Maina a ansembe ndi Alevi ofika ku Yerusalemu pamodzi ndi Zerubabele
1 Ndipo ansembe ndi Alevi amene anakwera ndi Zerubabele mwana wa Sealatiele, ndi Yesuwa, ndi awa: Seraya, Yeremiya, Ezara,
2 Amariya, Maluki, Hatusi,
3 Sekaniya, Rehumu, Meremoti,
4 Ido, Ginetoyi, Abiya,
5 Miyamini, Maadiya, Biliga,
6 Semaya, ndi Yoyaribu, Yedaya.
7 Salu, Amoki, Hilikiya, Yedaya. Awa ndi akulu a ansembe ndi abale ao m’masiku a Yesuwa.
8 Ndi Alevi ndiwo Yesuwa, Binuyi, Kadimiyele, Serebiya, Yuda, ndi Mataniya; iye ndi abale ake amatsogolera mayamiko.
9 Ndi Bakibukiya ndi Uni, abale ao, anawayang’anira maulonda.
10 Ndi Yesuwa anabala Yoyakimu, ndi Yoyakimu anabala Eliyasibu ndi Eliyasibu anabala Yoyada,
11 ndi Yoyada anabala Yonatani, ndi Yonatani, anabala Yaduwa.
12 Ndi m’masiku a Yoyakimu ansembe aakulu a nyumba za makolo ndiwo: wa Seraya, Meraya; wa Yeremiya, Hananiya;
13 wa Ezara, Mesulamu; wa Amariya, Yehohanani;
14 wa Maluki, Yonatani; wa Sebaniya, Yosefe;
15 wa Harimu, Adina; wa Meraiyoti, Helikai;
16 wa Ido, Zekariya; wa Ginetoni, Mesulamu;
17 wa Abiya, Zikiri; wa Miniyamini, wa Mowadiya, Pilitai;
18 wa Biliga, Samuwa; wa Semaya, Yehonatani;
19 ndi wa Yoyaribu, Matenai; wa Yedaya, Uzi;
20 wa Salai, Kalai; wa Amoki, Eberi;
21 wa Hilikiya, Hasabiya; wa Yedaya, Netanele.
22 M’masiku a Eliyasibu, Yoyada, Yohanani, ndi Yaduwa, Alevi analembedwa akulu a nyumba za makolo; ansembe omwe, mpaka ufumu wa Dariusi wa ku Persiya.
23 Ana a Levi, akulu a nyumba za makolo, analembedwa m’buku la machitidwe, mpaka masiku a Yohanani mwana wa Eliyasibu.
24 Ndi akulu a Alevi: Hasabiya, Serebiya, ndi Yesuwa mwana wa Kadimiyele, ndi abale ao openyana nao, kulemekeza ndi kuyamika, monga mwa lamulo la Davide munthu wa Mulungu, alonda kupenyana alonda.
25 Mataniya, ndi Bakibukiya, Obadiya, Mesulamu, Talimoni, Akubu, ndiwo odikira akulonda pa nyumba za chuma zili kuzipata.
26 Awa anakhala m’masiku a Yoyakimu mwana wa Yesuwa, mwana wa Yozadaki, ndi m’masiku a Nehemiya kazembe, ndi a Ezara wansembe mlembiyo.
Kuperekedwa kwa linga la Yerusalemu
27 Ndipo popereka linga laYerusalemuanafunafuna Alevi m’malo mwao monse, kubwera nao ku Yerusalemu, kuti achite kuperekaku mokondwera, ndi mayamiko, ndi kuimbira, ndi nsanje, zisakasa, ndi azeze.
28 Ana a oimbirawo anasonkhana ochokera ku dziko lozungulira Yerusalemu, ndi kumidzi ya Anetofa,
29 ndi ku Betegiligala, ndi ku minda ya Geba ndi Azimaveti; popeza oimbirawo adadzimangira midzi pozungulira Yerusalemu.
