nakusa zinzirizo; wokusa pang’ono anakusa zodzaza mahomeri khumi; ndipo anadziyanikira izi pozungulira pa chigono.

33 Nyamayi ikali pakati pa mano, asanaitafune, Mulungu anapsa mtima pa anthuwa, ndipo Yehova anawakantha anthu ndi kukantha kwakukulu ndithu.

34 Ndipo anatcha malowo dzina lake Kibroti-Hatava; popeza pamenepo anaika anthu osusuka.

35 Kuchokera ku Kibroti-Hatava anthuwo anayenda kunka ku Hazeroti; nakhala ku Hazeroti.

—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NUM/11-12a108c7cccf4da0a1422d54689bb562.mp3?version_id=1068—

Leave a Reply

Your email address will not be published. Required fields are marked *