30 Ndipo ansembe ndi Alevi anadziyeretsa okha, nayeretsa anthu, ndi zipata, ndi linga.
31 Pamenepo ndinakwera nao akulu a Yuda pa lingali, ndinaikanso oyamikira magulu awiri akulu oyenda molongosoka; lina loyenda ku dzanja lamanja palinga kunka ku Chipata cha Kudzala;
32 ndi pambuyo pao anayenda Hosaya, ndi limodzi la magawo awiri a akulu a Yuda,
33 ndi Azariya, Ezara ndi Mesulamu,
34 Yuda, ndi Benjamini, ndi Semaya, ndi Yeremiya,
35 ndi ana ena a ansembe ndi malipenga: Zekariya mwana wa Yonatani, mwana wa Semaya, mwana wa Mataniya, mwana wa Mikaya, mwana wa Zakuri, mwana wa Asafu,
36 ndi abale ake: Semaya, ndi Azarele, Milalai, Gilalai, Maai, Netanele, ndi Yuda, Hanani, ndi zoimbira za Davide munthu wa Mulungu; ndi Ezara mlembiyo anawatsogolera;
37 ndi ku Chipata cha ku Chitsime, ndi kundunji kwao, anakwerera pa makwerero a mzinda wa Davide, potundumuka linga, popitirira pa nyumba ya Davide, mpaka ku Chipata cha Madzi kum’mawa.
38 Ndi gulu lina la oyamikira linamuka mokomana nao, ndi ine ndinawatsata, pamodzi ndi limodzi la magawo awiri la anthu palinga, napitirira pa Nsanja ya Ng’anjo, mpaka kulinga lachitando;
39 ndi pamwamba pa Chipata cha Efuremu, ndi ku Chipata Chakale, ndi ku Chipata cha Nsomba, ndi Nsanja ya Hananele, ndi Nsanja ya Zana, mpaka ku Chipata cha Nkhosa; ndipo anaima ku Chipata cha Akaidi.
40 Atatero, magulu awiriwo a iwo oyamikira anaima m’nyumba ya Mulungu, ndipo ine ndi limodzi la magawo awiri a olamulira pamodzi ndi ine;
41 ndi ansembe, Eliyakimu, Maaseiya, Miniyamini, Mikaya, Eliyoenai, Zekariya, ndi Hananiya, ali nao malipenga;
42 ndi Maaseiya, ndi Semaya, ndi Eleazara, ndi Uzi, ndi Yehohanani, ndi Malikiya, ndi Elamu, ndi Ezere. Ndipo oimbira anaimbitsa Yezeraya ndiye woyang’anira wao.
43 Ndipo anaphera nsembe zambiri tsiku lija, nasekerera; pakuti Mulungu anawakondweretsa ndi chimwemwe chachikulu; ndi akazi omwe ndi ana anakondwera; ndi chikondwerero cha Yerusalemu chinamveka kutali.
Akonzanso za kupereka limodzi la magawo khumi
44 Ndipo tsiku lomwelo anaika anthu asunge zipinda za chuma, za nsembe zokweza, za zipatso zoyamba, ndi za limodzilimodzi la magawo khumi, kulonga m’mwemo, monga mwa minda ya midzi, magawo onenedwa ndi chilamulo, akhale a ansembe ndi Alevi; popeza Yuda anakondwera nao ansembe ndi Alevi akuimirirako.
45 Ndipo iwo anasunga udikiro wa Mulungu wao, ndi udikiro wa mayeretsedwe; momwemonso oimbira ndi odikira, monga mwa lamulo la Davide ndi la Solomoni mwana wake.
46 Pakuti m’masiku a Davide ndi Asafu kalelo kunali mkulu wa oimbira, ndi wa nyimbo zolemekeza ndi zoyamikira Mulungu.
47 Ndi Aisraele onse m’masiku a Zerubabele, ndi m’masiku a Nehemiya, anapereka magawo a oimbira ndi odikira, monga mudafunika tsiku ndi tsiku; nawapatulira Alevi; ndi Alevi anawapatulira ana a Aroni.
—https://api-cdn.youversionapi.com/audio-bible-youversionapi/355/32k/NEH/12-d60c071c94d49bac6f5232f0a30014b0.mp3?version_id=1068—